< U-Isaya 36 >
1 Kwasekusithi ngomnyaka wetshumi lane wenkosi uHezekhiya, uSenakheribi inkosi yeAsiriya wenyuka wamelana lemizi yonke evikelweyo yakoJuda, wayithatha.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 Njalo inkosi yeAsiriya yathuma uRabi-Shake esuka eLakishi esiya eJerusalema enkosini uHezekhiya lebutho elinzima. Wasesima emfolweni wechibi elingaphezulu, emgwaqweni omkhulu wensimu yomwatshi.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 Kwasekuphumela kuye uEliyakhimi, indodana kaHilikhiya, owayephezu kwendlu, loShebina umbhali, loJowa indodana kaAsafi umabhalane.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 URabi-Shake wasesithi kubo: Tshonini khathesi kuHezekhiya ukuthi: Itsho njalo inkosi enkulu, inkosi yeAsiriya: Lithemba bani leli othembele kulo?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 Ngithi (kodwa yilizwi lendebe): Kuleseluleko lamandla empi. Khathesi uthembele kubani ukuthi ungivukele?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Khangela, uthembele kuloludondolo lwalo umhlanga owephukileyo, kuyo iGibhithe, okuthi uba umuntu eseyama kulo, luzangena esandleni sakhe lusihlabe. Unjalo uFaro inkosi yeGibhithe kubo bonke abathembela kuye.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 Kodwa uba usithi kimi: Sithembela eNkosini uNkulunkulu wethu; kakusuye yini ozindawo zakhe eziphakemeyo lamalathi akhe uHezekhiya akususileyo, wathi kuJuda leJerusalema: Lizakhonza phambi kwaleli ilathi?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Ngakho-ke ake unike isibambiso enkosini yami, inkosi yeAsiriya; njalo ngizakunika amabhiza azinkulungwane ezimbili, uba wena ulakho ukunika abagadi bamabhiza phezu kwawo.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 Uzabuyisela njani-ke emuva ubuso bombusi oyedwa wabancinyane bezinceku zenkosi yami, wena-ke uthembela eGibhithe ngenxa yezinqola labagadi bamabhiza?
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Khathesi sengenyukile yini ngingelaNkosi ngimelene lalelilizwe ukulichitha? INkosi yathi kimi: Yenyuka umelene lalelilizwe, ulichithe.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 UEIiyakimi loShebina loJowa basebesithi kuRabi-Shake: Ake ukhulume lenceku zakho ngesiSiriya, ngoba siyasiqedisisa; ungakhulumi lathi ngesiJuda, endlebeni zabantu abaphezu komduli.
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Kodwa uRabi-Shake wathi: Inkosi yami ingithume enkosini yakho lakuwe yini ukukhuluma lamazwi? Kakusebantwini yini abahlezi phezu komduli ukuze badle ubulongwe babo, banathe umchamo wabo kanye lani?
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 URabi-Shake wema-ke, wamemeza ngelizwi elikhulu ngesiJuda, wathi: Zwanini amazwi enkosi enkulu, inkosi yeAsiriya.
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 Itsho njalo inkosi: UHezekhiya kangalikhohlisi, ngoba kayikuba lakho ukulikhulula.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 Futhi uHezekhiya angalenzi lithembele eNkosini, esithi: INkosi izasikhulula lokusikhulula; lumuzi kawuyikunikelwa esandleni senkosi yeAsiriya.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Lingamlaleli uHezekhiya, ngoba itsho njalo inkosi yeAsiriya: Dingani umusa wami ngesipho, lisithumele kimi; lidle ngulowo lalowo okwevini lakhe, langulowo lalowo okomkhiwa wakhe, linathe ngulowo lalowo amanzi omthombo wakhe;
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 ngize ngifike, ngilithathe, ngilise elizweni elifanana lelizwe lenu, ilizwe lamabele lewayini elitsha, ilizwe lesinkwa lezivini.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 UHezekhiya kangalihugi esithi: INkosi izasikhulula. Onkulunkulu bezizwe bakhulule yini, ngulowo lalowo ilizwe lakhe, esandleni samakhosi eAsiriya?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Bangaphi onkulunkulu beHamathi leArpadi? Bangaphi onkulunkulu beSefavayimi? Bayikhulule yini layo iSamariya esandleni sami?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Ngobani phakathi kwabo bonke onkulunkulu balawomazwe abakhulule ilizwe labo esandleni sami, ukuthi iNkosi ikhulule iJerusalema esandleni sami?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Kodwa bathula, kabaze bamphendula lizwi, ngoba umlayo wenkosi wawuyikuthi: Lingamphenduli.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 Kwasekufika uEliyakhimi, indodana kaHilikhiya, owayephezu kwendlu, loShebina umbhali, loJowa indodana kaAsafi, umabhalane, kuHezekhiya, izigqoko zabo zidatshuliwe, bamtshela amazwi kaRabi-Shake.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.