< UGenesisi 39 >

1 UJosefa wasesehliselwa eGibhithe; njalo uPotifa, umphathi kaFaro, induna yabalindi, indoda engumGibhithe, wamthenga esandleni samaIshmayeli, ababemehlisele khona.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 Njalo iNkosi yayiloJosefa, waze waba ngumuntu ophumelelayo; wayesendlini yenkosi yakhe, umGibhithe.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 Inkosi yakhe yasibona ukuthi iNkosi ilaye, lokuthi konke akwenzayo iNkosi yakuphumelelisa esandleni sakhe.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 UJosefa wasethola umusa emehlweni ayo, wayisebenzela; njalo yamenza waba ngumphathi wendlu yayo, lakho konke eyayilakho yakunikela esandleni sakhe.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 Kwasekusithi kusukela esikhathini eyamenza ngaso umphathi wendlu yayo, lakho konke eyayilakho, iNkosi yabusisa indlu yomGibhithe ngenxa kaJosefa; lesibusiso seNkosi saba phezu kwakho konke eyayilakho, endlini lensimini.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Yasitshiya konke eyayilakho esandleni sikaJosefa; yayingazi lutho lwayo, ngaphandle kokudla eyayikudla. Futhi uJosefa wayemuhle ngesimo, ekhangeleka kuhle.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 Kwasekusithi emva kwalezizinto, inkosikazi yenkosi yakhe yaphakamisela amehlo ayo kuJosefa; yathi: Lala lami.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Kodwa wala, wathi enkosikazini yenkosi yakhe: Khangela, inkosi yami kayikwazi okulami endlini, njalo konke elakho ikunikela esandleni sami;
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 kakho omkhulu kulami endlini le; njalo kayingigodlelanga lutho, ngaphandle kwakho, ngalokhu ukuthi ungumkayo; njalo ngingenza njani lobububi obukhulu, ngone kuNkulunkulu?
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Kwasekusithi ekukhulumeni kwakhe kuJosefa insuku ngensuku, kazange amlalele, ukulala laye, lokuba laye.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Kwasekusithi ngosuku oluthile wangena endlini ukuyakwenza umsebenzi wakhe, njalo kwakungekho owamadoda endlu lapho endlini,
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 yasimbamba ngesembatho sakhe isithi: Lala lami. Kodwa watshiya isembatho sakhe esandleni sayo, wabaleka, waphumela phandle.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 Kwasekusithi isibonile ukuthi utshiyile isembatho sakhe esandleni sayo, wabalekela phandle,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 yabiza amadoda endlu yayo, yakhuluma kuwo isithi: Bonani, usilethele indoda engumHebheru ukudlala ngathi; uze kimi ukuze alale lami, ngamemeza ngelizwi elikhulu;
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 kwasekusithi esezwile ukuthi ngiphakamise ilizwi lami ngakhala, watshiya isembatho sakhe eceleni kwami, wabaleka, waphumela phandle.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Yasisibeka isembatho sakhe eceleni kwayo, yaze yafika inkosi yakhe ekhaya.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 Njalo yakhuluma kuyo njengalamazwi isithi: Inceku engumHebheru, osilethele yona, izile kimi ukuze idlale ngami;
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 kwasekusithi sengiphakamise ilizwi lami ngakhala, yatshiya isembatho sayo eceleni kwami, yabalekela phandle.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 Kwasekusithi inkosi yakhe isizwe amazwi omkayo, ewakhulume kuyo, esithi: Njengalamazwi inceku yakho yenze kimi, ulaka lwayo lwavutha.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 Inkosi kaJosefa yasimthatha yamfaka entolongweni, indawo lapho izibotshwa zenkosi ezazibotshelwa khona; wasesiba lapho entolongweni.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Kodwa iNkosi yaba loJosefa, yelulela umusa kuye, yasimupha umusa emehlweni enduna yentolongo.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 Induna yentolongo yanikela-ke esandleni sikaJosefa zonke izibotshwa ezazisentolongweni; lakho konke ezazikwenza lapho, wayengumenzi.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Induna yentolongo kayisakhangelanga lutho olwalusesandleni sakhe, ngoba iNkosi yayilaye; lalokho akwenzayo iNkosi yakuphumelelisa.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< UGenesisi 39 >