< UJeremiya 33 >
1 Ilizwi leNkosi laselifika kuJeremiya ngokwesibili, esavalelwe egumeni lentolongo, lisithi:
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 Itsho njalo iNkosi, ekwenzayo, iNkosi, ekubumbayo, ukukumisa; uJehova libizo lakhe:
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Ngibiza, ngikuphendule, ngikwazise izinto ezinkulu lezifihlakeleyo elingazaziyo.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 Ngoba itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu wakoIsrayeli, ngezindlu zalumuzi langezindlu zamakhosi akoJuda, ezidilizelwe phansi ukuba ngamadundulu langenxa yenkemba:
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 Beza ukulwa lamaKhaladiya, kodwa bayazigcwalisa ngezidumbu zabantu engibatshayileyo ekuthukutheleni kwami lekufuthekeni kwami, njalo engifihle ubuso bami kulumuzi ngenxa yobubi babo bonke.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Khangela, ngizawandisela impilo enhle lokusiliswa; ngibelaphe, ngibembulele ukwanda kokuthula leqiniso.
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 Ngizabuyisa ukuthunjwa kukaJuda lokuthunjwa kukaIsrayeli, ngibakhe njengakuqala.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 Ngibahlambulule kubo bonke ububi babo abona ngabo kimi, ngithethelele zonke iziphambeko zabo abona ngazo kimi labaphambeka ngazo kimi.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 Njalo kuzakuba kimi libizo lenjabulo, kube ludumo, njalo kube yibuhle, kuzo zonke izizwe zomhlaba ezizakuzwa konke okuhle engibenzela khona; zesabe zithuthumele ngakho konke okuhle langakho konke ukuthula engibenzela khona.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Itsho njalo iNkosi: Kuzabuya kuzwakale kulindawo, elithi ngayo, ilunxiwa, engelamuntu lengelanyamazana, emizini yakoJuda lezitaladeni zeJerusalema, ezilunxiwa okungelamuntu lokungelamhlali lokungelanyamazana,
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 ilizwi lokuthaba, lelizwi lentokozo, ilizwi lomyeni, lelizwi likamakoti, ilizwi labathi: Dumisani iNkosi yamabandla, ngoba iNkosi ilungile, ngoba isihawu sayo simi kuze kube nininini; ilizwi lalabo abaletha indumiso endlini yeNkosi. Ngoba ngizabuyisa ukuthunjwa kwelizwe njengakuqala, itsho iNkosi.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Itsho njalo iNkosi yamabandla: Kule indawo elunxiwa engelamuntu kuze kube senyamazaneni, lemizini yonke yayo, kuzabuya kube khona imizi yabelusi abazakwenza imihlambi ilale kuyo.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 Emizini yentabeni, emizini yesihotsha, lemizini yeningizimu, lelizweni lakoBhenjamini, lemaphandleni eJerusalema, lemizini yakoJuda, izimvu zizabuya zedlule ngaphansi kwezandla zalowo obalayo, itsho iNkosi.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho ngizamisa ilizwi elihle engilikhulume endlini kaIsrayeli lendlini kaJuda.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 Ngalezonsuku langalesosikhathi ngizahlumisela uDavida iHlumela elilungileyo; njalo uzakwenza isahlulelo lokulunga elizweni.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 Ngalezonsuku uJuda uzasindiswa, leJerusalema ihlale ivikelekile. Njalo yileli ibizo elizabizwa ngalo: INkosi ukulunga kwethu.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 Ngoba itsho njalo iNkosi: Kakuyikuqunywa muntu kuDavida ohlala esihlalweni sobukhosi sendlu kaIsrayeli.
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 Njalo kakuyikuqunywa muntu kubapristi, amaLevi, ebusweni bami, onikela umnikelo wokutshiswa, atshise umnikelo wokudla, enze umhlatshelo insuku zonke.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 Ilizwi leNkosi laselifika kuJeremiya lisithi:
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 Itsho njalo iNkosi: Uba lingasephula isivumelwano sami semini lesivumelwano sami sobusuku, ukuze kungabi khona imini lobusuku ngesikhathi sakho,
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 khona sizakwephulwa isivumelwano sami loDavida inceku yami, ukuze angabi landodana yokubusa esihlalweni sakhe sobukhosi, lesivumelwano lamaLevi, abapristi, izikhonzi zami.
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 Njengoba ibutho lamazulu lingebalwe, letshebetshebe lolwandle lingelinganiswe, ngokunjalo ngizakwandisa inzalo kaDavida inceku yami lamaLevi angikhonzayo.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 Ilizwi leNkosi laselifika kuJeremiya lisithi:
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 Kawubonanga yini abakutshoyo lababantu besithi: Izinsapho ezimbili iNkosi ebizikhethile izilahlile? Yebo badelela abantu bami, ukuthi bangabe besaba yisizwe phambi kwabo.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 Itsho njalo iNkosi: Uba isivumelwano sami singeyisiso esemini lesebusuku, uba ngingamisanga izimiso zamazulu lezomhlaba,
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 khona ngizayala inzalo kaJakobe lekaDavida inceku yami, ukuthi kangiyikuthatha enzalweni yakhe ukuze abuse phezu kwenzalo kaAbrahama, uIsaka, loJakobe; ngoba ngizabuyisa ukuthunjwa kwabo, ngibe lesihawu kibo.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”