< U-Isaya 65 >
1 Ngadingwa yilabo abangangicelanga; ngatholwa yilabo abangangidinganga. Ngathi: Ngikhangelani, ngikhangelani, esizweni esingabizwa ngebizo lami.
“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2 Ngelule izandla zami usuku lonke ebantwini abavukelayo, abahamba ngendlela engalunganga, belandela imicabango yabo;
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
3 abantu abangithukuthelisayo njalonjalo ebusweni bami, abenza imihlatshelo ezivandeni, betshisa impepha phezu kwezitina;
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4 abahlala emangcwabeni, balale endaweni ezisithekileyo, abadla inyama yengulube, lomhluzi wezinto ezinengekayo emiganwini yabo.
Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5 Abathi: Xeka wena, ungasondeli kimi; ngoba ngingcwele kulawe. Laba bayintuthu emakhaleni ami, umlilo otshisayo usuku lonke.
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6 Khangela, kubhaliwe phambi kwami: Kangiyikuthula, kodwa ngizaphindisela, yebo ngiphindisele esifubeni sabo,
“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
7 iziphambeko zenu, leziphambeko zaboyihlo kanyekanye, itsho iNkosi, abatshise impepha phezu kwezintaba, bangithuka phezu kwamaqaqa; ngakho ngizalinganisa imisebenzi yabo yakuqala esifubeni sabo.
ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
8 Itsho njalo iNkosi: Njengewayini elitsha litholwa ehlukuzweni, lomunye athi: Ungalibhubhisi, ngoba isibusiso sikulo; ngizakwenza njalo ngenxa yenceku zami, ukuze ngingazibhubhisi zonke.
Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
9 Njalo ngizaveza inzalo ivela kuJakobe, lakoJuda kuvele indlalifa yezintaba zami; labakhethiweyo bami bazakudla ilifa lazo, lenceku zami zihlale khona.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Njalo iSharoni izakuba yisibaya semihlambi, lesihotsha seAkori sibe yindawo yokulala yenkomo, eyabantu bami abangidingayo.
Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11 Kodwa lina elidela iNkosi, elikhohlwa intaba yami engcwele, elihlelele leloviyo itafula, njalo eligcwalisele lelonani umnikelo wokunathwayo.
“Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 Ngakho ngizalimisela inkemba, njalo lonke lizakhothamela ukuhlatshwa; ngoba ngalibiza, kodwa kaliphendulanga, ngakhuluma, kodwa kalizwanga, kodwa lenza okubi emehlweni ami, lakhetha lokho engingathokozanga ngakho.
ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13 Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, izinceku zami zizakudla, kodwa lina lizalamba; khangela, inceku zami zizanatha, kodwa lina lizakoma; khangela, inceku zami zizathokoza, kodwa lina lizayangeka;
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 khangela, inceku zami zizahlabela ngentokozo yenhliziyo, kodwa lina lizakhala ngenxa yokudabuka kwenhliziyo, liqhinqe isililo ngenxa yokudabuka komoya.
Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Njalo lizatshiya ibizo lenu libe yisiqalekiso kwabakhethiweyo bami, ngoba iNkosi uJehova izalibulala; kodwa izabiza inceku zayo ngelinye ibizo;
Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 ukuthi lowo ozibusisa emhlabeni uzazibusisa kuNkulunkulu weqiniso, lalowo ofunga emhlabeni uzafunga ngoNkulunkulu weqiniso; ngoba inhlupheko zakuqala sezikhohlakele, njalo ngoba zisithekile emehlweni ami.
Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
17 Ngoba khangela, ngidala amazulu amatsha lomhlaba omutsha; okwakuqala kakusayikukhunjulwa, kumbe kuvele enhliziyweni.
“Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
18 Kodwa jabulani, lithokoze kuze kube laphakade ngengikudalayo, ngoba khangela, ngidala iJerusalema ibe yintokozo, labantu bayo babe yinjabulo.
Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Ngizathokoza-ke ngeJerusalema, ngijabule ngabantu bami; njalo kalisayikuzwakala kuyo ilizwi lokulila lelizwi lokukhala.
Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
20 Kusukela lapho kakusayikuba khona usane lwezinsuku, kumbe ixhegu elingagcwalisi insuku zalo; ngoba omutsha uzakufa eleminyaka elikhulu, kodwa isoni esileminyaka elikhulu sizaqalekiswa.
“Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
21 Njalo bazakwakha izindlu, bahlale kuzo; bahlanyele izivini, badle izithelo zazo.
Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 Kabayikwakha, kuhlale-ke omunye; kabayikuhlanyela, kudle-ke omunye; ngoba insuku zabantu bami zizakuba njengensuku zesihlahla, labakhethwa bami bazakholisa umsebenzi wezandla zabo okwesikhathi eside.
Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
23 Kabayikutshikatshikela ize, loba bazalele uhlupho; ngoba bayinzalo yababusisiweyo beNkosi, lembewu yabo kanye labo.
Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Kuzakuthi-ke bengakabizi, mina ngiphendule; lapho besakhuluma, mina-ke ngizwe.
Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 Impisi lewundlu kuzakudla ndawonye, lesilwane sidle amahlanga njengenkomo, lothuli lube yikudla kwenyoka. Kaziyikulimaza kumbe zibhubhise kuyo yonke intaba yami engcwele, itsho iNkosi.
Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.