< U-Isaya 14 >

1 Ngoba iNkosi izamhawukela uJakobe, imkhethe futhi uIsrayeli, ibabeke elizweni lakibo; labezizwe bazahlangana labo, njalo bazanamathela endlini kaJakobe.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Labantu bazabathatha, babase endaweni yabo; lendlu kaIsrayeli izabafuya elizweni leNkosi, babe yizigqili lezigqilikazi; njalo bazathumba abathumbi babo, babuse abacindezeli babo.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Kuzakuthi-ke ngosuku iNkosi ezaliphumuza ngalo ebuhlungwini benu lekuhluphekeni kwenu lemtshikatshikeni onzima ebelisetshenziswa kiwo,
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 lizaphakamisa lesisaga ngenkosi yeBhabhiloni lithi: Uphele njani umcindezeli! Owegolide usuphelile!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 INkosi ilwephule udondolo lwabakhohlakeleyo, intonga yababusi.
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Owatshaya abantu entukuthelweni ngokutshaya okungapheliyo, owabusa izizwe ngolaka, wazingelwa kungekho onqandayo.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Umhlaba wonke uphumule, ulokuthula; baqhamuka ngokuhlabelela.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Lezihlahla zefiri ziyathokoza ngawe, imisedari yeLebhanoni, isithi: Selokhu walala phansi, kakulamgamuli owenyukela kithi.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Isihogo ngaphansi siyanyakaziswa ngenxa yakho ukukuhlangabeza ekuzeni kwakho; sikuvusela imimoya efileyo, impongo zonke zomhlaba, sisukumise wonke amakhosi ezizwe ezihlalweni zawo zobukhosi. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Bonke bazaphendula bathi kuwe: Lawe usubuthakathaka njengathi; usufanana lathi.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Ubukhosi bakho sebehliselwe esihogweni, lokukhala kwamachacho akho; izimpethu zizakwendlalwa ngaphansi kwakho, lemihlavane ikugubuzele. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Uwe kanganani uvela emazulwini, wena okhanyayo, ndodana yokusa! Uqunyelwe emhlabathini, wena owawisela phansi izizwe!
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Wena wasusithi enhliziyweni yakho: Ngizakwenyukela emazulwini; ngaphezu kwenkanyezi zikaNkulunkulu ngiphakamise isihlalo sami sobukhosi; ngihlale entabeni yenhlangano ezinhlangothini zenyakatho;
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 ngizakwenyukela ngaphezu kwendawo eziphakemeyo zamayezi; ngizenze ngifanane loPhezukonke.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Kodwa uzakwehliselwa esihogweni, ezinhlangothini zomgodi. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Abakubonayo bazakujolozela, bakuqaphele, besithi: Nguye lo umuntu yini owenza ukuthi umhlaba uthuthumele, owanyakazisa imibuso,
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 owamisa ilizwe laba njengenkangala, wachitha imizi yalo, ongavulelanga izibotshwa zakhe ziye ekhaya?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Wonke amakhosi ezizwe, wonke alala phansi ngodumo, ileyo laleyo endlini yayo;
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 kodwa wena uphoselwe ngaphandle kwengcwaba lakho, njengehlumela elinengekayo, njengelembu lababuleweyo, begwazwe ngenkemba, abehlela phansi ematsheni omgodi, njengesidumbu esinyathelelwe phansi.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Kawuyikuhlanganiswa kanye labo ekungcwatshweni, ngoba ulichithile ilizwe lakini, wabulala abantu bakini. Inzalo yabenzi bobubi kayiyikubizwa kuze kube nininini.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Lungiselani ukubulawa kwabantwana babo ngenxa yobubi baboyise, ukuze bangavuki badle ilifa lelizwe, bagcwalise ubuso bomhlaba ngemizi.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Ngoba ngizabavukela, itsho iNkosi yamabandla, ngiqume kusuke eBhabhiloni ibizo, lensali, lendodana, lomzukulu, itsho iNkosi.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Ngizayimisa ibe yindawo yezinhloni lamatete amanzi, ngiyithanyele ngomthanyelo wencithakalo, kutsho iNkosi yamabandla.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 INkosi yamabandla ifungile isithi: Isibili, njengokucabanga kwami kuzakuba njalo, lanjengokweluleka kwami khona kuzakuma!
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Ukuthi ngimephule umAsiriya elizweni lami, ngimnyathele phezu kwezintaba zami; beselisuka ijogwe lakhe phezu kwabo, lomthwalo wakhe usuke ehlombe labo.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Lesi yiseluleko eselulekwe ngomhlaba wonke, njalo lesi yisandla eselulelwe izizwe zonke.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Ngoba iNkosi yamabandla ikucebile, ngubani-ke ongakuphuthisa? Lesandla sayo seluliwe, njalo ngubani ongasibuyisela emuva?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 Ngomnyaka wokufa kwenkosi uAhazi kwaba lalo umthwalo:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Ungathokozi, wena wonke Filisti, ngokuthi intonga ekutshayileyo yephukile; ngoba empandeni yenyoka kuzavela ibululu, lesithelo sabo sibe yinyoka ephaphayo etshisayo.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Lamazibulo abayanga azakwelusela, labaswelayo balale bevikelekile; kodwa ngizabulala impande yakho ngendlala, njalo abulale insali yakho.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Qhinqa isililo, sango, ukhale, muzi. Uncibilike, Filisti, wonke. Ngoba enyakatho kuvela intuthu, njalo kakho ozakuba yedwa ngezikhathi zakhe ezimisiweyo.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Lezithunywa zesizwe zizaphendulwa ngokuthini? Ngokuthi: INkosi iyisekele iZiyoni, labahluphekayo babantu bayo bazathembela kuyo.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< U-Isaya 14 >