< UGenesisi 40 >
1 Kwasekusithi emva kwalezizinto umphathinkezo wenkosi yeGibhithe lomphekizinkwa bona enkosini yabo, enkosini yeGibhithe.
Patapita nthawi, woperekera zakumwa ndi wopanga buledi a ku nyumba kwa mfumu ya ku Igupto analakwira mbuye wawoyo.
2 Ngakho uFaro wabathukuthelela abathenwa bakhe ababili, induna yabaphathinkezo lenduna yabaphekizinkwa.
Farao anapsa mtima ndi akuluakulu awiriwa,
3 Wazinikela esitokisini, endlini yenduna yabalindi, entolongweni, indawo lapho uJosefa ayebotshelwe khona.
ndipo anakawatsekera mʼndende, nakawayika mʼmanja mwa mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa mfumu kuja, mʼndende momwe Yosefe ankasungidwamo.
4 Induna yabalindi yasimlaya uJosefa ukuba lazo, wazisebenzela; njalo zaba lensuku esitokisini.
Mkulu wa alonda aja anawapereka mʼmanja mwa Yosefe, ndipo iye anawasamalira. Iwo anakhala mʼndendemo kwa kanthawi.
5 Zombili zaseziphupha amaphupho, ngamunye iphupho lakhe, ngabusuku bunye, ngamunye njengengcazelo yephupho lakhe, umphathinkezo lomphekizinkwa ababengabenkosi yeGibhithe ababebotshiwe entolongweni.
Usiku wina, aliyense wa anthu awiriwa, wopereka zakumwa pamodzi ndi wopanga buledi wa ku nyumba ya mfumu ya ku Igupto aja, amene ankasungidwa mʼndende, analota maloto. Malotowo anali ndi tanthauzo lake.
6 UJosefa wasengena kibo ekuseni, wababona, khangela-ke, benyukumele.
Mmawa wake, Yosefe atabwera, anaona kuti nkhope zawo zinali zakugwa.
7 Wasebabuza abathenwa bakaFaro ababelaye esitokisini endlini yenkosi yakhe, esithi: Kungani ubuso benu budanile lamuhla?
Choncho anafunsa akuluakulu a kwa Farao amene anali naye mʼndende muja kuti, “Bwanji nkhope zanu zili zachisoni lero?”
8 Basebesithi kuye: Siphuphile iphupho, njalo kakho umchasisi walo. UJosefa wasesithi kubo: Ingcazelo kayisizo zikaNkulunkulu yini? Ake lingilandisele wona.
Iwo anayankha, “Tonse awiri talota maloto, koma palibe wotitanthauzira malotowo.” Pamenepo Yosefe anawawuza kuti, “Ndi Mulungu yekha amene amapereka matanthauzo a maloto. Uzeni ine maloto anu.”
9 Induna yabaphathinkezo yalandisa iphupho layo kuJosefa, yathi kuye: Ephutsheni lami, khangela-ke, kwakukhona ivini phambi kwami;
Choncho mkulu wa operekera zakumwa uja anamuwuza Yosefe maloto ake. Anati, “Mʼmaloto anga ndinaona mtengo wa mpesa,
10 evinini-ke kwakukhona ingatsha ezintathu; njalo kwakungathi liyahluma, impoko zalo zaphuma, amahlukuzo alo athela izithelo zevini ezivuthiweyo.
unali ndi nthambi zitatu. Mpesawo utangophukira, unachita maluwa ndipo maphava ake anabereka mphesa zakupsa.
11 Njalo inkezo kaFaro yayisesandleni sami; ngasengithatha izithelo zevini, ngazikhamela enkezweni kaFaro, nganika inkezo esandleni sikaFaro.
Chikho cha Farao chinali mʼmanja mwanga, ndipo ndinatenga mphesa, kupsinyira mu chikho cha Farao ndi kuchipereka mʼmanja mwake.”
12 UJosefa wasesithi kuyo: Le yingcazelo yalo. Ingatsha ezintathu ziyizinsuku ezintathu;
Yosefe anati kwa iye, “Tanthauzo lake ndi ili: Nthambi zitatuzo ndi masiku atatu.
13 kusesephakathi kwensuku ezintathu uFaro uzaphakamisa ikhanda lakho, akubuyisele esikhundleni sakho; njalo uzanika inkezo kaFaro esandleni sakhe, njengendlela yakuqala lapho wawungumphathinkezo wakhe.
Pakangopita masiku atatu, Farao adzakutulutsa muno. Udzaperekera zakumwa kwa Farao monga momwe umachitira poyamba.
14 Kodwa ungikhumbule lawe, lapho uhlezi kuhle, ake ungenzele umusa, ungibike kuFaro, ungikhuphe kulindlu.
Koma zako zikakuyendera bwino, udzandikumbukire ndi kundikomera mtima. Chonde ukandipepesere kwa Farao kuti anditulutse muno.
15 Ngoba ngebiwa lokwebiwa elizweni lamaHebheru, lalapha futhi kangenzanga lutho ukuze bangifake emgodini.
Popezatu ine anangochita mondiba kubwera nane kuno kuchokera ku dziko la Ahebri, ndipo ngakhale kunoko, ine sindinalakwe kali konse kuti ndizipezeka mʼdzenje muno.”
16 Lapho induna yabaphekizinkwa ibona ukuthi uchasise kuhle, yathi kuJosefa: Lami bengisephutsheni; khangela-ke, bekukhona izitsha ezintathu zilezinkwa ezimhlophe ekhanda lami;
Mkulu wa opanga buledi ataona kuti Yosefe wapereka tanthauzo labwino, anati kwa Yosefe, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi.
17 njalo esitsheni esingaphezulu kwakukhona okokudla konke kukaFaro, umsebenzi obhakiweyo; njalo inyoni zakudla lokho esitsheni esisekhanda lami.
Mu nsengwa yapamwamba munali zakudya zamitundumitundu za Farao, koma mbalame zimadya zakudyazo.”
18 UJosefa wasephendula wathi: Le yingcazelo yalo. Izitsha ezintathu ziyizinsuku ezintathu;
Yosefe anati, “Tanthauzo lake ndi ili: nsengwa zitatuzo ndi masiku atatu.
19 kusesephakathi kwensuku ezintathu uFaro uzaphakamisa ikhanda lakho lisuke kuwe, akulengise esihlahleni; inyoni zizakudla inyama yakho ziyisuse kuwe.
Pakangotha masiku atatu Farao adzakutulutsa muno koma adzakupachika. Ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.”
20 Kwasekusithi ngosuku lwesithathu, usuku lokuzalwa kukaFaro, wenzela inceku zakhe zonke idili; waphakamisa ikhanda lenduna yabaphathinkezo lekhanda lenduna yabaphekizinkwa phakathi kwenceku zakhe.
Tsono tsiku lachitatulo linali lokumbukira kubadwa kwa Farao, ndipo anawakonzera phwando akuluakulu ake onse. Anatulutsa mʼndende mkulu wa operekera zakumwa ndi mkulu wa ophika buledi, ndipo anawayimiritsa pamaso pa nduna zake.
21 Wayibuyisela induna yabaphathinkezo ekuphatheni kwayo inkezo; yasinika inkezo esandleni sikaFaro.
Tsono Farao anamubwezera mkulu wa operekera zakumwa uja pa udindo wake, kotero kuti anayamba kuperekeranso zakumwa kwa Farao,
22 Kodwa wayilengisa induna yabaphekizinkwa, njengoba uJosefa ezichasisele.
koma mkulu wa ophika buledi anamupachika, mofanana ndi mmene Yosefe anatanthauzira maloto.
23 Kodwa induna yabaphathinkezo kayimkhumbulanga uJosefa, kodwa yamkhohlwa.
Koma mkulu wa operekera zakumwa uja sanamukumbukire Yosefe ndipo anamuyiwaliratu.