< UHoseya 13 >

1 Lapho uEfrayimi ekhuluma kwakulokuqhuqha, waziphakamisa koIsrayeli; kodwa waba lecala ngoBhali, wafa.
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Khathesi-ke baqhubeka besona, bazenzela izithombe ezibunjwe ngokuncibilikisa zesiliva sabo, izithombe njengokuqedisisa kwabo, zonke zingumsebenzi wezingcitshi; abathi ngazo: Abantu abanikela imihlatshelo bazakwanga amathole.
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 Ngakho bazakuba njengeyezi lekuseni, lanjengamazolo ovivi ahambayo; njengomule ophetshulwa yisivunguzane ebaleni lokubhulela, njengentuthu ephuma etshiminini.
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Kube kanti mina ngiyiNkosi, uNkulunkulu wakho, kusukela elizweni leGibhithe; ngakho kawuyikwazi unkulunkulu ngaphandle kwami, ngoba kakho umsindisi ngaphandle kwami.
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 Mina ngakwazi enkangala, elizweni elomileyo kakhulu.
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Njengokwedlelo labo, ngokunjalo basutha; basutha, lenhliziyo yabo yaphakama; ngenxa yalokho bangikhohlwa.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
7 Ngakho ngizakuba kubo njengesilwane, njengengwe endleleni ngizabacathamela.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 Ngizabahlangabeza njengebhere elithathelwe imidlwane, ngidabule isisibekelo senhliziyo yabo, ngibadlele lapho njengesilwane; isilo seganga sizabadabudabula.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 Kukuchithile, Israyeli, kodwa kimi kulosizo lwakho.
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Pho, ingaphi inkosi yakho, ukuthi ikusindise emizini yakho yonke? Labehluleli bakho owathi ngabo: Nginike inkosi leziphathamandla?
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Ngakunika inkosi ekuthukutheleni kwami, ngayisusa ngolaka lwami.
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Ububi bukaEfrayimi bubotshiwe, isono sakhe sibekiwe.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Insizi zowesifazana ohelelwayo zizamfikela; uyindodana engahlakaniphanga, ngoba ingehlale isikhathi emlonyeni wesizalo sabantwana.
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 Ngizabenzela inhlawulo yokuthula emandleni engcwaba, ngibahlenge ekufeni. Kufa, bangaphi omatshayabhuqe bezifo zakho? Ngcwaba, ingaphi incithakalo yakho? Uphenduko luzasitheliswa emehlweni ami. (Sheol h7585)
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
15 Loba yena engaveza izithelo phakathi kwabafowabo, kuzafika umoya wempumalanga, umoya weNkosi, usenyuka enkangala, lomthombo wakhe uzakutsha, kome lesiphethu sakhe; wona uzaphanga okuligugu kwazo zonke izitsha eziloyisekayo.
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 ISamariya izakuba lunxiwa, ngoba ihlamukele uNkulunkulu wayo; bazakuwa ngenkemba, labantwana babo bachotshozwe, labesifazana babo abakhulelweyo baqhaqhwe.
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

< UHoseya 13 >