< UJeremiya 40 >
1 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini emva kokuthi uNebuzaradani induna yabalindi esemyekele wahamba esuka eRama, esemthethe ebotshiwe ngamaketane phakathi kwabo bonke ababethunjwe eJerusalema lakoJuda, abasiwa ekuthunjweni eBhabhiloni.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Induna yabalindi yasimthatha uJeremiya yathi kuye: INkosi, uNkulunkulu wakho, yakhuluma lokhu okubi ngalindawo.
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
3 INkosi isikulethile yakwenza njengokutsho kwayo, ngoba lonile eNkosini, kalilalelanga ilizwi layo; ngakho loludaba lwenzakele kini.
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
4 Khathesi-ke, khangela, lamuhla ngiyakukhulula kulamaketane asezandleni zakho. Uba kukuhle emehlweni akho ukuya lami eBhabhiloni, woza, ngimise ilihlo lami phezu kwakho; kodwa uba kukubi emehlweni akho ukuya lami eBhabhiloni, yekela. Bona, ilizwe lonke liphambi kwakho; lapho kukuhle kuqondile emehlweni akho ukuhamba, hamba uye khona.
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
5 Kodwa engakabuyeli, wathi: Buyela kuGedaliya, indodana kaAhikhamu, indodana kaShafani, emmisileyo inkosi yeBhabhiloni abe phezu kwemizi yakoJuda, uhlale laye phakathi kwabantu; kumbe loba kungaphi lapho kuqondile emehlweni akho ukuya khona, hamba. Ngakho induna yabalindi yasimnika umphako lesipho, yamyekela ukuthi ahambe.
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
6 Ngakho uJeremiya wafika kuGedaliya indodana kaAhikhamu eMizipa, wahlala laye phakathi kwabantu ababesele elizweni.
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
7 Kwathi zonke induna zamabutho ezazisegangeni, zona kanye lamadoda azo, besizwa ukuthi inkosi yeBhabhiloni ibekile uGedaliya indodana kaAhikhamu abe phezu kwelizwe, lokuthi inikele kuye amadodana labesifazana labantwana, lakwabangabayanga belizwe, kulabo ababengathunjelwanga eBhabhiloni,
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
8 khona beza kuGedaliya eMizipa, oIshmayeli, indodana kaNethaniya, loJohanani, loJonathani, amadodana kaKareya, loSeraya, indodana kaTanihumethi, lamadodana kaEfayi, umNetofa, loJezaniya, indodana yomMahakathi, bona lamadoda abo.
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
9 UGedaliya, indodana kaAhikhamu, indodana kaShafani, wasefunga kibo lamadoda abo, esithi: Lingesabi ukusebenzela amaKhaladiya; hlalani elizweni, liyisebenzele inkosi yeBhabhiloni; khona kuzalilungela.
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
10 Khangelani-ke, mina ngihlala eMizipa ukuma phambi kobuso bamaKhaladiya azafika kithi; kodwa lina buthani iwayini lezithelo zehlobo lamafutha, likufake ezitsheni zenu, lihlale emizini yenu eliyithetheyo.
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
11 Futhi, lapho wonke amaJuda ayekoMowabi laphakathi kwabantwana bakoAmoni leEdoma lawayekuwo wonke amazwe esezwile ukuthi inkosi yeBhabhiloni itshiyile insali yakoJuda, lokuthi yabeka phezu kwabo uGedaliya, indodana kaAhikhamu, indodana kaShafani;
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
12 wonke amaJuda asebuya esuka endaweni zonke ayexotshelwe khona, eza elizweni lakoJuda, kuGedaliya eMizipa; abutha iwayini lezithelo zehlobo, kwaba kunengi kakhulu.
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
13 UJohanani indodana kaKareya lazo zonke induna zamabutho ayesegangeni basebesiza kuGedaliya eMizipa,
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
14 bathi kuye: Uyakwazi isibili yini ukuthi uBhahalisi inkosi yabantwana bakoAmoni uthume uIshmayeli indodana kaNethaniya ukukutshaya empilweni? Kodwa uGedaliya indodana kaAhikhamu kabakholwanga.
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
15 UJohanani indodana kaKareya wasekhuluma loGedaliya ensitha eMizipa esithi: Ake ungiyekele ngihambe ngiyetshaya uIshmayeli indodana kaNethaniya, kungabi lamuntu okwaziyo. Uzakutshayelani empilweni, ukuze bahlakazeke bonke abakoJuda ababuthene kuwe, kubhubhe insali yakoJuda?
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
16 Kodwa uGedaliya indodana kaAhikhamu wathi kuJohanani indodana kaKareya: Ungayenzi le indaba, ngoba uqamba amanga ngoIshmayeli.
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”