< UGenesisi 33 >

1 UJakobe wasephakamisa amehlo akhe, wabona, khangela-ke, uEsawu esiza lamadoda angamakhulu amane kanye laye. Wasesehlukanisa abantwana phakathi kukaLeya loRasheli lencekukazi zombili.
Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
2 Wasebeka izincekukazi labantwana bazo ngaphambili, loLeya labantwana bakhe ngemuva, loRasheli loJosefa ekucineni.
Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
3 Yena uqobo wasesedlula phambi kwabo, wakhothamela emhlabathini kasikhombisa waze wafika eduze lomnewabo.
Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
4 UEsawu wasegijima ukumhlangabeza, wamgona, wawela entanyeni yakhe, wamanga; basebekhala inyembezi.
Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
5 Wasephakamisa amehlo akhe wabona abesifazana labantwana, wathi: Ngobani laba olabo? Wasesithi: Abantwana uNkulunkulu ngomusa ayinike bona inceku yakho.
Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
6 Zasezisondela incekukazi, zona labantwana bazo, bakhothama.
Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
7 Laye uLeya wasesondela labantwana bakhe, bakhothama; emva kwalokho uJosefa wasondela loRasheli, bakhothama.
Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
8 Wasesithi: Uqondeni ngaleli iqembu lonke engihlangene lalo? Wasesithi: Ukuthola umusa emehlweni enkosi yami.
Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
9 UEsawu wasesithi: Ngilokunengi, mfowethu; okwakho kakube ngokwakho.
Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
10 UJakobe wasesithi: Hayi bo! Uba khathesi ngithole umusa emehlweni akho, yemukela isipho sami esivela esandleni sami; ngoba yikho ngibone ubuso bakho kunjengokuthi ngibone ubuso bukaNkulunkulu, njalo wathokoza ngami.
Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
11 Ake wemukele isipho sami esilethwa kuwe; ngoba uNkulunkulu ungiphile ngomusa, njalo ngoba ngilakho konke. Wasemncenga, waze wasemukela.
Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
12 Wasesithi: Asisuke sihambe, njalo ngizahamba phambi kwakho.
Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
13 Kodwa wathi kuye: Inkosi yami iyazi ukuthi abantwana babuthakathaka, lokuthi izimvu lezinkomo engilazo ziyenyisa; uba-ke beziqhuba ngamandla usuku olulodwa, umhlambi wonke uzakufa.
Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
14 Inkosi yami ake yedlule phambi kwenceku yayo; mina-ke ngizaqhubeka kuhle kuhle, ngokuhamba komsebenzi ophambi kwami, langokuhamba kwabantwana, ngize ngifike enkosini yami eSeyiri.
Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
15 UEsawu wasesithi: Ake ngibeke kuwe abanye babantu abalami. Wasesithi: Kungani lokhu? Kangithole umusa emehlweni enkosi yami.
Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
16 UEsawu wasebuyela ngendlela yakhe ngalolosuku, waya eSeyiri.
Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
17 Njalo uJakobe waqhubeka waya eSukothi, wazakhela indlu, wenzela izifuyo zakhe izibaya ezilophahla; ngakho wayitha ibizo lendawo iSukothi.
Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
18 UJakobe wasefika evikelekile emzini weShekema, oselizweni leKhanani, ekuveleni kwakhe ePadani-Arama; wamisa inkamba phambi komuzi.
Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
19 Njalo ingxenye yesiqinti amisela kuyo amathente akhe wayithenga esandleni samadodana kaHamori uyise kaShekema, ngezinhlamvu zemali ezilikhulu.
Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
20 Wasemisa khona ilathi, walibiza ngokuthi yiEli-Elohe-Israyeli.
Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.

< UGenesisi 33 >