< UJeremiya 27 >

1 Ekuqaleni kokubusa kukaJehoyakhimi indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda, kwafika lelilizwi kuJeremiya livela eNkosini, lisithi:
Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Itsho njalo iNkosi kimi: Zenzele imichilo lamajogwe, ukugaxe entanyeni yakho,
“Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
3 ukuthumele enkosini yeEdoma lenkosini yakoMowabi lenkosini yabantwana bakoAmoni lenkosini yeTire lenkosini yeSidoni, ngesandla sezithunywa ezifika eJerusalema kuZedekhiya inkosi yakoJuda;
Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
4 uzilaye ukuthi zithi emakhosini azo: Itsho njalo Nkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Lizakutsho njalo emakhosini enu:
Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
5 Mina ngenze umhlaba, umuntu, lenyamazana, okuphezu kobuso bomhlaba, ngamandla ami amakhulu langengalo yami eyeluliweyo, ngiwunike lowo okuqondileyo emehlweni ami.
Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
6 Khathesi mina sengiwanikele wonke lamazwe esandleni sikaNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni inceku yami; njalo ngimnikile lenyamazana zeganga ukuthi zimsebenzele.
Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
7 Lezizwe zonke zizasebenzela yena, lendodana yakhe, lendodana yendodana yakhe, kuze kufike isikhathi selakhe ilizwe uqobo; khona izizwe ezinengi lamakhosi amakhulu bezamkhonzisa.
Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
8 Kuzakuthi-ke isizwe lombuso okungayikumsebenzela yena, uNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni, lokungayikubeka intamo yakho ngaphansi kwejogwe lenkosi yeBhabhiloni, lesosizwe ngizasijezisa, itsho iNkosi, ngenkemba langendlala langomatshayabhuqe wesifo, ngize ngikuqede ngesandla sakhe.
“‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
9 Lina-ke lingabalaleli abaprofethi benu labavumisi benu labaphuphi benu labachasisi bemibono benu labalumbi benu abakhuluma kini besithi: Kaliyikuyisebenzela inkosi yeBhabhiloni.
Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
10 Ngoba baprofetha amanga kini, ukuze balisuse liye khatshana lelizwe lakini, lokuze ngilixotshe liphume, libhubhe.
Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
11 Kodwa isizwe esizangenisa intamo yaso ngaphansi kwejogwe lenkosi yeBhabhiloni, siyisebenzele, ngizasiyekela elizweni laso, itsho iNkosi, ukuthi silisebenze, sihlale kulo.
Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
12 Ngakhuluma lakuZedekhiya inkosi yakoJuda njengokwalawomazwi wonke ngathi: Ngenisani intamo zenu ngaphansi kwejogwe lenkosi yeBhabhiloni, lisebenzele yona labantu bayo, liphile.
Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
13 Lizafelani, wena labantu bakho, ngenkemba, ngendlala, langomatshayabhuqe wesifo, njengokutsho kweNkosi mayelana lesizwe esingayikuyisebenzela inkosi yeBhabhiloni?
Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
14 Ngakho lingawalaleli amazwi abaprofethi abakhuluma kini besithi: Kaliyikuyisebenzela inkosi yeBhabhiloni; ngoba baprofetha amanga kini.
Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
15 Ngoba kangibathumanga, itsho iNkosi, kodwa baprofetha amanga ngebizo lami, ukuze ngilixotshe, libhubhe, lina labaprofethi abaprofetha kini.
Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
16 Ngasengikhuluma kubapristi lakulababantu bonke, ngisithi: Itsho njalo INkosi: Lingawalaleli amazwi abaprofethi benu abaprofetha kini besithi: Khangelani, izitsha zendlu yeNkosi zizabuyiswa khathesi masinyane zivela eBhabhiloni; ngoba baprofetha amanga kini.
Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
17 Lingabalaleli; sebenzelani inkosi yeBhabhiloni, liphile. Kungani umuzi lo ube lunxiwa?
Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
18 Kodwa uba bengabaprofethi, njalo uba ilizwi leNkosi likubo, khathesi kabayincenge iNkosi yamabandla, ukuthi izitsha eziseleyo endlini yeNkosi lendlini yenkosi yakoJuda leJerusalema zingayi eBhabhiloni.
Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
19 Ngoba itsho njalo iNkosi yamabandla mayelana lezinsika, langolwandle, langezisekelo, langensali yezitsha ezisele kulumuzi,
Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
20 uNebhukadinezari inkosi yeBhabhiloni angazithathanga, ekuthumbeni kwakhe uJekoniya indodana kaJehoyakhimi inkosi yakoJuda eJerusalema emusa eBhabhiloni, lazo zonke izikhulu zakoJuda leJerusalema;
Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
21 yebo, itsho njalo iNkosi yamabandla uNkulunkulu kaIsrayeli mayelana lezitsha eziseleyo endlini kaJehova lendlini yenkosi yakoJuda leJerusalema:
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
22 Zizasiwa eBhabhiloni, zibe khona kuze kube lusuku engizakuzihambela ngalo, itsho iNkosi; khona ngizazenyusa, ngizibuyisele kulindawo.
‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”

< UJeremiya 27 >