< UJeremiya 2 >

1 Laselifika kimi ilizwi leNkosi lisithi:
Yehova anandiwuza kuti,
2 Hamba uyememezela endlebeni zeJerusalema usithi: Itsho njalo iNkosi: Ngiyakukhumbula, umusa wobutsha bakho, uthando lokuganwa kwakho, ukungilandela kwakho enkangala, elizweni elingahlanyelwanga.
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 UIsrayeli wayeyibungcwele eNkosini, izithelo zokuqala zesivuno sayo; bonke abamudlayo bazakuba lecala, ububi buzabehlela, itsho iNkosi.
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Zwanini ilizwi leNkosi, ndlu kaJakobe, lensendo zonke zendlu kaIsrayeli.
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 Itsho njalo iNkosi: Yibubi bani oyihlo ababuthola kimi, ukuze baye khatshana lami, balandele okuyize, babe yize?
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 Njalo kabatshongo ukuthi: Ingaphi iNkosi eyasenyusa elizweni leGibhithe, eyasikhokhela enkangala, elizweni elilamagwadule lelilemigodi, elizweni lokoma, lelethunzi lokufa, elizweni umuntu angalidabulanga, lalapho okungahlalanga muntu khona?
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 Njalo ngaliletha elizweni elivundileyo, ukuze lidle izithelo zalo lokuhle kwalo; kodwa selingenile lalingcolisa ilizwe lami, lenza ilifa lami laba yisinengiso.
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 Abapristi kabatshongo ukuthi: Ingaphi iNkosi? Lalabo abaphatha umlayo kabangazanga; lababusi baphambuka bemelene lami; labaprofethi baprofetha ngoBhali, balandela izinto ezingasiziyo.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 Ngakho ngisezaphikisana lawe, itsho iNkosi, njalo ngizaphikisana labantwana babantwana benu.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Ngoba dlulelani ezihlengeni zeKhithimi libone, lithumele eKedari, linakane kuhle, libone ukuthi kukhona into enjengale yini?
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Isizwe sake santshintsha yini onkulunkulu baso, abangeyisibo onkulunkulu? Kodwa abantu bami bantshintshile uDumo lwabo ngalokho okungasizi lutho.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Mangalani kakhulu, mazulu, ngalokhu, lethuke, lichitheke kakhulu, itsho iNkosi.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 Ngoba abantu bami benzile izinto ezimbi ezimbili; bangidelile mina mthombo wamanzi aphilayo, ukuthi bazigebhele izikhongozelo, izikhongozelo ezidabukileyo, ezingegcine manzi.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 UIsrayeli uyisigqili yini? Kumbe esizelwe ekhaya yini? Kungani waba yimpango?
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Amabhongo ezilwane abhongele phezu kwakhe, akhupha ilizwi lawo, enza ilizwe lakhe laba yincithakalo; imizi yakhe itshisiwe ingelamhlali.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Futhi abantwana beNofi leThahaphanesi badlele enkanda yakho.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 Kawuzenzelanga lokhu yini, ngokuthi udele iNkosi uNkulunkulu wakho, ngesikhathi ikukhokhela endleleni?
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 Khathesi-ke ulani lendlela yeGibhithe, ukuthi unathe amanzi eSihori? Futhi ulani lendlela yeAsiriya, ukuthi unathe amanzi omfula?
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Ububi bakho buzakulaya, lokuhlehlela kwakho nyovane kuzakukhuza. Ngakho yazi ubone ukuthi kuyinto embi lebabayo ukuthi uyidelile iNkosi uNkulunkulu wakho, lokuthi ukungesaba kakukho kuwe, itsho iNkosi uJehova wamabandla.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 Ngoba kwasendulo ngephula ijogwe lakho, ngaqamula izibopho zakho; wasusithi: Kangiyikukhonza; kodwa phezu kwalo lonke uqaqa oluphakemeyo langaphansi kwaso sonke isihlahla esiluhlaza wazulazula njengesifebe.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Kube kanti mina ngakuhlanyela, ulivini elihle, inhlanyelo ethembekileyo ngokupheleleyo. Pho, usuphenduke njani waba lugatsha olonakeleyo lwevini lemzini kimi?
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Ngoba lanxa ugeza ngesoda, uzithathele isepa enengi, kanti ububi bakho bube lichatha phambi kwami, itsho iNkosi uJehova.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 Ungatsho njani ukuthi: Kangingcolanga, kangilandelanga oBhali? Bona indlela yakho esigodini, wazi ukuthi wenzeni, kamela elisikazi elilejubane elizulazula ezindleleni zalo.
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 Ungubabhemi weganga owejwayele inkangala, ophembela umoya enkanukweni yenhliziyo yakhe. Ngubani ongamvimbela enkanukweni yakhe? Bonke abamdingayo kabayikuzidinisa; ngenyanga yakhe bazamthola.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Nqanda unyawo lwakho ekungabini ngolungelasicathulo, lomphimbo wakho ekomeni; kodwa wena wathi: Kakulathemba; hatshi; ngoba ngathanda abemzini, njalo ngizabalandela.
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Njengesela lilenhloni lapho selibanjiwe, ngokunjalo indlu kaIsrayeli ilenhloni, bona, amakhosi abo, iziphathamandla zabo, labapristi babo, labaprofethi babo,
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 besithi esigodweni: Wena ungubaba; lelitsheni: Wena wangizala. Ngoba baphendulele umhlana kimi, hatshi-ke ubuso; kodwa ngesikhathi sokuhlupheka kwabo bazakuthi: Sukuma, usisindise!
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Kodwa bangaphi onkulunkulu bakho ozenzele bona? Kabasukume uba bengakusindisa ngesikhathi sobubi bakho; ngoba njengenani lemizi yakho bangako onkulunkulu bakho, Juda.
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 Liphikisanelani lami? Lonke liphambekile kimi, itsho iNkosi.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 Ngibatshayile abantwana benu ngeze; kabemukelanga ukuqondiswa; inkemba yenu ibadlile abaprofethi benu, njengesilwane esichithayo.
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 Wena sizukulwana, lina bonani ilizwi leNkosi. Bengiyinkangala yini kuIsrayeli? Kumbe ilizwe lobumnyama obunzima yini? Batsholoni abantu bami ukuthi: Sizulazulile; kasisayikuza kuwe?
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Intombi ingazikhohlwa yini iziceciso zayo, kumbe umakoti amabhanti akhe? Kanti abantu bami bangikhohliwe insuku ezingelanani.
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 Kungani ulungisa indlela yakho ekudingeni uthando? Ngakho ubafundisile labo ababi izindlela zakho.
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Lezigqokweni zakho kutholakala igazi lemiphefumulo yabayanga abangelacala; kawubatholanga befohlela phakathi, kodwa phezu kwakho konke lokhu.
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 Kanti wena uthi: Ngoba kangilacala, isibili intukuthelo yakhe izaphenduka isuke kimi. Khangela, ngizakwehlulelana lawe, ngoba uthi: Kangonanga.
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Kungani uzulazula kangaka ukuntshintsha indlela yakho? Uzayangiswa yiGibhithe layo, njengoba wayangiswa yiAsiriya.
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Yebo, uzaphuma usuka lapha, lezandla zakho ziphezu kwekhanda lakho, ngoba iNkosi iwalile amathemba akho, njalo kawuyikuphumelela ngawo.
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.

< UJeremiya 2 >