< UHoseya 6 >

1 Wozani sibuyele eNkosini, ngoba yona idwengulile, njalo izaselapha; itshayile, njalo izasibopha.
“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
2 Izasivuselela emva kwensuku ezimbili, ngosuku lwesithathu isivuse, njalo siphile phambi kwayo.
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 Khona sizakwazi, silandele ukuyazi iNkosi; ukuphuma kwayo kulungiswe njengokusa; njalo izafika kithi njengezulu, njengezulu lemuva lelokuqala emhlabeni.
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 Ngizakwenzani kuwe, Efrayimi? Ngizakwenzani kuwe, Juda? Ngoba umusa wenu unjengeyezi lekuseni, lanjengamazolo ovivi athintithekayo.
Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 Ngenxa yalokhu ngibagamule ngabaprofethi, ngababulala ngamazwi omlomo wami; lezahlulelo zakho zinjengokukhanya okuphumayo.
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 Ngoba ngaloyisa umusa, hatshi-ke umhlatshelo, lolwazi lukaNkulunkulu kuleminikelo yokutshiswa.
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
7 Kodwa bona njengoluntu baseqile isivumelwano; lapho benza ngenkohliso kimi.
Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
8 IGileyadi ingumuzi wabenzi bokubi, ilemikhondo yegazi.
Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
9 Njengamaviyo abaphangi acathamele umuntu, linjalo ixuku labapristi; bayabulala endleleni yeShekema; ngoba benza inkohlakalo.
Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
10 Endlini yakoIsrayeli ngibone into eyesabekayo; lapho kulobuwule bukaEfrayimi, uIsrayeli ungcolisiwe.
Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
11 Lawe Juda, ukumisele isivuno, lapho ngibuyise ukuthunjwa kwabantu bami.
“Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”

< UHoseya 6 >