< U-Isaya 44 >

1 Kodwa khathesi zwana, Jakobe nceku yami, lawe Israyeli engikukhethileyo.
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Itsho njalo INkosi umenzi wakho lombumbi wakho kusukela esiswini, ezakusiza: Ungesabi, Jakobe, nceku yami, lawe Jeshuruni engikukhethileyo.
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 Ngoba ngizathela amanzi phezu kwakhe owomileyo, lezikhukhula emhlabathini owomileyo; ngizathela umoya wami phezu kwenzalo yakho, lesibusiso sami phezu kwembewu yakho.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 Bazahluma phakathi kotshani, njengeminyezane ngasezifuleni zamanzi.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 Omunye uzakuthi: Mina ngingoweNkosi; lomunye azibize ngebizo likaJakobe, lomunye abhale esandleni sakhe ukuthi: NgingoweNkosi; azibonge ngebizo likaIsrayeli.
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 Utsho njalo uJehova, inkosi yakoIsrayeli, loMhlengi wakhe, iNkosi yamabandla: Ngingowokuqala njalo ngingowokucina; njalo ngaphandle kwami kakho uNkulunkulu.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Njalo ngubani ongabiza njengami, akumemezele, angihlelele khona, kusukela ngimisa abantu bendulo? Lezinto ezizayo, lezizakuza, kabazimemezele kubo.
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Lingatshaywa luvalo, lingesabi; kangikuzwisanga yini kusukela ngalesosikhathi, ngakumemezela? Njalo lina lingabafakazi bami. Kukhona yini uNkulunkulu ngaphandle kwami? Yebo, kalikho elinye iDwala; kangilazi.
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 Bonke ababumba izithombe ezibaziweyo bayize, lezinto zabo ezithandekayo kazisizi lutho; labo bangabafakazi babo, kababoni, kabazi; ukuze bayangeke.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Ngubani obumbe unkulunkulu, loba wabumba ngokuncibilikisa isithombe esibaziweyo esingasizi lutho?
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Khangela, bonke abangane bakhe bazayangeka; lababazi bangababantu; kababuthane bonke, basukume; bazakwesaba, bayangeke kanyekanye.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Umkhandi wensimbiukhanda ihloka, asebenze emalahleni, alibumbe ngezando, alisebenze ngamandla engalo yakhe; yebo, alambe, aze aphele amandla; kanathi manzi, aze adinwe.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Umbazi welula intambo yokulinganisa, adwebe ngosungulo, asenze ngezancele, asidwebe ngekhampasi, asenze ngomfanekiso womuntu, ngokobuhle bomuntu, ukuze sihlale endlini.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 Uzigamulela imisedari, athathe umsayiphuresi lesihlahla se-okhi, aziqinisela zona phakathi kwezihlahla zegusu, ahlanyele ifiri, lezulu liyikhulise.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Kuzakuba-ke ngokomuntu ukuthi akubase, njalo uzathatha kukho, othe; yebo akubase, abhake isinkwa; yebo enze unkulunkulu, amkhonze, enze isithombe esibaziweyo, akhothame kuso.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Atshise ingxenye yakho emlilweni; ngengxenye yakho adle inyama, ose amawoso asuthe; yebo, uyotha athi: Alala! ngiyakhudumala, ngiwubonile umlilo.
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Njalo okuseleyo kwakho akwenze kube ngunkulunkulu, kube yisithombe sakhe esibaziweyo; akhothame kuso, akhonze, akhuleke kuso athi: Ngophula, ngoba ungunkulunkulu wami.
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Kabazanga, kabaqedisisanga; ngoba ebhade amehlo abo ukuze bangaboni; lenhliziyo zabo ukuze bangaqedisisi.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Kakho ocabanga enhliziyweni yakhe, njalo kakulalwazi njalo kakulakuqedisisa kokuthi: Ngibasile ingxenye yakho emlilweni, yebo ngibhake isinkwa phezu kwamalahle akho, ngosa inyama, ngayidla; kambe ngizakwenza insali yakho isinengiso yini? Ngizakhothamela okwesihlahla yini?
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Udla umlotha; inhliziyo ekhohlisiweyo imphambule, okokuthi angekhulule umphefumulo wakhe njalo kathi: Kakulamanga yini esandleni sami sokunene?
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 Khumbula lezizinto, Jakobe, lawe Israyeli, ngoba uyinceku yami; ngikubumbile, uyinceku yami. Wena Israyeli, kawuyikukhohlwa yimi.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 Ngesule iziphambeko zakho njengeyezi elinzima, lanjengeyezi izono zakho; buyela kimi, ngoba ngikuhlengile.
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 Hlabelelani, lina mazulu, ngoba iNkosi ikwenzile; memezani, zindawo eziphansi zomhlaba; qhamukani lihlabele, zintaba, gusu, laso sonke isihlahla esiphakathi kwakho; ngoba iNkosi imhlengile uJakobe, yazidumisa koIsrayeli.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Itsho njalo iNkosi, uMhlengi wakho, leyakubumba kwasesiswini: NgiyiNkosi eyenza zonke izinto; eyendlala amazulu, mina ngedwa; eyeneka umhlaba ngokwami;
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 efubisa izibonakaliso zabaqambimanga; yenze izanuse zihlanye; ebuyisela emuva abahlakaniphileyo; yenze ulwazi lwabo lube yibuthutha;
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 eqinisa ilizwi lenceku yayo; ifeze amacebo ezithunywa zayo; ethi kuyo iJerusalema: Uzahlalwa; lemizini yakoJuda: Lizakwakhiwa; futhi ngizavusa amanxiwa ayo;
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 etshoyo enzikini: Tshana; njalo ngizakomisa imifula yakho;
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 etshoyo ngoKoresi: Ungumelusi wami, uzaphelelisa intokozo yami yonke; ithi lakuJerusalema: Kayakhiwe; lethempelini: Isisekelo sakho kasibekwe.
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”

< U-Isaya 44 >