< UGenesisi 28 >
1 UIsaka wasebiza uJakobe, wambusisa, wamlaya wathi kuye: Ungathathi umfazi kumadodakazi eKhanani.
Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
2 Sukuma uye ePadani-Arama, endlini kaBethuweli uyise kanyoko, uzithathele khona umfazi kumadodakazi kaLabani umalumakho.
Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
3 Njalo uNkulunkulu uSomandla akubusise, akwenze ube lenzalo akwandise, ukuze ube ngumbuthano wezizwe;
Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
4 abesekupha isibusiso sikaAbrahama, kuwe lenzalweni yakho kanye lawe, ukuze udle ilifa lelizwe lapho ohlala khona njengowezizwe, uNkulunkulu alinika uAbrahama.
Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
5 UIsaka wasethuma uJakobe waya ePadani-Arama kuLabani indodana kaBethuweli umSiriya, umfowabo kaRebeka unina kaJakobe loEsawu.
Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
6 UEsawu wasebona ukuthi uIsaka umbusisile uJakobe, wamthuma ePadani-Arama ukuze azithathele khona umfazi, lapho embusisa wamlaya esithi: Ungathathi umfazi kumadodakazi eKhanani;
Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
7 lokuthi uJakobe walalela oyise lonina, waya ePadani-Arama.
Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
8 UEsawu wasebona ukuthi amadodakazi eKhanani ayemabi emehlweni kaIsaka uyise.
Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
9 Ngakho uEsawu waya kuIshmayeli, wazithathela uMahalathi indodakazi kaIshmayeli, indodana kaAbrahama, udadewabo kaNebayothi, abe ngumkakhe phezu kwabafazi ayelabo.
anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
10 UJakobe wasephuma eBherishebha waya eHarani.
Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
11 Wafika endaweni, achitha khona ubusuku ngoba ilanga lalitshonile. Wasethatha ilitshe ematsheni aleyondawo, wenza umqamelo wakhe, walala kuleyondawo.
Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
12 Waphupha, khangela-ke, ilele limisiwe emhlabeni, isihloko salo sifinyelela emazulwini, khangela-ke, ingilosi zikaNkulunkulu zisenyuka zisehla kulo.
Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
13 Khangela-ke, iNkosi yema phezu kwalo, yathi: NgiyiNkosi uNkulunkulu kaAbrahama uyihlo loNkulunkulu kaIsaka; ilizwe olele kulo, ngizakunika lona, lenzalo yakho;
Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
14 njalo inzalo yakho izakuba ngangothuli lomhlaba, uzasabalalela entshonalanga lempumalanga lenyakatho leningizimu; njalo zizabusiswa kuwe zonke insendo zomhlaba, lasenzalweni yakho.
Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
15 Khangela-ke, ngilawe, ngizakulondoloza kuzo zonke indawo lapha oya khona, ngikubuyise kulelilizwe; ngoba kangiyikukutshiya ngize ngikwenze lokho engikhulume ngakho kuwe.
Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
16 Kwathi uJakobe ephaphama ebuthongweni bakhe, wathi: Isibili iNkosi ikulindawo, mina-ke bengingakwazi.
Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
17 Wasesesaba wathi: Yesabeka kangakanani lindawo! Kayisilutho ngaphandle kokuthi yindlu kaNkulunkulu, laleli lisango lamazulu.
Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
18 UJakobe wasevuka ekuseni kakhulu, wathatha ilitshe alenza laba ngumqamelo wakhe, walimisa laba yinsika, wathela amagcobo phezu kwesihloko salo.
Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
19 Wasebiza ibizo laleyondawo iBhetheli; kodwa-ke kuqala ibizo lomuzi laliyiLuzi.
Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
20 UJakobe wasethembisa isithembiso esithi: Uba uNkulunkulu ezakuba lami, angilondoloze kulindlela engiyihambayo, angiphe isinkwa sokudla, lesembatho sokwembatha,
Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
21 njalo ngibuyele ngokuthula endlini kababa, khona iNkosi izakuba nguNkulunkulu wami,
ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
22 lelitshe leli engilimise ukuthi libe yinsika lizakuba yindlu kaNkulunkulu; kukho konke ozangipha khona, isibili ngizakunika okwetshumi.
ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”