< U-Isaya 63 >

1 Ngubani lo ovela eEdoma, olezembatho ezibomvu evela eBhozira? Lo odumisekileyo ngezembatho zakhe, ehamba ngobukhulu bamandla akhe? Yimi engikhuluma ngokulunga, engilamandla okusindisa.
Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Kungani izigqoko zakho zibomvu, lezembatho zakho zinjengezonyathela esikhamelweni sewayini?
Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
3 Ngisinyathele ngedwa isikhamelo sewayini, lebantwini kwakungekho loyedwa lami; ngoba ngizabanyathela ekuthukutheleni kwami, ngibahlifize elakeni lwami; legazi labo lizafafazwa ezembathweni zami, ngingcolise izigqoko zami zonke.
“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Ngoba usuku lwempindiselo lusenhliziyweni yami, lomnyaka wabahlengwa bami usufikile.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Njalo ngakhangela, kodwa kwakungekho osizayo, ngamangala kakhulu ukuthi kwakungekho osekelayo; ngakho ingalo yami yaletha usindiso kimi, lolaka lwami lona lwangisekela.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 Besenginyathela abantu ekuthukutheleni kwami, ngibadakise olakeni lwami, ngehlisele emhlabathini amandla abo.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
7 Ngizakhumbuza ngothandolomusa omkhulu weNkosi, izindumiso zeNkosi, njengakho konke iNkosi esinike khona, lobuhle obukhulu ngasendlini kaIsrayeli, ebanike bona ngokwezisa zayo, lanjengobunengi bothandolomusa wayo omkhulu.
Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
8 Ngoba yathi: Isibili bangabantu bami, abantwana abangayikukhuluma amanga; ngakho yaba nguMsindisi wabo.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
9 Enhluphekweni yabo yonke yahlupheka, lengilosi yobukhona bayo yabasindisa; ngothando lwayo langesihawu sayo yona yabahlenga, yabaphakamisa, yabathwala zonke izinsuku zendulo.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
10 Kodwa bona baba lenkani, badabukisa uMoya wayo oNgcwele; ngakho yaphenduka yaba yisitha sabo, yona yalwa imelene labo.
Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Yasikhumbula insuku zendulo, uMozisi, labantu bakhe, isithi: Ungaphi lowo owabakhuphula olwandle labelusi bomhlambi wakhe? Ungaphi lowo owafaka uMoya wakhe oyiNgcwele phakathi kwakhe?
Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Owakhokhela ingalo yakhe elodumo esandleni sokunene sikaMozisi, esehlukanisa amanzi phambi kwabo, ukuzenzela ibizo eliphakade?
Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 Owabakhokhela ezinzikini, njengebhiza enkangala kabakhubekanga?
amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
14 Njengenkomo isehlela esigodini, uMoya weNkosi wabaphumuza. Ngokunjalo wabakhokhela abantu bakho, ukuze uzenzele ibizo elilodumo.
Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Khangela phansi usemazulwini, ubone usendaweni yakho yokuhlala yobungcwele bakho leyodumo lwakho. Kungaphi ukutshiseka kwakho lamandla akho? Ubunengi bemibilini yakho, lezihawu zakho kimi, kuyazibamba yini?
Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Isibili wena ungubaba; lanxa uAbrahama engasazi, loIsrayeli engasivumi; wena Nkosi ungubaba wethu, umhlengi wethu; ibizo lakho lisukela ephakadeni.
Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Nkosi, kungani usenza siduhe ezindleleni zakho, usenza inhliziyo yethu ibe lukhuni sisuka ekukwesabeni? Phenduka ngenxa yenceku zakho, izizwe zelifa lakho.
Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Abantu bobungcwele bakho babe lakho okwesikhatshana; izitha zethu zinyathelele phansi indlu yakho engcwele.
Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Singabakho; kawuzange ubuse phezu kwabo; kababizwanga ngebizo lakho.
Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

< U-Isaya 63 >