< UJeremiya 32 >

1 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini emnyakeni wetshumi kaZedekhiya, inkosi yakoJuda, owawungumnyaka wetshumi lesificaminwembili kaNebhukadirezari.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 Ngoba ngalesosikhathi ibutho lenkosi yeBhabhiloni layivimbezela iJerusalema; uJeremiya umprofethi wayevalelwe-ke egumeni lentolongo, elalisendlini yenkosi yakoJuda.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 Ngoba uZedekhiya inkosi yakoJuda wayemvalele esithi: Kungani wena uprofetha usithi: Itsho njalo iNkosi: Khangela, ngiwunikela lumuzi esandleni senkosi yeBhabhiloni, njalo izawuthumba;
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 loZedekhiya inkosi yakoJuda kayiyikuphunyuka esandleni samaKhaladiya, kodwa uzanikelwa isibili esandleni senkosi yeBhabhiloni, lomlomo wakhe uzakhuluma lomlomo wayo, lamehlo akhe abone amehlo ayo;
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 izakhokhela-ke uZedekhiya imuse eBhabhiloni, abe khona ngize ngimhambele, itsho iNkosi; lanxa lisilwa lamaKhaladiya, kaliyikuphumelela.
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 UJeremiya wasesithi: Ilizwi leNkosi lafika kimi lisithi:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Khangela, uHanameli indodana kaShaluma umalumakho uzafika kuwe esithi: Zithengele insimu yami eseAnathothi, ngoba nguwe olelungelo lokuhlenga ukuthi uthenge.
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 Kwasekufika kimi uHanameli indodana kamalumami, njengokutsho kweNkosi, egumeni lentolongo, wasesithi kimi: Ake uthenge insimu yami eseAnathothi eselizweni lakoBhenjamini, ngoba ulelungelo lelifa, ulohlengo; zithengele yona. Ngasengisazi ukuthi yilizwi leNkosi.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 Ngasengiyithenga insimu kuHanameli indodana kamalumami, eseAnathothi, ngamlinganisela imali engamashekeli ayisikhombisa lenhlamvu ezilitshumi zesiliva.
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 Ngasengibhala incwadi, ngayiphawula, ngenza abafakazi bafakaze, ngalinganisa imali ngesikali.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 Ngasengithatha incwadi yokuthenga enanyekiweyo njengokomthetho lezimiso, levulekileyo,
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 nganika incwadi yokuthenga kuBharukhi indodana kaNeriya, indodana kaMahaseya, phambi kwamehlo kaHanameli indodana kamalumami, laphambi kwamehlo abafakazi ababephawule incwadi yokuthenga, phambi kwamehlo awo wonke amaJuda ayehlezi egumeni lentolongo.
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 Ngasengilaya uBharukhi phambi kwamehlo abo ngisithi:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 Itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Thatha lezizincwadi, le incwadi yokuthenga, zombili enanyekiweyo lale incwadi evulekileyo, uzifake embizeni yebumba, ukuze zihlale insuku ezinengi.
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 Ngoba itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Kuzabuya kuthengwe izindlu lamasimu lezivini kulelilizwe.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Ngasengikhuleka eNkosini, senginike uBharukhi indodana kaNeriya incwadi yokuthenga, ngisithi:
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 Hawu Nkosi Jehova! Khangela, nguwe owenze amazulu lomhlaba ngamandla akho amakhulu langengalo yakho eyeluliweyo; kakuladaba olunzima kakhulu kuwe;
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 owenza uthandolomusa kwabayizinkulungwane, uphindisela isiphambeko saboyise kusifuba sabantwana babo emva kwabo; uNkulunkulu omkhulu, olamandla, iNkosi yamabandla libizo layo;
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 omkhulu ngeseluleko, lolamandla ngokwenza; ngoba amehlo akho avulekele zonke indlela zamadodana abantu, ukunika ngulowo lalowo ngokwendlela zakhe, lanjengesithelo sezenzo zakhe;
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 owamisa izibonakaliso lezimangaliso elizweni leGibhithe, kuze kube lamuhla, lakoIsrayeli laphakathi kwabantu; wasuzenzela ibizo njengalamuhla.
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 Wabakhupha abantu bakho uIsrayeli elizweni leGibhithe ngezibonakaliso, langezimangaliso, langesandla esilamandla, langengalo eyeluliweyo, langokwesabeka okukhulu;
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 wabanika lelilizwe, owafunga kuboyise ukubanika lona, ilizwe eligeleza uchago loluju.
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 Basebengena badla ilifa lalo, kodwa kabalilalelanga ilizwi lakho, kabahambanga ngomlayo wakho, kabakwenzanga konke owabalaya khona ukuthi bakwenze; ngakho ubehlisele bonke lobububi.
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Khangela amadundulu; afikile emzini ukuwuthumba, lomuzi unikelwe esandleni samaKhaladiya alwa emelene lawo; ngenxa yenkemba lendlala lomatshayabhuqe wesifo; lalokho owakukhulumayo kwenzakele; khangela-ke, uyakubona.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 Kanti, wena Nkosi Jehova, uthe kimi: Zithengele insimu ngemali, wenze abafakazi bafakaze; ngoba umuzi unikelwe esandleni samaKhaladiya.
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 Laselifika ilizwi leNkosi kuJeremiya lisithi:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 Khangela, ngiyiNkosi, uNkulunkulu wayo yonke inyama; kambe, kukhona loba yini okunzima kakhulu kimi?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Ngakho itsho njalo iNkosi: Khangela, ngiwunikela lumuzi esandleni samaKhaladiya, lesandleni sikaNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni, ozawuthumba.
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 LamaKhaladiya alwa emelene lalumuzi azangena, awuthungele lumuzi ngomlilo, awutshise kanye lezindlu obekunikelelwa phezu kwazo impepha kuBhali, lobekuthululelwa phezu kwazo iminikelo yokunathwayo kwabanye onkulunkulu, ukuze bangithukuthelise.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 Ngoba abantwana bakoIsrayeli labantwana bakoJuda bebesenza okubi kuphela emehlweni ami, kusukela ebutsheni babo; ngoba abantwana bakoIsrayeli bangizondisile kuphela ngesenzo sezandla zabo, itsho iNkosi.
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 Ngoba lumuzi ubukimi ngokolaka lwami langokwentukuthelo yami, kusukela ngosuku abawakha ngalo kuze kube lamuhla, ukuze ngiwususe ebusweni bami;
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 ngenxa yabo bonke ububi babantwana bakoIsrayeli lobabantwana bakoJuda abakwenzayo ukungithukuthelisa, bona, amakhosi abo, iziphathamandla zabo, abapristi babo, labaprofethi babo, labantu bakoJuda, labahlali beJerusalema.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 Basebengiphendulela umhlana, hatshi-ke ubuso; lanxa ngibafundisile ngivuka ngovivi ngibafundisa; kanti kabalalelanga ukwemukela ukulaywa.
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 Kodwa bamisa izinengiso zabo endlini, obizo lami libizwa kuyo, ukuze bayingcolise.
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 Basebesakha indawo eziphakemeyo zikaBhali ezisesihotsheni sendodana kaHinomu, ukuthi badabulise amadodana abo lamadodakazi abo emlilweni aye kuMoleki, engingabalayanga khona lokungafikanga enhliziyweni yami, ukuthi benze lesisinengiso, ukuze benze uJuda one.
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 Khathesi-ke, ngakho itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, mayelana lomuzi lo elithi ngawo: Unikelwe esandleni senkosi yeBhabhiloni ngenkemba langendlala langomatshayabhuqe wesifo:
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Khangelani, ngizabaqoqa bevela emazweni wonke lapho engibaxotshele khona ekuthukutheleni kwami langokufutheka kwami langolaka olukhulu; njalo ngizababuyisa kulindawo, ngibenze bahlale bevikelekile.
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 Yebo, bazakuba ngabantu bami, lami ngibe nguNkulunkulu wabo.
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 Ngizabanika inhliziyonye lendlelanye, ukuze bangesabe zonke insuku, kube kuhle kubo lakubantwana babo emva kwabo.
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 Njalo ngizakwenza labo isivumelwano esilaphakade, ukuze ngingaphenduki ekubalandeleni, ukuthi ngibenzele okuhle, ngifake ukungesaba enhliziyweni yabo, ukuze bangaphenduki basuke kimi.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 Yebo, ngizathokoza ngabo ukubenzela okuhle, ngibahlanyele ngobuqotho kulelilizwe, ngenhliziyo yami yonke langomphefumulo wami wonke.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 Ngoba itsho njalo iNkosi: Njengoba ngehlisele phezu kwalababantu bonke lobububi obukhulu, ngokunjalo ngizabehlisela konke okuhle engikukhulumileyo ngabo.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 Amasimu azathengwa-ke kulelilizwe elithi ngalo: Liyinkangala engelamuntu lenyamazana, linikelwe esandleni samaKhaladiya.
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Bazathenga amasimu ngemali, babhale izincwadi, baphawule, benze abafakazi bafakaze, elizweni lakoBhenjamini lemaphandleni eJerusalema lemizini yakoJuda lemizini yezintaba lemizini yesihotsha lemizini yeningizimu; ngoba ngizabuyisa ukuthunjwa kwabo, itsho iNkosi.
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< UJeremiya 32 >