< UGenesisi 17 >
1 Kwathi uAbrama eseleminyaka engamatshumi ayisificamunwemunye lesificamunwemunye iNkosi yasibonakala kuAbrama, yathi kuye: NginguNkulunkulu uSomandla; hamba phambi kwami, uphelele.
Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
2 Njalo ngizakwenza isivumelwano sami phakathi kwami lawe, ngizakwandisa kakhulukazi.
Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
3 UAbrama wasesiwa ngobuso bakhe, uNkulunkulu wasekhuluma laye, esithi:
Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
4 Mina ngokwami, khangela, isivumelwano sami silawe; futhi uzakuba nguyise wezizwe ezinengi.
“Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
5 Lebizo lakho kalisayikubizwa ngokuthi Abrama, kodwa ibizo lakho lizakuba nguAbrahama, ngoba ngikwenze uyise wexuku lezizwe.
Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
6 Ngizakwenza uzale kakhulukazi, ngizakwenza izizwe, lamakhosi azaphuma kuwe.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
7 Njalo ngizamisa isivumelwano sami phakathi kwami lawe lenzalo yakho emva kwakho ezizukulwaneni zayo, kube yisivumelwano esilaphakade, sokuthi ngibe nguNkulunkulu kuwe lakuyo inzalo yakho emva kwakho.
Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
8 Ngizanika-ke wena lenzalo yakho emva kwakho ilizwe ohlala kilo njengowezizwe, ilizwe lonke leKhanani, libe yimfuyo elaphakade; njalo ngizakuba nguNkulunkulu kibo.
Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
9 UNkulunkulu wasesithi kuAbrahama: Wena-ke uzagcina isivumelwano sami, wena lenzalo yakho emva kwakho ezizukulwaneni zayo.
Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
10 Lesi yisivumelwano sami elizasigcina phakathi kwami lani lenzalo yakho emva kwakho; sonke isilisa sisokwe kini.
Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
11 Lizasoka inyama yejwabu lenu laphambili; kuzakuba yisibonakaliso sesivumelwano phakathi kwami lani.
Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
12 Lendodana yensuku eziyisificaminwembili izasokwa phakathi kwenu, sonke isilisa ezizukulwaneni zenu, ozelwe endlini, lothengwe ngemali kuye wonke oyisizwe, ongayisuye wenzalo yakho.
Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
13 Ozelwe endlini yakho lothengwe ngemali yakho kumele asokwe. Lesivumelwano sami sizakuba senyameni yenu, sibe yisivumelwano esilaphakade.
Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
14 Lesilisa esingasokwanga, esinyama yejwabu laphambili lingasokwanga, lowomphefumulo uzaqunywa usuke esizweni sawo, weqile isivumelwano sami.
Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
15 UNkulunkulu wasesithi kuAbrahama: NgoSarayi umkakho, ungabizi ibizo lakhe uthi nguSarayi, ngoba uSara libizo lakhe.
Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
16 Njalo ngizambusisa, ngikunike indodana evela lakuye; yebo ngizambusisa abesesiba yizizwe, amakhosi ezizwe azavela kuye.
Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
17 UAbrahama wasesiwa ngobuso bakhe, wahleka, wathi enhliziyweni yakhe: Oleminyaka elikhulu uzazalelwa yini? Kambe loSara oleminyaka engamatshumi ayisificamunwemunye uzazala?
Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
18 UAbrahama wasesithi kuNkulunkulu: Kungathi uIshmayeli angaphila phambi kwakho!
Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
19 UNkulunkulu wasesithi: Hatshi, uSara umkakho uzakuzalela indodana; uzayitha ibizo uthi nguIsaka; njalo ngizamisa isivumelwano sami laye, sibe yisivumelwano esilaphakade kunzalo yakhe emva kwakhe.
Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
20 Mayelana loIshmayeli ngikuzwile-ke; khangela, ngimbusisile, njalo ngizamenza abe lenzalo, ngimandise kakhulukazi; uzazala iziphathamandla ezilitshumi lambili, njalo ngizamenza isizwe esikhulu.
Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
21 Kodwa isivumelwano sami ngizasimisa loIsaka, uSara azakuzalela yena ngalesisikhathi esimisiweyo ngomnyaka ozayo.
Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
22 Wasecina ukukhuluma laye, uNkulunkulu wenyuka esuka kuAbrahama.
Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
23 UAbrahama wasethatha uIshmayeli indodana yakhe labo bonke ababezelwe endlini yakhe labo bonke ababethengwe ngemali yakhe, sonke isilisa phakathi kwabendlu kaAbrahama, wasoka inyama yejwabu labo laphambili, ngalona lolosuku, njengalokho uNkulunkulu akutshoyo kuye.
Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
24 LoAbrahama wayeleminyaka engamatshumi ayisificamunwemunye lesificamunwemunye ekusokweni kwakhe inyama yejwabu lakhe laphambili.
Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
25 UIshmayeli-ke indodana yakhe wayeleminyaka elitshumi lantathu ekusokweni kwakhe inyama yejwabu lakhe laphambili.
ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
26 Ngalona lolosuku uAbrahama wasokwa, loIshmayeli indodana yakhe.
Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
27 Lamadoda wonke omuzi wakhe, ayezelwe endlini layethengwe ngemali kowezizwe, asokwa kanye laye.
Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.