< UGenesisi 50 >

1 UJosefa wasewela phezu kobuso bukayise, wakhala inyembezi phezu kwakhe, wamanga.
Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
2 UJosefa waselaya inceku zakhe abelaphi ukuthi baqhole uyise ngomuthi; labelaphi bamqhola uIsrayeli ngomuthi.
Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
3 Zagcwaliseka kuye insuku ezingamatshumi amane, ngoba ngokunjalo zazigcwaliseka insuku zabaqholwe ngomuthi. LamaGibhithe amlilela insuku ezingamatshumi ayisikhombisa.
Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
4 Kwathi sezidlulile insuku zokumkhalela, uJosefa wakhuluma lendlu kaFaro esithi: Uba-ke ngithole umusa emehlweni enu, ake likhulume endlebeni zikaFaro, lisithi:
Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
5 Ubaba wangifungisa esithi: Khangela, ngiyafa; engcwabeni engazigebhela lona elizweni leKhanani, lapho ungingcwabe. Khathesi-ke, ake ngenyuke ngiyengcwaba ubaba, besengibuya.
‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
6 UFaro wasesithi: Yenyuka uyengcwaba uyihlo njengokukufungisa kwakhe.
Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
7 UJosefa wasesenyuka ukuyangcwaba uyise, kwenyuka kanye laye zonke izinceku zikaFaro, abadala bendlu yakhe, labo bonke abadala belizwe leGibhithe,
Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
8 lendlu yonke kaJosefa, labafowabo, lendlu kayise; kuphela abantwana babo abancinyane lezimvu zabo lenkomo zabo bakutshiya elizweni leGosheni.
Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
9 Kwasekusenyuka kanye laye konke izinqola labagadi bamabhiza, kwaba liviyo elinzima kakhulu.
Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
10 Kwathi sebefike esizeni seAtadi, eliphetsheya kweJordani, balila khona, isililo esikhulu lesinzima kakhulu, bamenzela uyise isililo insuku eziyisikhombisa.
Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
11 Kwathi abakhileyo belizwe, amaKhanani, bebona ukulila esizeni seAtadi, bathi: Lesi yisililo esinzima samaGibhithe. Ngakho basebesitha ibizo laso iAbeli-Mizirayimi, eliphetsheya kweJordani.
Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
12 Amadodana akhe asemenzela njalo njengalokhu ewalayile;
Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
13 ngoba amadodana akhe amthwalela elizweni leKhanani, amngcwaba obhalwini lwensimu yeMakaphela, uAbrahama aluthenga lensimu, lube yindawo yakhe yokungcwabela, kuEfroni umHethi, eqondane leMamre.
Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
14 UJosefa wasebuyela eGibhithe, yena labafowabo labo bonke abenyuka laye ukuyangcwaba uyise, esemngcwabile uyise.
Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
15 Kwathi abafowabo bakaJosefa sebebonile ukuthi uyise usefile bathi: Mhlawumbe uJosefa uzasizonda, ngoqotho asiphindisele ububi bonke esabenza kuye.
Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
16 Basebenika isilayezelo kuJosefa besithi: Uyihlo walaya engakafi, esithi:
Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
17 Lizakutsho kanje kuJosefa lithi: Ngiyakucela, akuxolele isiphambeko sabafowenu lesono sabo, ngoba bakwenzela okubi; khathesi-ke ake uxolele isiphambeko sezinceku zikaNkulunkulu kayihlo. UJosefa wasekhala inyembezi nxa bekhuluma kuye.
‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
18 Labafowabo labo beza, bawa phansi phambi kwakhe, bathi: Khangela, siyizinceku zakho.
Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
19 Kodwa uJosefa wathi kibo: Lingesabi, ngoba kanti ngisendaweni kaNkulunkulu yini?
Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
20 Kodwa lina laceba okubi kimi, uNkulunkulu waceba ngokuhle, ukuze enze njengalamuhla, ukuze alondoloze abantu abanengi bephila.
Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
21 Khathesi-ke lingesabi; mina ngizalondla lina labantwanyana benu. Wasebaduduza, wakhuluma labo ngomusa.
Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
22 UJosefa wasehlala eGibhithe, yena lendlu kayise. Njalo uJosefa waphila iminyaka elikhulu letshumi.
Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
23 UJosefa wasebona abantwana bakaEfrayimi abesizukulwana sesithathu; labantwana bakaMakiri indodana kaManase bazalelwa emadolweni kaJosefa.
ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
24 UJosefa wasesithi kubafowabo: Ngiyafa, kodwa uNkulunkulu uzalihambela isibili, alenyuse kulelilizwe alise elizweni alifungela oAbrahama, uIsaka loJakobe.
Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
25 UJosefa wafungisa amadodana kaIsrayeli esithi: UNkulunkulu uzalihambela isibili, njalo lizakwenyusa amathambo ami asuke lapha.
Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
26 UJosefa wasesifa, eleminyaka elikhulu letshumi; basebemqhola ngomuthi, wafakwa ebhokisini eGibhithe.
Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.

< UGenesisi 50 >