< UGenesisi 18 >

1 INkosi yasibonakala kuye ema-okhini eMamre, wathi ehlezi emnyango wethente ekutshiseni kosuku,
Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
2 wasephakamisa amehlo akhe wabona, khangela-ke amadoda amathathu emi phambi kwakhe; esewabonile wagijima ukuwahlangabeza esuka emnyango wethente, wakhothamela emhlabathini,
Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
3 wasesithi: Nkosi, uba-ke ngithole umusa emehlweni akho, ngicela ungadluli usuke encekwini yakho.
“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
4 Ake kulethwe amanzi amalutshwana, beseligeza inyawo zenu, liphumule ngaphansi kwesihlahla.
Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
5 Ngizaletha-ke ucezu lwesinkwa, beseliqinisa inhliziyo yenu, beselisedlula, ngoba yikho ledlule encekwini yenu. Asesithi: Ngokunjalo yenza njengokutsho kwakho.
Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
6 UAbrahama wasephangisa esiya ethenteni kuSara, wasesithi: Phangisa! Amaseya amathathu empuphu ecolekileyo! Xova, wenze amaqebelengwana.
Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
7 UAbrahama wasegijimela enkomeni, wathatha ithole elibuthakathaka njalo elihle, walinika ijaha; laphangisa ukulilungisa.
Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
8 Wasethatha amasi lochago, lethole abelilungisile, wakubeka phambi kwawo; wema eduze lawo ngaphansi kwesihlahla, asesidla.
Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
9 Asesithi kuye: Ungaphi uSara umkakho? Wasesithi: Khangela, ethenteni.
Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
10 Yasisithi: Isibili ngizabuya kuwe ngalesisikhathi sempilo; khangela, uSara umkakho uzakuba lendodana. USara wakuzwa esemnyango wethente elalingemva kwayo.
Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
11 UAbrahama loSara basebebadala sebelensuku ezinengi; kwasekuphelile kuSara okwendlela yabafazi.
Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
12 USara wasehlekela ngaphakathi, esithi: Sengigugile, ngingaba lenjabulo, lenkosi yami isindala yini?
Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
13 INkosi yasisithi kuAbrahama: Kungani uSara ehleka, esithi: Isibili lami ngizazala mina sengimdala yini?
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
14 Kukhona into enzima kakhulu eNkosini yini? Ngesikhathi esimisiweyo ngizabuya kuwe, ngalesisikhathi sempilo, njalo uSara uzakuba lendodana.
Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
15 USara wasephika esithi: Kangihlekanga, ngoba wayesesaba. Kodwa wathi: Hatshi, ngoba uhlekile.
Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
16 Amadoda asesukuma esuka lapho akhangela phansi eSodoma; uAbrahama wasehamba lawo ewaphelekezela.
Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
17 INkosi yasisithi: Mina ngingamfihlela uAbrahama yini engikwenzayo?
Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
18 Ngoba isibili uAbrahama uzakuba yisizwe esikhulu esilamandla; lazo zonke izizwe zomhlaba zizabusiswa kuye.
Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
19 Ngoba ngimazile, ukuze alaye abantwana bakhe lendlu yakhe emva kwakhe, besebegcina indlela yeNkosi ukuze benze ukulunga lokwahlulela, ukuze iNkosi imehlisele uAbrahama lokho ekutshoyo ngaye.
Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
20 INkosi yasisithi: Ngoba isikhalo seSodoma leGomora sikhulu, langoba isono sabo sinzima kakhulu,
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
21 ngizakwehla-ke besengibona ukuthi njengokwesikhalo sayo esesifike kimi, benzile ngokupheleleyo; kodwa uba kungenjalo ngizakwazi.
choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
22 Amadoda esefulathele lapho, asesiya eSodoma; kodwa uAbrahama wayelokhu emile phambi kweNkosi.
Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
23 UAbrahama wasesondela, wathi: Kambe uzambhubhisa lolungileyo kanye lomubi?
Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
24 Mhlawumbe kukhona abalungileyo abangamatshumi amahlanu phakathi komuzi; kambe uzabhubhisa ungaxoleli indawo ngenxa yabalungileyo abangamatshumi amahlanu abakuwo?
Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
25 Kakube khatshana lawe ukwenza into enjalo, ukubulala olungileyo kanye lomubi lokuthi olungileyo abe njengomubi; kakube khatshana lawe; umahluleli womhlaba wonke kayikwenza ukulunga yini?
Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
26 INkosi yasisithi: Uba ngithola eSodoma abalungileyo abangamatshumi amahlanu phakathi komuzi, ngizaxolela yonke indawo ngenxa yabo.
Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
27 UAbrahama wasephendula wathi: Khangela-ke, ngizimisele ukukhuluma eNkosini, lanxa ngiluthuli lomlotha.
Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
28 Mhlawumbe kuzasweleka abahlanu kubo abalungileyo abangamatshumi amahlanu; uzabhubhisa umuzi wonke ngenxa yabahlanu yini? Yasisithi: Kangiyikuwubhubhisa uba ngithola khona abangamatshumi amane lanhlanu.
bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
29 Waseqhubeka elokhu ekhuluma kuyo wathi: Mhlawumbe kuzatholwa khona abangamatshumi amane. Yasisithi: Kangiyikukwenza ngenxa yabangamatshumi amane.
Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
30 Wasesithi: Ngicela iNkosi ingathukutheli lapho ngikhuluma. Mhlawumbe kuzatholwa khona abangamatshumi amathathu. Yasisithi: Kangiyikukwenza uba ngithola khona abangamatshumi amathathu.
Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
31 Wasesithi: Khangela-ke, ngizimisele ukukhuluma eNkosini; mhlawumbe kuzatholwa khona abangamatshumi amabili. Yasisithi: Kangiyikuwubhubhisa ngenxa yabangamatshumi amabili.
Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
32 Wasesithi: Ngicela iNkosi ingathukutheli, ngizakhuluma khathesi kuphela; mhlawumbe kuzatholwa khona abalitshumi. Yasisithi: Kangiyikuwubhubhisa ngenxa yabalitshumi.
Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
33 INkosi yasihamba isiqedile ukukhuluma kuAbrahama; uAbrahama wasebuyela endaweni yakhe.
Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

< UGenesisi 18 >