< UJeremiya 34 >
1 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini, lapho uNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni, lebutho lakhe lonke, lemibuso yonke yomhlaba yokubusa kwesandla sakhe, lazo zonke izizwe, babesilwa bemelene leJerusalema bemelene layo yonke imizi yayo, lisithi:
Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Hamba ukhulume kuZedekhiya inkosi yakoJuda uthi kuye: Itsho njalo iNkosi: Khangela, nginikela lumuzi esandleni senkosi yeBhabhiloni, ukuthi iwutshise ngomlilo.
“Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
3 Lawe kawuyikuphunyuka esandleni sayo, kodwa uzabanjwa isibili, unikelwe esandleni sayo; lamehlo akho azabona amehlo enkosi yeBhabhiloni, lomlomo wayo uzakhuluma lomlomo wakho; njalo uzakuya eBhabhiloni.
Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
4 Kodwa zwana ilizwi leNkosi, Zedekhiya, nkosi yakoJuda: Itsho njalo iNkosi ngawe: Kawuyikufa ngenkemba.
“Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
5 Uzakufa ngokuthula, lanjengokubaselwa kwaboyihlo, amakhosi endulo, ayephambi kwakho, ngokunjalo bazakubasela, bakulilele, besithi: Maye inkosi! Ngoba mina ngilikhulumile lelolizwi, itsho iNkosi.
udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
6 UJeremiya umprofethi wasewakhuluma wonke lamazwi kuZedekhiya inkosi yakoJuda eJerusalema,
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
7 lapho ibutho lenkosi yeBhabhiloni lisilwa limelene leJerusalema limelene layo yonke imizi yakoJuda eyayisele, limelene leLakishi limelene leAzeka; ngoba yiyo imizi ebiyelweyo eyayisisele phakathi kwemizi yakoJuda.
Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
8 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini, emva kokuthi inkosi uZedekhiya esenzile isivumelwano labo bonke abantu ababeseJerusalema ukumemezela inkululeko kubo,
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
9 ukuthi ngulowo lalowo ayekele isigqili sakhe sihambe sikhululekile, langulowo lalowo isigqilikazi sakhe, umHebheru kumbe umHebherukazi, ukuze kungabi khona umuntu owenza umJuda engumfowabo abe yisigqili.
Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
10 Kwasekulalela zonke iziphathamandla labo bonke abantu ababengene lesosivumelwano sokuthi ngulowo lalowo ayekele isigqili sakhe langulowo lalowo isigqilikazi sakhe sihambe sikhululekile, bangaphindi bazenze zibe yizigqili; basebelalela, baziyekela zahamba.
Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
11 Kodwa emva kwalokho baphenduka, bazibuyisa izigqili lezigqilikazi ababeziyekele zihambe zikhululekile, bazehlisela phansi zaba yizigqili lezigqilikazi.
Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
12 Ngakho ilizwi leNkosi lafika kuJeremiya livela eNkosini, lisithi:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
13 Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Mina ngenza isivumelwano laboyihlo mhla ngibakhupha elizweni leGibhithe, endlini yobugqili, ngisithi:
“Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
14 Ekupheleni kweminyaka eyisikhombisa lizayekela ahambe, ngulowo lalowo umfowabo umHebheru owayethengiswe kuwe, esekusebenzele iminyaka eyisithupha, umyekele ahambe ekhululekile esuka kuwe. Kodwa oyihlo kabangilalelanga, kababekanga indlebe yabo.
‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
15 Lina seliphendukile lamuhla, lenza okulungileyo emehlweni ami, limemezela inkululeko, ngulowo lalowo kumakhelwane wakhe, lenza isivumelwano phambi kwami endlini ebizwa ngebizo lami.
Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
16 Kodwa liphendukile, langcolisa ibizo lami, libuyisa, ngulowo lalowo isigqili sakhe langulowo lalowo isigqilikazi sakhe, ebeliziyekele zahamba zikhululekile njengokufisa kwazo, lazehlisela phansi, zaba yizigqili lezigqilikazi zenu.
Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
17 Ngakho itsho njalo iNkosi: Lina kalingilalelanga, ukumemezela inkululeko, kube ngulowo lalowo kumfowabo langulowo lalowo kumakhelwane wakhe; khangelani, ngizamemezela kini, itsho iNkosi, inkululeko enkembeni, kumatshayabhuqe wesifo, lendlaleni; ngilinikele libe yisesabiso kuyo yonke imibuso yomhlaba.
“Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
18 Nginikele amadoda aseqileyo isivumelwano sami, angaqinisanga amazwi esivumelwano asenza phambi kwami, lapho adabula ithole kabili, adlula phakathi kweziqa zalo;
Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
19 iziphathamandla zakoJuda, leziphathamandla zeJerusalema, abathenwa, labapristi, labo bonke abantu belizwe, abadabula phakathi kweziqa zethole.
Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
20 Yebo, ngizabanikela esandleni sezitha zabo lesandleni salabo abadinga impilo yabo; lezidumbu zabo zizakuba yikudla kwenyoni zamazulu lenyamazana zomhlaba.
Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
21 LoZedekhiya inkosi yakoJuda leziphathamandla zakhe ngizabanikela esandleni sezitha zabo, lesandleni salabo abadinga impilo yabo, lesandleni sebutho lenkosi yeBhabhiloni, abenyuke basuka kini.
“Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
22 Khangelani, ngizalaya, itsho iNkosi, ngibabuyise kulumuzi; njalo bazakulwa bemelene lawo, bawuthumbe, bawutshise ngomlilo; lemizi yakoJuda ngizayenza ibe lunxiwa olungelamhlali.
Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”