< UGenesisi 9 >
1 UNkulunkulu wasebusisa uNowa lamadodana akhe, wathi kibo: Zalani lande ligcwalise umhlaba.
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 Lokwesatshwa kwenu lokuqhuqhwa kwenu kuzakuba phezu kwayo yonke inyamazana yomhlaba laphezu kwayo yonke inyoni yamazulu; kukho konke okuhamba emhlabeni lakuzo zonke inhlanzi zolwandle; zinikelwe ezandleni zenu.
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 Konke okuhambayo okuphilayo kuzakuba yikudla kini; njengombhida oluhlaza ngilinikile konke.
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 Kodwa inyama lempilo yayo, igazi layo, kalisoze likudle.
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 Njalo sibili, igazi lenu, elempilo yenu, ngizalibiza; esandleni sayo yonke inyamazana ngizalibiza; lesandleni somuntu, lesandleni somfowabo womunye lomunye ngizabiza umphefumulo womuntu.
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 Ochitha igazi lomuntu, ngomuntu lizachithwa igazi lakhe; ngoba ngomfanekiso kaNkulunkulu wamenza umuntu.
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 Ngakho lina, zalani, lande, lizale ngokwengezelelweyo emhlabeni, lande kuwo.
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 UNkulunkulu wasekhuluma kuNowa lakumadodana akhe kanye laye, esithi:
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 Mina-ke, khangelani, ngiyamisa isivumelwano sami lani lenzalo yenu emva kwenu,
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 laso sonke isidalwa esiphilayo esilani, esenyoni lesesifuyo, lesayo yonke inyamazana yomhlaba lani; kusukela kubo bonke abaphume emkhunjini, kusiya kuyo yonke inyamazana yomhlaba.
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 Njalo ngizamisa isivumelwano sami lani; njalo kakusayikubhujiswa yonke inyama ngamanzi kazamcolo; ukuze kungasabi khona uzamcolo ukubhubhisa umhlaba.
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 UNkulunkulu wasesithi: Lokhu kuyisibonakaliso sesivumelwano engisinika phakathi kwami lani laso sonke isidalwa esiphilayo esilani, kuze kube yizizukulwana laphakade.
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 Ngizamisa umchilowamakhosikazi wami emayezini; uzakuba yisibonakaliso sesivumelwano phakathi kwami lomhlaba.
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 Kuzakuthi nxa ngibuyisa amayezi phezu komhlaba, umchilowamakhosikazi uzabonwa eyezini;
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 khona ngizakhumbula isivumelwano sami, esiphakathi kwami lani laso sonke isidalwa esiphilayo sayo yonke inyama; lamanzi kawasayikuba nguzamcolo ukubhubhisa yonke inyama.
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 Lomchilowamakhosikazi uzakuba semayezini, njalo ngizawubona ukukhumbula isivumelwano esilaphakade phakathi kukaNkulunkulu laso sonke isidalwa esiphilayo, sayo yonke inyama esemhlabeni.
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 UNkulunkulu wasesithi kuNowa: Lokhu kuyisibonakaliso sesivumelwano engisimise phakathi kwami layo yonke inyama esemhlabeni.
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 Amadodana kaNowa aphumayo-ke emkhunjini ayengoShemu loHamu loJafethi; njalo uHamu nguyise kaKhanani.
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 Laba bobathathu ngamadodana kaNowa; lomhlaba wonke wasatshalaliswa ngokuvela kubo.
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 UNowa waseqala ukuba ngumlimi, wahlanyela isivini.
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 Wasenatha okwewayini, wadakwa; njalo waba nqunu phakathi kwethente lakhe.
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 UHamu, uyise kaKhanani, wasebona ubunqunu bukayise, wasetshela abafowabo ababili phandle.
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 OShemu loJafethi basebethatha isembatho, basibeka emahlombe abo bobabili, bahamba nyovane, bagubuzela ubunqunu bukayise; lobuso babo babusemuva ukuze bangaboni ubunqunu bukayise.
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 UNowa wasevuka ewayinini lakhe, wakwazi lokho indodana yakhe encinyane ekwenze kuye.
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 Wasesithi: Kaqalekiswe uKhanani, uzakuba yisigqili sezigqili kubafowabo.
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 Wasesithi: Ibusisiwe iNkosi uNkulunkulu kaShemu, loKhanani abe yisigqili sakhe.
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 UNkulunkulu amqhelise uJafethi, njalo ahlale emathenteni kaShemu, loKhanani abe yisigqili sakhe.
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 Emva kukazamcolo uNowa wasephila iminyaka engamakhulu amathathu lamatshumi amahlanu.
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 Zonke-ke insuku zikaNowa zaba yiminyaka engamakhulu ayisificamunwemunye lamatshumi amahlanu; wasesifa.
Anamwalira ali ndi zaka 950.