< U-Isaya 15 >

1 Umthwalo kaMowabi. Ngoba ngobusuku iAri kaMowabi ichithekile, iqunyiwe; ngoba ngobusuku iKiri kaMowabi ichithekile, iqunyiwe.
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 Wenyukela eBayiti leDiboni, indawo eziphakemeyo, ukuyalila; uMowabi uzaqhinqa isililo ngeNebo langeMedeba; kulempabanga kuwo wonke amakhanda abo, zonke indevu zigeliwe;
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 ezitaladeni zabo bazibhinca ngamasaka; empahleni zezindlu zabo lezitaladeni zabo wonke uqhinqa isililo, besehla bekhala inyembezi.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 LeHeshiboni leEleyale kuzakhala; ilizwi labo lizwakale kuze kube seJahazi; ngenxa yalokhu abahlomileyo bakoMowabi bayamemeza; umphefumulo wakhe uyathuthumela kuye.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Inhliziyo yami iyamkhalela uMowabi; ababalekayo bakhe bafinyelele eZowari, ithokazi elileminyaka emithathu; ngoba umqanso weLuhithi, bawenyuka bekhala inyembezi; ngoba endleleni yeHoronayimi baphakamisa ukukhala kwencithakalo.
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 Ngoba amanzi eNimirimi azakuba zincithakalo; ngoba utshani buyoma, uhlaza luyaphela, kakukho okuluhlaza.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Ngenxa yalokhu ukwanda abakwenzileyo lempahla yabo bazakuthwalela esifuleni seminyezane.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Ngoba ukukhala kuzabhoda umngcele kaMowabi, ukuqhinqa kwakhe isililo kufinyelela eEgilayimi, yebo, ukuqhinqa kwakhe isililo kufinyelela eBeri-Elimi.
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 Ngoba amanzi eDiboni agcwele igazi; ngoba ngizamisela iDiboni okunye futhi, isilwane kulabo abaphunyukileyo bakoMowabi lakunsali yelizwe.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< U-Isaya 15 >