< UHoseya 11 >
1 UIsrayeli esengumntwana ngamthanda, ngayibiza indodana yami ukuthi iphume eGibhithe.
“Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
2 Kwathi bebabiza, ngokunjalo basuka phambi kwabo; bahlabela oBhali, batshisela izithombe ezibaziweyo impepha.
Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
3 Mina-ke ngacathulisa uEfrayimi; ngababamba ngezingalo zabo; kodwa kabazanga ukuthi ngibelaphile.
Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
4 Ngabadonsa ngamagoda omuntu, ngentambo zothando, ngaba kibo njengalabo abasusa ijogwe ezihlathini zabo, ngakhothama kubo, ngabanika ukudla.
Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
5 Kayikubuyela elizweni leGibhithe, kodwa umAsiriya yena uzakuba yinkosi yakhe, ngoba balile ukuphenduka.
“Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
6 Inkemba izatheleka emizini yakhe, iqede imigoqo yakhe, ibadle, ngenxa yamacebo abo.
Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
7 Njalo abantu bami banamathela ekuhlehleleni muva kimi; lanxa bebabizela koPhezukonke, kakho ngitsho owayengamphakamisa.
Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
8 Ngizakunikela njani, Efrayimi? Ngikudele njani, Israyeli? Ngizakwenza njani ube njengeAdima? Ngikubeke njani njengeZeboyimi? Inhliziyo yami isiphendukile phakathi kwami, izihawu zami ziyakhudumala kanyekanye.
“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
9 Kangiyikwenza ukuvutha kolaka lwami; kangiyikubuyela ngichithe uEfrayimi; ngoba nginguNkulunkulu, kangisuye umuntu, oNgcwele phakathi kwakho; kangiyikungena emzini.
Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
10 Bazayilandela iNkosi; izabhonga njengesilwane; lapho yona isibhonga, khona abantwana bazavela entshonalanga beqhaqhazela.
Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 Bazaqhaqhazela njengenyoni evela eGibhithe, lanjengejuba elivela elizweni leAsiriya; njalo ngizabenza bahlale ezindlini zabo, itsho iNkosi.
Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
12 UEfrayimi ungizingelezele ngamanga, lendlu kaIsrayeli ngenkohliso; kodwa uJuda usabusa loNkulunkulu, uthembekile kanye labangcwele.
Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.