< UHoseya 1 >

1 Ilizwi leNkosi elafika kuHoseya indodana kaBeyeri ensukwini zaboUziya, uJothamu, uAhazi, uHezekhiya, amakhosi akoJuda, lensukwini zikaJerobhowamu indodana kaJowasi inkosi yakoIsrayeli.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 Ukuqala kwelizwi leNkosi ngoHoseya. INkosi yasisithi kuHoseya: Hamba uzithathele umfazi wobuwule, labantwana bobuwule; ngoba ilizwe liyawula kakhulu ngokungayilandeli iNkosi.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 Wasehamba wathatha uGomeri indodakazi kaDibilayimi; wasekhulelwa, wamzalela indodana.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 INkosi yasisithi kuye: Biza ibizo layo uthi nguJizereyeli, ngoba kuseseyisikhatshana ngizaphindisela icala legazi leJizereyeli phezu kwendlu kaJehu, ngiwuqede umbuso wendlu kaIsrayeli.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 Kuzakuthi ngalolosuku ngephule idandili likaIsrayeli esigodini seJizereyeli.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 Wasebuya ekhulelwa, wazala indodakazi. UNkulunkulu wasesithi kuye: Biza ibizo layo uthi nguLo-Ruhama, ngoba kangisayikubuya ngihawukele indlu kaIsrayeli, kodwa ngizabasusa lokubasusa.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 Kodwa ngizayihawukela indlu yakoJuda, ngibasindise ngeNkosi uNkulunkulu wabo; njalo kangiyikubasindisa ngedandili, loba ngenkemba, loba ngempi, ngamabhiza, kumbe ngabagadi bamabhiza.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Esemlumulile uLo-Ruhama, wakhulelwa, wazala indodana.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 UNkulunkulu wasesithi: Biza ibizo layo uthi nguLo-Ami; ngoba kalisibo abantu bami, ngakho mina kangisuye owenu.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Kube kanti inani labantwana bakoIsrayeli lizakuba ngangetshebetshebe lolwandle elingeke lilinganiswe elingeke libalwe. Njalo kuzakuthi, endaweni yokuthi kuthiwe kubo: Kalisibo abantu bami; kuzakuthiwa kubo: Lingabantwana bakaNkulunkulu ophilayo.
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 Ngakho abantwana bakoJuda labantwana bakoIsrayeli bazabuthaniswa ndawonye, bazimisele inhloko eyodwa, benyuke baphume elizweni. Ngoba luzakuba lukhulu usuku lweJizereyeli.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

< UHoseya 1 >