< UHagayi 1 >

1 Ngomnyaka wesibili kaDariyusi inkosi, ngenyanga yesithupha, ngosuku lokuqala lwenyanga, kwafika ilizwi leNkosi ngesandla sikaHagayi umprofethi kuZerubhabheli indodana kaSheyalithiyeli, umbusi wakoJuda, lakuJoshuwa indodana kaJehozadaki, umpristi omkhulu, lisithi:
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 Itsho njalo iNkosi yamabandla, isithi: Lababantu bathi: Isikhathi kasikafiki, isikhathi sokuthi indlu yeNkosi yakhiwe.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Laselifika ilizwi leNkosi ngesandla sikaHagayi umprofethi, lisithi:
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 Kuyisikhathi senu yini, lina ngokwenu, sokuthi lihlale ezindlini zenu ezembeswe ngaphakathi ngamapulanka, kanti le indlu ilunxiwa?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 Ngakho khathesi itsho njalo iNkosi yamabandla: Bekani inhliziyo yenu ezindleleni zenu.
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 Lihlanyele okunengi, langenisa okulutshwana; liyadla, kodwa kalisuthi; liyanatha, kodwa kalikholwa; liyagqoka, kodwa kakho okhudumalayo, lohola umholo uholela umholo esikhwameni esibhobokileyo.
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Itsho njalo iNkosi yamabandla: Bekani inhliziyo yenu ezindleleni zenu.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 Yenyukelani entabeni, lilethe izigodo, liyakhe indlu; njalo ngizathokoza ngayo, ngidunyiswe, itsho iNkosi.
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 Belikhangele okunengi, kodwa khangelani, kube kulutshwana; lapho likuletha ekhaya, ngikuphephethile. Kungani? itsho iNkosi yamabandla. Ngenxa yendlu yami elunxiwa, kanti lina liyagijimela ngulowo lalowo endlini yakhe.
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 Ngakho-ke amazulu phezu kwenu ayagodla ukuze kungabi lamazolo, lomhlabathi uyagodla izithelo zawo.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 Ngasengibiza ukoma phezu kwelizwe, laphezu kwezintaba, laphezu kwamabele, laphezu kwewayini elitsha, laphezu kwamafutha, laphezu kwalokho umhlabathi okuvezayo, laphezu kwabantu, laphezu kwezinkomo, laphezu kwawo wonke umsebenzi wezandla.
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Khona uZerubhabheli indodana kaSheyalithiyeli, loJoshuwa indodana kaJehozadaki, umpristi omkhulu, layo yonke insali yabantu, balilalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wabo, lamazwi kaHagayi umprofethi, njengoba iNkosi uNkulunkulu wabo wayemthumile; njalo abantu besaba phambi kweNkosi.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Wasekhuluma uHagayi isithunywa seNkosi ngelizwi leNkosi ebantwini, esithi: Ngilani, itsho iNkosi.
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 INkosi yasivusa umoya kaZerubhabheli indodana kaSheyalithiyeli, umbusi wakoJuda, lomoya kaJoshuwa indodana kaJehozadaki, umpristi omkhulu, lomoya wensali yonke yabantu; basebesiza, benza umsebenzi endlini yeNkosi yamabandla, uNkulunkulu wabo,
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 ngosuku lwamatshumi amabili lane lwenyanga yesithupha, ngomnyaka wesibili kaDariyusi inkosi.
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< UHagayi 1 >