< U-Isaya 3 >
1 Ngoba khangela, iNkosi, uJehova wamabandla, izasusa eJerusalema lakoJuda insika lodondolo, insika yonke yesinkwa, lensika yonke yamanzi,
Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 iqhawe, lendoda yempi, umahluleli, lomprofethi, lomvumisi, lomdala,
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
3 induna yamatshumi amahlanu, lowemukelekayo ngobuso, lomeluleki, lombazi ohlakaniphileyo, lowazi amalumbo.
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 Ngizabanika abafana babe yiziphathamandla zabo, lezihluku zizabusa phezu kwabo.
Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 Labantu bazacindezelwa, omunye komunye, njalo ngulowo lalowo kumakhelwane wakhe; ijaha lizadelela omdala, lodelelekayo ohloniphekayo.
Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
6 Lapho umuntu ezabamba umfowabo wendlu kayise athi: Wena ulesembatho, woba ngumbusi wethu, lokhukuchithakala kube ngaphansi kwesandla sakho;
Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
7 uzaphakamisa ngalolosuku athi: Kangiyikuba ngumelaphi, ngoba endlini yami kakulakudla kakulasembatho; lingangimisi ngibe ngumbusi wabantu.
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 Ngoba iJerusalema ikhubekile, loJuda uwile, ngoba ulimi lwabo lezenzo zabo kumelene leNkosi, ukuvukela amehlo obukhosi bayo.
Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 Ukukhangeleka kobuso babo kuyafakaza ngabo; bememezela izono zabo njengeSodoma, kabazifihli. Maye kumphefumulo wabo! Ngoba bazenzela okubi.
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
10 Tshelani olungileyo ukuthi kuzakuba kuhle kuye; ngoba bazakudla isithelo sezenzo zabo.
Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Maye kokhohlakeleyo! Kuzakuba kubi kuye; ngoba umvuzo wezandla zakhe uzakwenziwa kuye.
Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 Abantu bami, abacindezeli babo ngabantwana, labesifazana bayababusa. Bantu bami, abakhokheli benu ngabaduhisi, basanganisa indlela yemikhondo yenu.
Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
13 INkosi izimisele ukuphikisana, imi ukuthi yahlulele abantu.
Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 INkosi ingena kusahlulelo labadala babantu bayo leziphathamandla zayo; ngoba lina lidle isivini; impango yomyanga isezindlini zenu.
Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Lina libachobozelani abantu bami, lichola ubuso babayanga? itsho iNkosi uJehova wamabandla.
Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 INkosi yasisithi: Ngenxa yokuthi amadodakazi eZiyoni eziphakamisile, ehamba elule intamo, ehuga ngamehlo, ehamba ngokuqoqomela ehamba, ekhencezisa izigqizo enyaweni zawo,
Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 ngakho iNkosi izakwenza inkanda yamadodakazi eZiyoni ibe loqweqwe, leNkosi izanqunula izitho zawo zangasese.
Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 Ngalolosuku iNkosi izasusa ubuhle bezigqizo zawo, lezicwatsho, lamasongo anjengenyanga,
Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
19 amacici, lamasongo, lezimbombozo,
ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
20 amaqhiye, lezigetsho, lamabhanti, lemifuma, lezintebe,
maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
21 izindandatho, lamacici amakhala,
mphete ndi zipini,
22 izigqoko zemikhosi, lamajazi, lezembatho, lezamba,
zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
23 lezibuko, lezigqoko zelembu elicolekileyo kakhulu, lamaqhele, lamaveyili.
magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 Kuzakuthi-ke endaweni yamakha kube levumba, lendaweni yebhanti kube khona igoda, lendaweni yenwele ezilungiswe kuhle kube khona impabanga, lendaweni yesigqoko esihle kube khona isaka, ukutsha endaweni yobuhle.
Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Amadoda akho azakuwa ngenkemba, lamaqhawe akho empini.
Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 Lamasango ayo azakhala alile; yenziwe ize izahlala emhlabathini.
Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.