< U-Isaya 37 >
1 Kwasekusithi inkosi uHezekhiya isikuzwile, yadabula izigqoko zayo, yazembesa ngesaka, yangena endlini yeNkosi.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Yasithuma uEliyakhimi umphathi wendlu, loShebina umabhalane, labadala babapristi bembethe amasaka, kuIsaya umprofethi indodana kaAmozi.
Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Basebesithi kuye: Utsho njalo uHezekhiya: Lolusuku lusuku lohlupho lolokusolwa lolokweyiswa, ngoba abantwana sebefikile emlonyeni wesizalo, kanti akulamandla okubeletha.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
4 Mhlawumbe iNkosi, uNkulunkulu wakho, izawezwa amazwi kaRabi-Shake, onkosi yeAsiriya, inkosi yakhe, emthume ukuthuka uNkulunkulu ophilayo, lokusola ngamazwi iNkosi uNkulunkulu wakho ewazwileyo. Ngakho phakamisa umkhuleko ngensali etholakeleyo.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
5 Ngakho inceku zenkosi uHezekhiya zafika kuIsaya.
Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 UIsaya wasesithi kuzo: Lizakutsho njalo enkosini yenu: Itsho njalo iNkosi: Ungesabi amazwi owezwileyo, inceku zenkosi yeAsiriya ezingithuke ngawo.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Khangela, ngizafaka umoya kuyo, njalo izakuzwa ihungahunga, ibuyele elizweni layo; njalo ngizayenza ukuthi iwe ngenkemba elizweni layo.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 URabi-Shake wasebuyela, wafica inkosi yeAsiriya isilwa imelene leLibhina; ngoba wayezwile ukuthi isisukile eLakishi.
Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Wasesizwa ngoTirihaka inkosi yeEthiyophiya kuthiwa: Uphumile ukuzakulwa lawe. Esekuzwile wathuma izithunywa kuHezekhiya esithi:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 Lizakhuluma kanje kuHezekhiya inkosi yakoJuda lithi: UNkulunkulu wakho othembele kuye kangakukhohlisi esithi: IJerusalema kayiyikunikelwa esandleni senkosi yeAsiriya.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Khangela, wena usuzwile ukuthi amakhosi eAsiriya enzeni kuwo wonke amazwe ngokuwatshabalalisa. Wena-ke uzakhululwa yini?
Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
12 Onkulunkulu bezizwe bazikhulula yini obaba abazichithayo, iGozani leHarani leRezefi, labantwana beEdeni ababeseTelasari?
Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
13 Ingaphi inkosi yeHamathi, lenkosi yeArpadi, lenkosi yomuzi weSefavayimi, iHena, leIva?
Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
14 UHezekhiya wasesemukela izincwadi esandleni sezithunywa, wazifunda, wenyukela endlini yeNkosi; uHezekhiya wasezichaya phambi kweNkosi.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 UHezekhiya wasekhuleka eNkosini, esithi:
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
16 Nkosi yamabandla, Nkulunkulu kaIsrayeli, ohlala phakathi kwamakherubhi, nguwe wedwa onguNkulunkulu wayo yonke imibuso yomhlaba; wena wenze amazulu lomhlaba.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
17 Thoba indlebe yakho, Nkosi, uzwe, vula amehlo akho, Nkosi, ubone; uzwe wonke amazwi kaSenakheribi awathumele ukuklolodela uNkulunkulu ophilayo.
Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
18 Qiniso, Nkosi, amakhosi eAsiriya achithile zonke izizwe lamazwe azo;
“Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
19 aphosela onkulunkulu bazo emlilweni, ngoba babengeyisibo onkulunkulu, kodwa umsebenzi wezandla zabantu, izigodo lamatshe; ngalokho bababhubhisa.
Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
20 Ngakho-ke, Nkosi Nkulunkulu wethu, sisindise esandleni sakhe, ukuze yonke imibuso yomhlaba yazi ukuthi wena wedwa uyiNkosi.
Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
21 UIsaya indodana kaAmozi wasethumela kuHezekhiya, esithi: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Lokho okukhuleke kimi ngoSenakheribi inkosi yeAsiriya,
Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
22 leli yilizwi iNkosi elikhulume ngaye: Intombi emsulwa, indodakazi yeZiyoni iyakudelela, iyakuklolodela; indodakazi yeJerusalema inikina ikhanda ngemva kwakho.
Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
23 Ngubani omeyisileyo wamhlambaza? Njalo uphakamisele bani ilizwi, waphakamisela amehlo akho phezulu? Umelene loNgcwele kaIsrayeli.
Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
24 Uklolodele iNkosi ngesandla sezinceku zakho, wathi: Ngobunengi bezinqola zami mina ngenyukele endaweni ephakemeyo yezintaba, ezinhlangothini zeLebhanoni. Njalo ngizagamula imisedari yayo emide, ikhethelo lezihlahla zamafiri ayo, ngingene ekuphakameni kwemingcele yayo, igusu leKharmeli layo.
Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
25 Mina ngagebha, nganatha amanzi, langengaphansi yenyawo zami ngomisa yonke imifula yendawo evinjelweyo.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
26 Kawuzwanga yini ukuthi ngakwenza endulo, ngakubumba ensukwini zendulo? Khathesi ngikufikisile, ukuthi ube ngowokudiliza imizi evikelweyo ibe zinqumbi zamanxiwa.
“Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
27 Ngakho abahlali bayo babelesandla esifitshane, besaba, baba lenhloni, baba njengotshani beganga, lemibhida eluhlaza, utshani bempahla, lamabele ahanguliweyo engakami.
Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
28 Kodwa ngiyakwazi ukuhlala kwakho, lokuphuma kwakho, lokungena kwakho, lokungithukuthelela kwakho.
“Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
29 Ngenxa yokungithukuthelela kwakho, lokuthi umsindo wakho wenyukele endlebeni zami, ngizakufaka umkhala wami emakhaleni akho, letomu lami endebeni zakho, ngikwenze ubuyele ngendlela oweza ngayo.
Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
30 Lokhu-ke kuzakuba yisibonakaliso kuwe; lonyaka uzakudla okuzikhulelayo; langomnyaka wesibili umkhukhuzela; kuthi ngomnyaka wesithathu lihlanyele, livune, lihlanyele izivini, lidle izithelo zazo.
“Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
31 Lokuphephileyo kwendlu yakoJuda okuseleyo kuzaphinda kugxumeke impande phansi, kuthele izithelo ngaphezulu.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
32 Ngoba kuzaphuma eJerusalema insali, lokuphephileyo entabeni yeZiyoni. Ukutshiseka kweNkosi yamabandla kuzakwenza lokhu.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
33 Ngakho, utsho njalo uJehova ngenkosi yeAsiriya: Kayiyikungena kulumuzi, kayiyikutshoka umtshoko khona, kayiyikuza phambi kwawo ilesihlangu, kayiyikubuthelela idundulu maqondana lawo.
“Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
34 Ngendlela eyeza ngayo, ngayo izabuyela, njalo kayiyikungena kulo umuzi, itsho iNkosi.
Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
35 Ngoba ngizawuvikela lumuzi ukuwusindisa, ngenxa yami, langenxa kaDavida inceku yami.
“Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
36 Khona kwaphuma ingilosi yeNkosi, yatshaya enkambeni yamaAsiriya abazinkulungwane ezilikhulu lamatshumi ayisificaminwembili lanhlanu. Kwathi bevuka ekuseni kakhulu, khangela-ke, bonke babeyizidumbu ezifileyo.
Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
37 Ngakho uSenakheribi inkosi yeAsiriya wasuka, wahamba ebuyela, wahlala eNineve.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
38 Kwasekusithi ekhonza endlini kaNisiroki unkulunkulu wakhe, oAdrameleki loSharezeri amadodana akhe bamtshaya ngenkemba; bona basebephephela elizweni leArarathi. UEsarihadoni indodana yakhe wasebusa esikhundleni sakhe.
Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.