< UGenesisi 41 >

1 Kwasekusithi ekupheleni kweminyaka emibili egcweleyo uFaro waphupha; khangela-ke, emi emfuleni.
Patapita zaka ziwiri zathunthu, Farao analota atayimirira mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo,
2 Khangela-ke, emfuleni kwakhuphuka amankomokazi ayisikhombisa, ekhangeleka emahle, enonile enyameni; adla emihlangeni.
ndipo anangoona ngʼombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zooneka bwino ndi zonenepa zikutuluka mu mtsinje muja ndi kuyamba kudya msipu wa mu mawango.
3 Khangela-ke, amanye amankomokazi ayisikhombisa akhuphuka emfuleni emva kwawo, ekhangeleka kubi, ecakile enyameni; ema eduze lamankomokazi ekhunjini lomfula.
Kenaka ngʼombe zina zazikazi zisanu ndi ziwiri zosaoneka bwino ndi zowonda zinatulukanso mu mtsinje wa Nailo ndipo zinayimirira pambali pa zina zija zimene zinali mʼmphepete mwa mtsinje uja.
4 Amankomokazi akhangeleka kubi acakileyo enyameni adla amankomokazi akhangeleka kuhle anonileyo. UFaro wasephaphama.
Ndipo ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya ngʼombe zonenepa zija. Kenaka Farao anadzidzimuka.
5 Walala futhi, waphupha ngokwesibili; khangela-ke, kwakhahlela izikhwebu eziyisikhombisa ehlangeni linye, ezigcweleyo zilungile.
Posakhalitsa anagonanso ndipo analota kachiwiri: Analota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi labwino zitabala pa phata limodzi.
6 Khangela-ke, izikhwebu eziyisikhombisa ezicakileyo, zihangulwe ngumoya wempumalanga, zakhahlela emva kwazo.
Kenaka ngala zina zisanu ndi ziwiri zinaphuka. Izi zinali zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
7 Izikhwebu ezicakileyo zaginya izikhwebu ezipheleleyo ezigcweleyo. UFaro wasephaphama, khangela-ke, kwakuliphupho.
Ngala zowonda zija zinameza ngala zathanzi ndi zonenepa zija. Farao anadzidzimuka ndipo anaona kuti anali maloto chabe.
8 Kwasekusithi ekuseni umoya wakhe wakhathazeka; wathumela wabiza izangoma zonke zeGibhithe lazo zonke izazi zayo. UFaro wazilandisela iphupho lakhe; kodwa kwakungekho ongamchasisela wona uFaro.
Mmawa, Farao anavutika mu mtima kotero anayitanitsa amatsenga ndi anzeru onse a mu Igupto. Iwo atabwera, iye anawawuza maloto ake, koma panalibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kutanthauzira malotowo kwa Farao.
9 Induna yabaphathinkezo yasikhuluma kuFaro isithi: Lamuhla ngiyakhumbula amacala ami.
Ndipo mkulu wa operekera zakumwa anati kwa Farao, “Lero ndakumbukira kulephera kwanga.
10 UFaro wazithukuthelela inceku zakhe, wanginikela esitokisini, endlini yenduna yabalindi, mina lenduna yabaphekizinkwa;
Paja nthawi ina Farao anapsera mtima antchito akefe, ndipo anatitsekera (ine ndi mkulu wa ophika buledi) mʼndende, mʼnyumba ya mkulu wa alonda.
11 njalo saphupha iphupho ngabusuku bunye, mina layo. Saphupha, ngamunye njengengcazelo yephupho lakhe.
Tsiku lina tonse awiri tinalota maloto, ndipo loto lililonse linali ndi tanthauzo lake.
12 Kwakukhona lapho kanye lathi ijaha umHebheru, inceku yenduna yabalindi; sayilandisela yasichasisela amaphupho ethu, yachasisa ngamunye njengephupho lakhe.
Tsono momwemo munali mnyamata wina Wachihebri, wantchito wa mkulu wa alonda. Ife tinamufotokozera maloto athu, ndipo anatitanthauzira malotowo. Munthu aliyense anamupatsa tanthauzo la loto lake.
13 Kwasekusithi njengokusichasisela kwayo kwaba njalo; mina wangibuyisela esikhundleni sami, yena wamlengisa.
Ndipo zinthu zinachitikadi monga mmene anatitanthauzira. Ine anandibwezera pa ntchito yanga ndipo winayo anapachikidwa.”
14 UFaro wasethumela wabiza uJosefa; bamkhupha emgodini ngokuphangisa; esephucile wafaka ezinye izigqoko, wangena kuFaro.
Choncho Farao anamuyitanitsa Yosefe, ndipo mofulumira anabwera naye kuchokera mʼdzenje muja. Ndipo atameta, ndi kusintha zovala, anapita kwa Farao.
15 UFaro wasesithi kuJosefa: Ngiphuphile iphupho, kodwa kakho olichasisayo; njalo mina ngizwile ngawe ukuthi: Usizwa iphupho, uyalichasisa.
Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota maloto ndipo palibe amene watha kunditanthauzira. Tsono ndawuzidwa kuti iwe ukamva loto umadziwanso kulimasulira.”
16 UJosefa wasemphendula uFaro esithi: Kakukho kimi. UNkulunkulu uzaphendula impilakahle kaFaro.
Yosefe anamuyankha Farao kuti, “Sindingathe koma Mulungu apereka yankho limene Farao akufuna.”
17 UFaro wasekhuluma kuJosefa wathi: Ephutsheni lami, khangela, ngangimi ekhunjini lomfula;
Ndipo Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota nditayimirira mʼmphepete mwa mtsinje wa Nailo,
18 njalo khangela, kwakhuphuka emfuleni amankomokazi ayisikhombisa, anonileyo enyameni, akhangeleka emahle, adla emihlangeni.
ndipo ngʼombe zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zooneka bwino zinatuluka mu mtsinje muja ndi kumadya msipu wa mu mawango.
19 Khangela-ke, amanye amankomokazi ayisikhombisa akhuphuka emva kwawo, ayangekileyo, akhangeleka emabi kakhulu, acakileyo enyameni; angizanga ngiwabone anjengawo ngobubi elizweni lonke leGibhithe.
Kenaka, ngʼombe zina zisanu ndi ziwiri zinatuluka. Izi zinali zosaoneka bwino ndiponso zowonda ndipo sindinaonepo ngʼombe zosaoneka bwino chonchi mʼdziko lonse la Igupto.
20 Kwathi amankomokazi acakileyo lamabi adla amankomokazi ayisikhombisa okuqala anonileyo.
Ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya zisanu ndi ziwiri zonenepa zimene zinatuluka poyamba zija.
21 Lapho esengene esiswini sawo, kakubonakalanga ukuthi angenile esiswini sawo, ngoba ekhangeleka kubi njengakuqala. Ngasengiphaphama.
Koma ngakhale ngʼombezi zinadya zinazo, palibe amene akanatha kuzindikira kuti zinatero popeza zinali zosaonekabe bwino monga poyamba. Ndipo ndinadzidzimuka.
22 Ngasengibona ephutsheni lami, khangela-ke, izikhwebu eziyisikhombisa zikhahlela ehlangeni linye, zigcwele zilungile;
“Nditagonanso kachiwiri, ndinalota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi ndi zonenepa zitabala pa phata limodzi.
23 njalo khangela, izikhwebu eziyisikhombisa ezitshwabheneyo, ezicakileyo, ezihangulwe ngumoya wempumalanga zakhahlela emva kwazo.
Kenaka panaphukanso ngala zina zisanu ndi ziwiri zofota, zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
24 Njalo izikhwebu ezicakileyo zaginya izikhwebu eziyisikhombisa ezilungileyo. Njalo ngakulandisela izangoma; kodwa kwakungekho esangichasiselayo.
Ngala zowondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino zija. Ndinawawuza amatsenga koma palibe ndi mmodzi yemwe anatha kundimasulira.”
25 UJosefa wasesithi kuFaro: Iphupho likaFaro linye. Lokho uNkulunkulu akwenzayo, umazisile uFaro.
Ndipo Yosefe anati kwa Farao, “Maloto awiriwa ndi ofanana ndipo ali ndi tanthauzo limodzi. Mulungu waululira Farao chimene atachite.
26 Amankomokazi ayisikhombisa alungileyo ayiminyaka eyisikhombisa; lezikhwebu eziyisikhombisa ezilungileyo ziyiminyaka eyisikhombisa. Iphupho linye.
Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Kutanthauza kwa maloto nʼkumodzi.
27 Njalo amankomokazi acakileyo lamabi akhuphuka emva kwawo ayiminyaka eyisikhombisa; lezikhwebu eziyisikhombisa ezicakileyo ezihangulwe ngumoya wempumalanga zizakuba yiminyaka eyisikhombisa yendlala.
Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zowonda ndi zosaoneka bwino zimene zinatuluka pambuyozo ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zachabechabe, zowauka ndi mphepo ya kummawa zija ndi zaka zisanu ndi ziwiri za njala.
28 Le yinto engiyikhulume kuFaro ukuthi: Lokho uNkulunkulu akwenzayo, ukutshengisile kuFaro.
“Tsono ndi monga ndafotokozeramu kuti Mulungu wakuwuziranitu zimene adzachite.
29 Khangela, kuyeza iminyaka eyisikhombisa yenala enkulu elizweni lonke leGibhithe.
Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zikubwera mu dziko lonse la Igupto,
30 Kuzavela iminyaka eyisikhombisa yendlala emva kwayo; izakhohlakala-ke inala yonke elizweni leGibhithe; njalo indlala izaliqeda ilizwe.
koma zidzatsatana ndi zaka zina zisanu ndi ziwiri za njala. Chakudya chochuluka cha mu Igupto chija chidzayiwalika ndipo njalayo idzawononga dziko.
31 Njalo inala kayiyikwaziwa elizweni ngenxa yaleyondlala emva kwalokho, ngoba izakuba nzima kakhulu.
Zakudya zochuluka za mʼdzikomo zija sizidzakumbukirikanso chifukwa njala imene iti idzabwereyo idzakhala yoopsa.
32 Njalo ukuthi iphupho liphindwe kabili kuFaro, kungoba into le imisiwe nguNkulunkulu, futhi uNkulunkulu uyaphangisa ukukwenza.
Popeza kuti malotowa aperekedwa kwa inu Mfumu kawiri, ndiye kuti Mulungu watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi posachedwapa.
33 Khathesi-ke uFaro kakhangele indoda eqedisisayo lehlakaniphileyo, ayibeke phezu kwelizwe leGibhithe.
“Tsopano Farao apezeretu munthu wozindikira ndi wanzeru ndipo amuyike kukhala woyangʼanira dziko lonse la Igupto.
34 UFaro kenze lokhu, abeke ababonisi phezu kwelizwe, athathe ingxenye yesihlanu yelizwe leGibhithe eminyakeni eyisikhombisa yenala.
Asankhenso akuluakulu a mʼdziko lino. Iwowa azitenga ndi kuyika padera limodzi la magawo asanu aliwonse a zokolola za mʼdziko muno mu zaka zonse zisanu ndi ziwiri za chakudya chochuluka.
35 Kababuthe konke ukudla kwaliminyaka elungileyo ezayo, njalo kababuthelele amabele ngaphansi kwesandla sikaFaro, kube yikudla emizini, bawagcine.
Iwo asonkhanitse zakudya zonse za mʼzaka zabwino zikubwerazi. Pansi pa ulamuliro wa Farao, akuluakuluwo asonkhanitse ndi kusunga bwino tirigu mʼmizinda yonse.
36 Njalo ukudla kuzakuba yisiphala selizwe okweminyaka eyisikhombisa yendlala ezakuba khona elizweni leGibhithe, ukuze ilizwe lingabhujiswa yindlala.
Chakudya chimenechi chisungidwe kuti chidzagwiritsidwe ntchito mʼzaka zisanu ndi ziwiri za njala imene ikubwerayo mu Igupto, kuti anthu a mʼdzikoli asadzafe ndi njalayo.”
37 Njalo into le yabanhle emehlweni kaFaro lemehlweni ezinceku zakhe zonke.
Farao ndi nduna zake anagwirizana nawo malangizo a Yosefe.
38 UFaro wasesithi ezincekwini zakhe: Singamthola yini onjengaye, indoda okuyo uMoya kaNkulunkulu?
Choncho Farao anafunsa nduna zake nati, “Kodi tingathe kumupeza munthu wina ngati uyu, amene ali ndi mzimu wa Mulungu?”
39 UFaro wasesithi kuJosefa: Njengalokhu uNkulunkulu ekwazisile konke lokhu, kakho oqedisisayo lohlakaniphileyo njengawe.
Farao anati kwa Yosefe, “Pakuti Mulungu wakudziwitsa iwe zonsezi, palibe wina wodziwa zinthu ndi wanzeru ngati iwe.
40 Wena uzakuba phezu kwendlu yami, njalo emlonyeni wakho bonke abantu bami bazabuswa; kuphela esihlalweni sobukhosi ngizakuba mkhulu kulawe.
Iwe ukhala nduna yayikulu mu dziko langa ndipo anthu onse adzamvera zimene walamula. Ine ndekha ndiye amene ndidzakuposa mphamvu chifukwa ndimakhala pa mpando waufumu.”
41 UFaro wasesithi kuJosefa: Khangela, ngikubekile phezu kwelizwe lonke leGibhithe.
Choncho Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndikukuyika iwe kukhala nduna yoyangʼanira dziko lonse la Igupto.”
42 UFaro wasekhupha indandatho yakhe elophawu lwakhe esandleni sakhe, wayifaka esandleni sikaJosefa, wamgqokisa izigqoko zelembu elicolekileyo kakhulu, wamgaxa iketane legolide entanyeni yakhe.
Ndipo Farao anavula mphete ku chala chake nayiveka ku chala cha Yosefe. Anamuvekanso mkanjo wonyezimira ndi nkufu wagolide mʼkhosi mwake.
43 Wamhambisa enqoleni yesibili ayelayo; njalo bamemeza phambi kwakhe besithi: Guqani! Ngokunjalo wambeka phezu kwelizwe lonke leGibhithe.
Anamukweza Yosefe pa galeta ngati wachiwiri pa ulamuliro. Ndipo anthu anafuwula pamaso pake nati, “Mʼgwadireni!” Motero anakhala nduna yayikulu ya dziko lonse la Igupto.
44 UFaro wasesithi kuJosefa: NginguFaro; kodwa ngaphandle kwakho kakho ozaphakamisa isandla sakhe loba unyawo lwakhe elizweni lonke leGibhithe.
Kenaka Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndine Farao; tsono iwe ukapanda kulamula, palibe amene akhoza kuchita chilichonse ngakhale kuyenda kumene mʼdziko lonse la Igupto.”
45 UFaro wasebiza ibizo likaJosefa ngokuthi uZafenathi-Paneya. Wamnika uAsenathi, indodakazi kaPotifera umpristi weOni, ukuthi abe ngumkakhe. UJosefa wasephuma wadabula elizweni leGibhithe.
Farao anamupatsa Yosefe dzina lakuti Zafenati-Panea ndipo anamupatsanso Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni, kuti akhale mkazi wake. Choncho Yosefe anayendera dziko lonse la Igupto.
46 Njalo uJosefa wayeleminyaka engamatshumi amathathu mhla esima phambi kukaFaro inkosi yeGibhithe. UJosefa wasephuma esuka ebusweni bukaFaro, wadabula ilizwe lonke leGibhithe.
Yosefe anali ndi zaka 30 pamene amayamba ntchito kwa Farao, mfumu ya ku Igupto. Ndipo Yosefe anachoka pa maso pa Farao nayendera dziko lonse la Igupto.
47 Umhlaba wathela ngezandla ezigcweleyo eminyakeni eyisikhombisa yenala.
Mʼzaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zambiri zija, anthu mʼdzikomo anakolola zochuluka.
48 Waseqoqa konke ukudla kweminyaka eyisikhombisa eyayiselizweni leGibhithe, wabeka ukudla emizini; ukudla kwensimu ezingelezele lowo lalowomuzi wakubeka kuwo.
Yosefe anasonkhanitsa zakudya zonse zokololedwa mʼzaka zisanu ndi ziwiri zija ndipo anazisunga mʼmizinda. Mu mzinda uliwonse anayikamo chakudya chimene chinalimidwa mʼminda yozungulira komweko.
49 UJosefa wasebuthelela amabele njengetshebetshebe lolwandle, aba manengi kakhulu, waze wayekela ukubala, ngoba ayengelanani.
Yosefe anasunga tirigu wochuluka kwambiri ngati mchenga wa ku nyanja. Kunali tirigu wochuluka kwambiri motero kuti analeka nʼkulembera komwe.
50 Wasezalelwa uJosefa amadodana amabili, ungakafiki umnyaka wendlala, amzalela wona uAsenathi indodakazi kaPotifera umpristi weOni.
Zisanafike zaka zanjala, Yosefe anabereka ana aamuna awiri mwa Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni.
51 UJosefa wasebiza ibizo lezibulo wathi nguManase, wathi: Ngoba uNkulunkulu ungenze ukuthi ngikhohlwe konke ukuhlupheka kwami lendlu yonke kababa.
Yosefe anamutcha mwana wake woyamba, Manase popeza anati, “Mulungu wandiyiwalitsa zovuta zanga zija ndiponso banja la abambo anga.”
52 Lebizo leyesibili walibiza wathi nguEfrayimi, wathi: Ngoba uNkulunkulu ungenze ukuthi ngibe lezithelo elizweni lokuhlupheka kwami.
Mwana wachiwiri wa mwamuna anamutcha Efereimu popeza anati, “Mulungu wandipatsa ana mʼdziko la masautso anga.”
53 Kwasekuphela iminyaka eyisikhombisa yenala eyayiselizweni leGibhithe.
Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zija zinatha,
54 Kwasekuqala ukufika iminyaka eyisikhombisa yendlala, njengoba uJosefa wayetshilo. Kwasekusiba khona indlala emazweni wonke, kodwa elizweni lonke leGibhithe kwakukhona isinkwa.
ndipo zaka zisanu ndi ziwiri za njala zija zinayamba monga ananenera Yosefe. Njalayi inafika ku mayiko ena onse koma ku dziko lonse la Igupto kunali chakudya.
55 Kwathi ilizwe leGibhithe lonke selilamba, abantu bakhala ngesinkwa kuFaro. UFaro wasesithi kuwo wonke amaGibhithe: Yanini kuJosefa, lenze lokho alitshela khona.
Pamene njala ija inakwanira dziko lonse la Igupto anthu analilira Farao kuti awapatse chakudya. Koma Farao anawawuza kuti, “Pitani kwa Yosefe ndipo mukachite zimene akakuwuzeni.”
56 Kwathi sekulendlala ebusweni belizwe lonke, uJosefa wavula zonke iziphala, wathengisela amaGibhithe; indlala-ke yaba lamandla elizweni leGibhithe.
Pamene njala inafalikira dziko lonse, Yosefe anatsekula nkhokwe za zakudya namagulitsa tirigu kwa anthu a ku Igupto aja, pakuti njala inafika poyipa kwambiri mu Igupto monse.
57 Lonke ilizwe lafika eGibhithe kuJosefa ukuthenga, ngoba indlala yayilamandla emhlabeni wonke.
Anthu ankabwera ku Igupto kuchokera ku mayiko ena onse kudzagula tirigu kwa Yosefe, chifukwa njala inafika poyipa kwambiri pa dziko lonse lapansi.

< UGenesisi 41 >