< UGenesisi 24 >
1 UAbrahama wayesemdala eselezinsuku ezinengi; leNkosi yayimbusisile kukho konke.
Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
2 UAbrahama wasesithi encekwini yakhe, endala yendlu yakhe, ebusa phezu kwakho konke alakho: Ake ubeke isandla sakho ngaphansi kwethangazi lami,
Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
3 ukuze ngikufungise ngeNkosi, uNkulunkulu wamazulu loNkulunkulu womhlaba, ukuthi kawuyikuyithathela indodana yami umfazi emadodakazini amaKhanani, engihlala phakathi kwawo;
Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
4 kodwa uzakuya elizweni lakithi lezihlotsheni zami, uyithathele umfazi indodana yami uIsaka.
koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
5 Inceku yasisithi kuye: Mhlawumbe owesifazana angafuni ukungilandela kulelilizwe, ngingayibuyisela lokuyibuyisela yini indodana yakho elizweni owaphuma kulo?
Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
6 UAbrahama wasesithi kuye: Qaphela ukuthi ungayibuyiseli khona indodana yami.
Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
7 INkosi, uNkulunkulu wamazulu, eyangithatha endlini kababa lelizweni lokuzalwa kwami, eyakhuluma kimi, eyafunga kimi isithi: Ngizalinika inzalo yakho lelilizwe; yona izathuma ingilosi yayo phambi kwakho, ukuze uyithathele khona umfazi indodana yami.
Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
8 Kodwa uba owesifazana engafuni ukukulandela, uzakuba ukhululekile kulesisifungo sami; kuphela ungayibuyiseli indodana yami khona.
Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
9 Inceku yasibeka isandla sayo ngaphansi kwethangazi likaAbrahama inkosi yayo, yafunga kuye ngaloludaba.
Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
10 Njalo inceku yasithatha amakamela alitshumi kuwo amakamela enkosi yayo, yahamba, lakho konke okuhle kwenkosi yayo kwakusesandleni sayo, yasisukuma yaya eMesopotamiya emzini kaNahori.
Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
11 Yasiguqisa amakamela ngaphandle komuzi emthonjeni wamanzi ngesikhathi santambama, ngesikhathi sokuphuma kwabakhi bamanzi besifazana.
Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
12 Yasisithi: Nkosi, Nkulunkulu wenkosi yami uAbrahama, ake ungiphumelelise lamuhla, uyenzele umusa inkosi yami uAbrahama.
Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
13 Khangela, ngimi emthonjeni wamanzi, kuphuma amadodakazi amadoda omuzi ukukha amanzi.
Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
14 Njalo kuzakuthi intombazana engizakuthi kuyo: Ake ukhothamise imbiza yakho ukuze nginathe, ibisisithi: Natha, lamakamela akho ngizawanathisa; yiyo oyimisele inceku yakho uIsaka; ngalokho-ke ngizakwazi ukuthi uyenzele umusa inkosi yami.
Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
15 Kwasekusithi ingakaqedi ukukhuluma, khangela-ke, uRebeka waphuma, owazalelwa uBethuweli indodana kaMilka, umkaNahori umfowabo kaAbrahama, njalo elembiza ehlombe lakhe.
Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
16 Njalo inkazana yayikhangeleka kuhle kakhulu, intombi emsulwa, okungelandoda eyaziyo; yasisehlela emthonjeni, yagcwalisa imbiza yayo, yenyuka.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
17 Inceku yasigijima ukuyihlangabeza yathi: Ake unginathise amanzi amalutshwana embizeni yakho.
Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
18 Yasisithi: Natha, nkosi yami. Yaphangisa yehlisela imbiza yayo esandleni sayo, yayinathisa.
Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
19 Isiqedile ukuyinathisa yathi: Ngizakhelela lamakamela akho aze aqede ukunatha.
Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
20 Yasiphangisa yathululela isigxingi sayo emkolweni wokunathela, yabuya yagijimela emthonjeni ukuyakukha, yakhelelela amakamela ayo wonke.
Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
21 Indoda yasiyikhangelisisa ithule ukuze yazi ukuthi iNkosi iyiphumelelisile indlela yayo kumbe hatshi.
Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
22 Kwasekusithi amakamela eseqedile ukunatha, indoda yasithatha icici legolide, osisindo salo sasiyingxenye yeshekeli, lamasongo amabili ezandleni zayo, isisindo sawo saba ngamashekeli alitshumi egolide.
Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
23 Yasisithi: Uyindodakazi kabani? Ake utsho. Kukhona indawo yethu yini endlini kayihlo ukuthi silale?
Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
24 Yasisithi kuyo: Ngiyindodakazi kaBethuweli indodana kaMilka owayizalela uNahori.
Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
25 Yathi kuyo futhi: Silakho konke amahlanga lokudla kwezinyamazana okunengi, lendawo yokulala.
Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
26 Indoda yasikhothama, yakhonza iNkosi,
Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
27 yasisithi: Ibusisiwe iNkosi, uNkulunkulu wenkosi yami uAbrahama, engayekelanga umusa wayo lobuqotho bayo enkosini yami; mina-ke, ngisendleleni, iNkosi ingikhokhelele endlini yabafowabo benkosi yami.
nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
28 Intombi yasigijima, yazisa abendlu kanina ngalezizinto.
Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
29 Njalo uRebeka wayelomnewabo obizo lakhe lalinguLabani; uLabani wasegijimela phandle endodeni emthonjeni.
Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
30 Kwasekusithi esebonile icici lamasongo ezandleni zikadadewabo, esezwile amazwi kaRebeka udadewabo okuthi: Itsho njalo indoda kimi; wasesiya endodeni, khangela-ke, yayimi ngasemakameleni emthonjeni.
Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
31 Wasesithi: Ngena wena obusisiweyo weNkosi; umeleni ngaphandle? Ngoba mina sengilungisile indlu lendawo yamakamela.
Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
32 Indoda yasisiza endlini, yakhulula amakamela; wasenika amakamela amahlanga lokudla kwenyamazana, lamanzi okugeza inyawo zayo lenyawo zamadoda ayelayo.
Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
33 Kwasekubekwa ukudla phambi kwayo; kodwa yathi: Kangiyikudla ngize ngikhulume indaba zami. Wasesithi: Khuluma.
Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
34 Yasisithi: Ngiyinceku kaAbrahama.
Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
35 Futhi iNkosi iyibusisile kakhulu inkosi yami, yaze yaba nkulu. Yayinika izimvu lezinkomo, lesiliva legolide, lezinceku lezincekukazi, lamakamela labobabhemi.
Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
36 Njalo uSara inkosikazi yenkosi yami uyizalele inkosi yami indodana emva kokuba esemdala; yasiyinika konke elakho.
Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
37 Inkosi yami yasingifungisa isithi: Ungayithatheli indodana yami umfazi kumadodakazi amaKhanani, engihlala elizweni lawo;
Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
38 kodwa uzakuya endlini kababa lezihlotsheni zami, ubusuyithathela indodana yami umfazi.
koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
39 Ngasengisithi enkosini yami: Mhlawumbe owesifazana kayikungilandela.
“Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
40 Yasisithi kimi: INkosi, engihamba phambi kwayo, izathuma ingilosi yayo lawe, izaphumelelisa indlela yakho, njalo uzayithathela indodana yami umfazi ezihlotsheni zami lendlini kababa.
“Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
41 Emva kwalokho uzakhululeka esifungweni sami uba uye ezihlotsheni zami njalo uba bengakuniki yena, uzakhululeka-ke esifungweni sami.
Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
42 Kuthe ngifika emthonjeni lamuhla, ngathi: Nkosi, Nkulunkulu wenkosi yami uAbrahama, uba-ke uphumelelisa indlela yami, engihamba ngayo;
“Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
43 khangela, ngimi emthonjeni wamanzi; njalo kakuthi intombi ezaphuma ukukha lengizakuthi kuyo: Ake unginathise amanzi amalutshwana esigxingini sakho;
taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
44 ibisisithi kimi: Natha lawe, futhi ngizakhelelela lamakamela akho; kayibe nguye owesifazana iNkosi emmisele indodana yenkosi yami.
ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
45 Ngingakaqedi ukukhuluma enhliziyweni yami, khangela-ke, uRebeka waphuma lesigxingi sisehlombe lakhe; wehlela emthonjeni, wakha. Ngasengisithi kuye: Akunginathise.
“Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
46 Wasephangisa, wethula isigxingi kuye wathi: Natha, futhi ngizanathisa lamakamela akho. Ngasenginatha, wasenathisa lamakamela.
“Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
47 Ngasengimbuza ngathi: Uyindodakazi kabani? Wasesithi: Indodakazi kaBethuweli, indodana kaNahori uMilka amzalela yona; ngasengifaka icici emakhaleni akhe lamasongo ezandleni zakhe.
“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
48 Ngasengikhothama, ngakhonza iNkosi, ngabusisa iNkosi uNkulunkulu wenkosi yami uAbrahama, engikhokhele endleleni elungileyo ukuthi indodakazi yomfowabo wenkosi yami ngiyithathele indodana yayo.
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
49 Khathesi-ke uba lizayenzela inkosi yami umusa lobuqotho, ngitshelani; uba-ke kungenjalo, ngitshelani, ukuze ngiphendukele ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo.
Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
50 Khona oLabani loBethuweli baphendula, bathi: Le into ivela eNkosini; kasilakutsho lutho kuwe, olubi kumbe oluhle.
Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
51 Khangela, uRebeka uphambi kwakho; mthathe uhambe, ukuze abe ngumkandodana yenkosi yakho, njengoba iNkosi ikhulumile.
Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
52 Kwasekusithi inceku kaAbrahama isizwile amazwi abo yakhothamela emhlabathini phambi kweNkosi.
Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
53 Inceku yasikhupha imiceciso yesiliva, lemiceciso yegolide, lezembatho, yakunika uRebeka, yabanika lomnewabo lonina impahla eziligugu.
Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
54 Basebesidla banatha, yona lamadoda ayelayo, balala; bavuka ekuseni, yasisithi: Ngiyekelani ngiye enkosini yami.
Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
55 Kodwa umnewabo lonina bathi: Kayihlale lathi intombazana izinsuku loba ezilitshumi, emva kwalokho ihambe.
Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
56 Yasisithi kubo: Lingangibambeleli, lokhu iNkosi iphumelelisile indlela yami; ngiyekelani ngihambe ukuze ngiye enkosini yami.
Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
57 Basebesithi: Asiyibize intombi, sizwe emlonyeni wayo.
Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
58 Basebembiza uRebeka, bathi kuye: Uzahamba lalindoda yini? Wasesithi: Ngizahamba.
Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
59 Basebemyekela ehamba uRebeka udadewabo lomlizane wakhe, lenceku kaAbrahama lamadoda ayo.
Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
60 Basebembusisa uRebeka, bathi kuye: Wena dadewethu, woba zinkulungwane zezigidi, lenzalo yakho ibe ngumnikazi wesango labayizondayo!
Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
61 URebeka wasesukuma lamantombazana akhe, bagada amakamela, balandela indoda; inceku yasimthatha uRebeka, yahamba.
Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
62 UIsaka wasefika lapho abavelela khona emthonjeni iLahayi-Royi, njalo wayehlala elizweni leningizimu.
Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
63 UIsaka wasephuma ukuyazindla ensimini sekuntambama; waphakamisa amehlo akhe wabona, khangela-ke, amakamela ayesiza.
Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
64 LoRebeka waphakamisa amehlo akhe; esembonile uIsaka waziwisa ekamelweni.
Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
65 Wasesithi encekwini: Ngubani lindoda ehamba emasimini ukusihlangabeza? Inceku yasisithi: Yinkosi yami. Wasethatha isimbombozo, wazigubuzela.
nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
66 Inceku yasilandisa kuIsaka zonke indaba ezenzileyo.
Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
67 UIsaka wasemngenisa ethenteni likaSara unina, wamthatha uRebeka, waba ngumkakhe, wamthanda. UIsaka waseduduzwa emva kokufa kukanina.
Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.