< UJeremiya 18 >
1 Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini lisithi:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Sukuma, wehlele endlini yombumbi, lapho-ke ngizakuzwisa amazwi ami.
“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
3 Ngasengisehlela endlini yombumbi, khangela-ke wayesenza umsebenzi emavilini.
Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
4 Njalo imbiza ayeyenza ngebumba yonakala esandleni sombumbi; wasebuya wenza ngayo enye imbiza njengoba kwakuqondile emehlweni ombumbi ukwenza.
Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
5 Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
6 Ndlu kaIsrayeli, ngingeze ngenza kini njengalo umbumbi yini? itsho iNkosi. Khangela, njengebumba esandleni sombumbi, linjalo lina esandleni sami, lina ndlu kaIsrayeli.
“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
7 Ngesikhatshana ngizakhuluma ngesizwe langombuso ukuthi ngizakusiphuna, ngikudilize, ngikuchithe;
Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
8 uba lesosizwe engikhulume ngimelene laso siphenduka ebubini baso, ngizazisola ngokubi ebengicabanga ukuthi ngizakwenza kiso.
ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
9 Langesikhatshana ngizakhuluma ngesizwe langombuso, ukwakha lokukuhlanyela;
Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
10 uba kusenza okubi emehlweni ami, kungalaleli ilizwi lami, khona ngizazisola ngokuhle ebengisithi ngizakwenzela okuhle ngakho.
Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
11 Ngakho khathesi ake ukhulume ebantwini bakoJuda lakubahlali beJerusalema, usithi: Itsho njalo iNkosi: Khangelani, ngilibumbela okubi, ngilicebela icebo. Phendukani khathesi, ngulowo lalowo endleleni yakhe embi, lenze indlela zenu lezenzo zenu zibe zinhle.
“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
12 Kodwa bathi: Kakulathemba; kodwa sizalandela awethu amacebo, senze, ngulowo lalowo inkani yenhliziyo yakhe embi.
Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
13 Ngakho itsho njalo iNkosi: Buzani khathesi phakathi kwabahedeni, ngubani owake wezwa izinto ezinje? Intombi emsulwa yakoIsrayeli yenzile into eyesabekayo kakhulu.
Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
14 Umuntu angatshiya yini iliqhwa elikhithikileyo leLebhanoni elivela edwaleni leganga? Angatshiywa yini amanzi aqandayo ageleza evela kwezinye indawo?
Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Kodwa abantu bami bangikhohliwe, batshisela okuyize impepha, babenza bakhubeka ezindleleni zabo, emikhondweni yasendulo, ukuthi bahambe ezindledlaneni, endleleni engabuthelelwanga;
Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
16 besenza ilizwe labo libe lunxiwa, ukuncifelwa njalonjalo; wonke owedlula khona uzamangala kakhulu, anikine ikhanda lakhe.
Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Ngizabahlakaza njengomoya wempumalanga phambi kwesitha; ngizabatshengisa umhlana, hatshi ubuso, ngosuku lwengozi yabo.
Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
18 Basebesithi: Wozani simcebele amacebo uJeremiya; ngoba umthetho kawuyikuphela kumpristi, lokweluleka kohlakaniphileyo, lelizwi kumprofethi. Wozani simtshaye ngolimi, singananzi lawaphi amazwi akhe.
Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
19 Nginakekela, Nkosi, ulalele ilizwi labaphikisana lami.
Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Kuyavuzwa okubi esikhundleni sokuhle yini? Ngoba bagebhele umphefumulo wami umgodi. Khumbula ukuthi ngema phambi kwakho ukubakhulumela okuhle, ukuphambula ulaka lwakho kibo.
Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 Ngakho nikela abantwana babo endlaleni, ubanikele emandleni enkemba; labafazi babo balahlekelwe ngabantwana, babe ngabafelokazi, lamadoda abo abulawe yikufa, amajaha abo atshaywe ngenkemba empini.
Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Kakuzwakale ukukhala endlini zabo, lapho uzahle ulethe iviyo phezu kwabo; ngoba begebhe umgodi ukungibamba, bafihlela inyawo zami imijibila.
Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 Kanti wena, Nkosi, uyawazi wonke amacebo abo bemelene lami ukungibulala. Ungathetheleli isiphambeko sabo, lesono sabo ungasicitshi sisuke phambi kwakho; kodwa kabawiswe phambi kwakho, bana lokwenza labo ngesikhathi sokuthukuthela kwakho.
Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”