< U-Isaya 6 >
1 Ngomnyaka wokufa kwenkosi uUziya ngabona iNkosi ihlezi esihlalweni sobukhosi esiphezulu lesiphakemeyo, lemiphetho yesembatho sayo yagcwalisa ithempeli.
Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
2 Amaserafi ayemi ngaphezu kwayo; impiko eziyisithupha, impiko eziyisithupha zalelo lalelo; ngezimbili lagubuzela ubuso balo, langezimbili lagubuzela inyawo zalo, langezimbili laphapha.
Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
3 Lelinye lamemeza kwelinye lathi: Ingcwele, ingcwele, ingcwele iNkosi yamabandla; umhlaba wonke ugcwele inkazimulo yayo.
Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
4 Insika zomnyango zasezinyikinyeka ngenxa yelizwi lomemezayo, lendlu yagcwala intuthu.
Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
5 Ngasengisithi: Maye kimi, ngoba ngiyabhubha! Ngoba ngingumuntu wendebe ezingcolileyo, futhi ngihlala phakathi kwabantu bendebe ezingcolileyo; ngoba amehlo ami abonile iNkosi, uJehova wamabandla.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
6 Kwasekuphaphela kimi elinye lamaserafi lilelahle elivuthayo esandleni salo elalilithethe ngodlawu elathini.
Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
7 Lathinta umlomo wami, lathi: Khangela, lokhu kuzithintile indebe zakho; ngakho ububi bakho bususiwe, lesono sakho senzelwe inhlawulo lokuthula.
Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
8 Ngasengisizwa ilizwi leNkosi lisithi: Ngizathuma bani? Njalo ngubani ozasiyela? Ngasengisithi: Khangela, ngilapha, thuma mina.
Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
9 Yasisithi: Hamba, uthi kulababantu: Zwanini lizwe, kodwa kaliyikuqedisisa; njalo bonani libone, kodwa kaliyikubonisisa.
Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Yenza inhliziyo yalababantu ikhuluphale, wenze indlebe zabo zibe nzima, uvale amehlo abo, hlezi babone ngamehlo abo, bezwe ngendlebe zabo, baqedisise ngenhliziyo zabo, baphenduke, babesebesiliswa.
Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
11 Ngasengisithi: Koze kube nini, Nkosi? Yasisithi: Kuze kuchitheke imizi ingabi lamhlali, lezindlu zingabi lamuntu, lelizwe lichitheke lithi nya,
Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 leNkosi ibasusele khatshana abantu, njalo kube lokutshiywa okukhulu phakathi kwelizwe.
mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 Kodwa ingxenye eyodwa etshumini isezakuba kulo; izaphenduka, ibe ngeyokudliwa; njengomtherebhinti lanjengesihlahla se-okhi, esiwohloza amahlamvu aso, isidindi saso sikuzo; inzalo engcwele iyisidindi salo.
Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”