< U-Isaya 29 >
1 Maye kuyo iAriyeli, kuyo iAriyeli umuzi uDavida amisa kuwo inkamba! Yengezelelani umnyaka emnyakeni; kayibhode imikhosi.
Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Kanti ngizayicindezela iAriyeli, njalo kube khona ukulila losizi; njalo kuzakuba njengeAriyeli kimi.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 Njalo ngizamisa inkamba inhlangothi zakho zonke, ngikuvimbezele ngedundulu, ngikumisele izinqaba ezimelene lawe.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 Njalo uzakwehliselwa phansi, ukhulume usemhlabathini, lenkulumo yakho izakuba phansi ethulini, lelizwi lakho lizakuba njengeloledlozi liphuma emhlabathini, lenkulumo yakho ibe ngumlozwi ophuma othulini.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 Njalo ixuku labezizwe bakho lizakuba njengothuli olucholekileyo, lexuku labalesihluku njengamakhoba adlulayo. Yebo, kuzahle kube masinyane.
Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 Uzakwethekelelwa yiNkosi yamabandla ngomdumo, langokuzamazama komhlaba, lomsindo omkhulu, isivunguzane, lesiphepho, lelangabi lomlilo oqothulayo.
Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 Lexuku lezizwe zonke elilwa limelene leAriyeli, ngitsho zonke ezilwa zimelene layo lezinqaba zayo, leziyicindezelayo, zizakuba njengephupho, umbono wobusuku.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 Kuzakuba lanjengolambileyo ephupha, khangela-ke, uyadla, kodwa aphaphame, lomphefumulo wakhe ungelalutho; loba njengowomileyo ephupha, khangela-ke, uyanatha, kodwa aphaphame, khangela-ke uphelelwa ngamandla, lomphefumulo wakhe uyalangatha; lizakuba njalo ixuku lazo zonke izizwe ezilwa zimelene lentaba iZiyoni.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Manini, lithithibale; zithokoziseni liphumputheke; badakiwe, kodwa hatshi ngewayini; bayadiyazela, kodwa hatshi ngenxa yokunathwayo okulamandla.
Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 Ngoba iNkosi ithululele phezu kwenu umoya wobuthongo obunzima, yavala amehlo enu; abaprofethi lezinhloko zenu, ababoni, ibagubuzele.
Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 Lawo wonke umbono usube kini njengamazwi ogwalo olunanyekiweyo okuthi balunika owazi umbhalo, besithi: Bala lokhu siyakuncenga; yena athi: Ngingeke, ngoba lunanyekiwe.
Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
12 Ugwalo beselunikwa ongazi umbhalo, besithi: Bala lokhu, siyakuncenga; yena athi: Kangiwazi umbhalo.
Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 INkosi yasisithi: Ngenxa yokuthi lababantu besondela ngomlomo wabo langezindebe zabo bengihlonipha, kodwa babeka inhliziyo yabo khatshana lami, lokungesaba kwabo kufundiswa ngumlayo wabantu;
Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 ngakho, khangela, ngizaqhubeka ukukwenza ngokumangalisayo lalababantu, umsebenzi omangalisayo lesimanga; ngoba inhlakanipho yabahlakaniphileyo babo izaphela, lokuqedisisa kwabaqedisisayo babo kucatshe.
Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Maye kulabo abajula besuka eNkosini ukuze bafihle icebo labo, lemisebenzi yabo isemnyameni, bathi: Ngubani osibonayo? Njalo ngubani osaziyo?
Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Ukugonqomisa kwenu kuthiwa kunjengebumba lombumbi! Ngoba umsebenzi uzakutsho yini ngaye owenzileyo ukuthi: Kangenzanga? Kumbe okubunjiweyo kungatsho yini ngombumbi wakho ukuthi: Kaqedisisi?
Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Kakuseyisikhatshana esifitshane yini, ukuthi iLebhanoni iphendulwe ibe yinsimu ethelayo, lensimu ethelayo ithiwe injengehlathi?
Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Njalo ngalolosuku izacuthe zizakuzwa amazwi ogwalo, lamehlo eziphofu abone ekufiphaleni lemnyameni.
Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
19 Abathobekileyo labo bazakwandisa intokozo eNkosini, labangabayanga ebantwini bathokoze koNgcwele kaIsrayeli.
Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 Ngoba olesihluku uzaphela, lodelelayo uqediwe, labo bonke abalindele okubi baqunyiwe;
Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 abenza umuntu one ngelizwi, bambekele umjibila okhuzayo esangweni, baphambule olungileyo ngento engelutho.
Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 Ngakho itsho njalo iNkosi eyahlenga uAbrahama, ngendlu kaJakobe: Khathesi uJakobe kayikuba lanhloni, lobuso bakhe khathesi kabuyikuhloba.
Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 Ngoba lapho ebona abantwana bakhe, umsebenzi wezandla zami, phakathi kwakhe, bazangcwelisa ibizo lami; bangcwelise oNgcwele kaJakobe, besabe uNkulunkulu kaIsrayeli.
Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Lalabo abaduhayo emoyeni bazakwazi ukuqedisisa, labangungunayo bazafunda imfundiso.
Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”