< U-Isaya 22 >
1 Umthwalo wesigodi sombono. Kutheni kuwe khathesi, ukuthi ngulowo lalowo wakho akhwele empahleni zezindlu?
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Wena ogcwele imisindo, muzi oxokozelayo, dolobho elilentokozo, ababuleweyo bakho kababulawanga ngenkemba, kabafelanga empini.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 Bonke ababusi bakho babaleke kanyekanye, babotshwe ngabatshoki, bonke abatholakala kuwe, babotshiwe kanyekanye, babaleke besuka khatshana.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Ngenxa yalokhu ngathi: Susani amehlo kimi; kangikhale kabuhlungu; ungaphangisi ukungiduduza ngenxa yokuchitheka kwendodakazi yabantu bakithi.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 Ngoba kulusuku lokusanganiseka, lolokunyathelela phansi, lolokuphithizela kweNkosi uJehova wamabandla esigodini sombono, lokudilizela phansi umduli, lolokuhlaba umkhosi kuze kube sentabeni.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 IElamu yathatha-ke isikhwama semitshoko, kanye lenqola, abantu, abagadi bamabhiza; leKiri yembula isihlangu.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 Kuzakuthi-ke izigodi zakho ezikhethekileyo zigcwala izinqola, labagadi bamabhiza bazihlele lokuzihlela ngasesangweni.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 Njalo yena uzakwembula isimbombozo sakoJuda; langalolosuku wena uzakhangela izikhali zendlu yehlathi.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 Njalo lizabona imikenke yomuzi kaDavida, ukuthi minengi, liqoqe amanzi echibini elingaphansi.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 Lizabala izindlu zeJerusalema, lidilize izindlu ukuze liqinise umduli.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 Lizakwenza ichibi phakathi kwemiduli yomibili lisenzela amanzi omgodi omdala. Kodwa kaliyikukhangela kowakwenzayo, kalimnanzanga owakubumbayo kudala.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 Langalolosuku iNkosi uJehova wamabandla izamemezela ukulila, lokukhala, lokuphucwa kwamakhanda, lokugqokwa kwesaka.
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 Kodwa khangela, injabulo lokuthaba, ukubulawa kwenkomo, lokuhlatshwa kwezimvu, ukudliwa kwenyama, lokunathwa kwewayini; lathi: Asidleni sinathe, ngoba kusasa sizakufa.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 Kodwa iNkosi yamabandla yembula endlebeni zami isithi: Isibili lesisono kaliyikusenzelwa inhlawulo yokuthula lize life, kutsho iNkosi uJehova wamabandla.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Itsho njalo iNkosi uJehova wamabandla: Hamba uye kulo umphathi, kuShebina, ophezu kwendlu, uthi:
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 Ulani lapha, njalo ulobani lapha, ukuthi uzigebhele ingcwaba lapha, njengozigebhela ingcwaba lakhe phezulu, ozigubhela indawo yokuhlala edwaleni?
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Khangela, iNkosi izakujikijela khatshana ngokujika kwendoda; izakugoqela ngokukugoqela,
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 ikuthandele lokukuthandela njengebhola eligoqelwayo; njengebhola izakuphosela elizweni elibanzi; lalapho uzafela, lalapho izinqola zodumo lwakho zizakuba lihlazo, olwendlu yenkosi yakho!
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 Njalo ngizakusunduza usuke esikhundleni sakho, ikuwise ekumeni kwakho.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 Kuzakuthi-ke ngalolosuku ngibize inceku yami uEliyakhimi indodana kaHilikhiya;
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 ngizamgqokisa isigqoko sakho, ngimqinise ngebhanti lakho, nginikeze umbuso wakho esandleni sakhe; njalo yena uzakuba nguyise kubahlali beJerusalema lendlini yakoJuda.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 Ngizabeka-ke isihluthulelo sendlu kaDavida ehlombe lakhe; yena uzavula kungavali muntu, avale kungavuli muntu.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 Ngizambethela njengesikhonkwane endaweni eqinileyo; njalo uzakuba yisihlalo sobukhosi esilodumo endlini kayise.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 Njalo bazaphanyeka phezu kwakhe udumo lonke lwendlu kayise, inzalo lembewu, zonke izitsha ezincinyane, kusukela ezitsheni zenkezo kusiya kuzo zonke izitsha zeziphiso.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 Ngalolosuku, itsho iNkosi yamabandla, isikhonkwane esabethelwa endaweni eqinileyo sizasuswa, siganyulwe siwe; lomthwalo obuphezu kwaso uzaqunywa; ngoba iNkosi ikhulumile.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.