< U-Isaya 45 >

1 Itsho njalo iNkosi kogcotshiweyo wayo, kuKoresi, osandla sakhe sokunene ngisibambile ukuze ngehlisele phansi izizwe phambi kwakhe; ngithukulule izinkalo zamakhosi, ukuvula phambi kwakhe amasango alezivalo ezimbili, lamasango angavalwa.
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Mina ngizahamba phambi kwakho, ngenze indawo ezigobileyo ziqonde, ngiphahlaze izivalo zethusi, ngiqume phakathi imigoqo yensimbi.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Ngizakunika okuligugu kobumnyama, lenotho ethukuziweyo yezindawo ezisithekileyo, ukuze wazi ukuthi mina Nkosi, engikubiza ngebizo lakho, nginguNkulunkulu kaIsrayeli.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 Ngenxa yenceku yami uJakobe, loIsrayeli umkhethwa wami, ngikubizile ngitsho ngebizo lakho, ngakunika isibongo, lanxa ungangazanga.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 NgiyiNkosi, njalo kakho omunye, ngaphandle kwami kakulaNkulunkulu; ngikubhincisile lanxa ungangazanga.
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 Ukuze bazi kusukela lapho eliphuma khona ilanga, njalo kusukela entshonalanga, ukuthi kakho omunye ngaphandle kwami; ngiyiNkosi, njalo kakho omunye.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Ngibumba ukukhanya, ngidale umnyama; ngenza ukuthula, ngidale ububi; mina Nkosi ngenza zonke lezizinto.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Thontisani, mazulu, kuvela phezulu, lamayezi athulule ukulunga; umhlaba kawuvuleke, njalo kuthele usindiso, njalo kakuthi ukulunga kumile kanyekanye; mina Nkosi ngikudalile.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Maye kuye ophikisana loMbumbi wakhe, udengezi lezindengezi zomhlabathi! Ibumba lizakutsho yini kolibumbayo ukuthi: Wenzani? kumbe: Umsebenzi wakho, kawulazandla yini?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Maye kuye othi kuyise: Uzalani? kumbe kowesifazana: Ubeletheni?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Itsho njalo iNkosi, oNgcwele kaIsrayeli, loMbumbi wakhe: Buzani kimi ngezinto ezizayo, ngamadodana ami, langomsebenzi wezandla zami liyangilaya.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Mina ngiwenzile umhlaba, ngadala umuntu phezu kwawo; mina, izandla zami zendlale amazulu, ngalawula amabutho awo wonke.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Mina ngimvusile ngokulunga, njalo ngizaqondisa zonke izindlela zakhe; yena uzakwakha umuzi wami, akhulule abathunjiweyo bami, hatshi ngentengo njalo hatshi ngesivalamlomo, kutsho iNkosi yamabandla.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Itsho njalo iNkosi: Umsebenzi weGibhithe, lokuthengiswayo kweEthiyophiya lokwamaShebha, amadoda amade, kuzadlulela kuwe, kuzakuba ngokwakho; bazakulandela, bedlule besemaketaneni, bakhothame kuwe, balabhele kuwe besithi: Isibili uNkulunkulu ukuwe, njalo kakho omunye, kakho omunye uNkulunkulu.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Isibili unguNkulunkulu ozifihlayo, uNkulunkulu wakoIsrayeli, uMsindisi.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Bazayangeka, ngitsho babe lenhloni, bonke; bazahamba belehlazo kanyekanye ababazi bezithombe.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Kodwa uIsrayeli uzasindiswa eNkosini ngosindiso olulaphakade; kaliyikuyangeka, kaliyikuba lenhloni, kuze kube nini lanini.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Ngoba itsho njalo iNkosi eyadala amazulu, yona enguNkulunkulu, eyabumba umhlaba yawenza; yona yawumisa, ingawudalelanga ize, yawubumbela ukuze kuhlalwe kuwo: NgiyiNkosi, njalo kakho omunye.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Kangikhulumelanga ekusithekeni, endaweni emnyama yomhlaba; kangitshongo kuyo inzalo kaJakobe ukuthi: Ngidingani ngeze. Mina Nkosi ngikhuluma iqiniso, ngimemezela izinto eziqotho.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Buthanani libuye; sondelani kanyekanye, lina elaphunyuka ezizweni; abathwala izigodo zezithombe zabo ezibaziweyo kabazi, abakhuleka kunkulunkulu ongelakusindisa.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Tshelani, libasondeze; yebo kabacebisane kanyekanye: Ngubani owazwakalisa lokhu kwasendulo? Owakukhulumayo kusukela kulesosikhathi na? Kakusimi iNkosi yini? Njalo kakho omunye uNkulunkulu ngaphandle kwami, uNkulunkulu olungileyo loMsindisi; kakho ngaphandle kwami.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Khangelani kimi, lisindiswe, lina lonke mikhawulo yomhlaba; ngoba nginguNkulunkulu, njalo kakho omunye.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Ngizifungile mina, ilizwi liphumile emlonyeni wami ngokulunga, njalo kaliyikuphenduka, elithi: Kimi lonke idolo lizaguqa, lonke ulimi luzafunga.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Ngeqiniso, omunye uzakuthi: ENkosini ngilokulunga lamandla; kuyo bazakuza; kodwa bonke abayithukuthelelayo bazayangeka.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 ENkosini yonke inzalo yakoIsrayeli izalungisiswa, izincome.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< U-Isaya 45 >