< UGenesisi 13 >

1 UAbrama wasesenyuka eGibhithe, yena lomkakhe lakho konke ayelakho loLothi kanye laye, waya eningizimu.
Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
2 Njalo uAbrama wayenothile kakhulu, ngezifuyo, ngesiliva, langegolide.
Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
3 Wasehamba kuzinhambo zakhe esuka eningizimu, waze wafika eBhetheli, endaweni lapho ithente lakhe elalikhona kuqala, phakathi kweBhetheli leAyi;
Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
4 endaweni yelathi ayelenzile khona kuqala; uAbrama wasebiza ibizo leNkosi lapho.
ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
5 LoLothi laye, owayehamba loAbrama, wayelezimvu lezinkomo lamathente.
Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
6 Njalo ilizwe lalingebathwale ukuthi bahlale ndawonye, ngoba impahla yabo yayinengi, ukuthi babengeke bahlala ndawonye.
Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
7 Kwasekusiba khona ukuxabana phakathi kwabelusi bezifuyo zikaAbrama labelusi bezifuyo zikaLothi. Ngalesosikhathi amaKhanani lamaPerizi ayehlala elizweni.
Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
8 UAbrama wasesithi kuLothi: Ake kungabi khona ukuxabana phakathi kwami lawe, laphakathi kwabelusi bami labelusi bakho, ngoba singamadoda osendo.
Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
9 Ilizwe lonke kaliphambi kwakho yini? Yehlukana-ke lami; uba usiya kwesokhohlo, ngizakuya kwesokunene; kodwa uba kwesokunene, ngizakuya kwesokhohlo.
Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
10 ULothi wasephakamisa amehlo akhe, wabona lonke igceke leJordani ukuthi lalithelelwe kuhle lonke. INkosi ingakachithi iSodoma leGomora, lalinjengensimu yeNkosi, njengelizwe leGibhithe, nxa usiya eZowari.
Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
11 ULothi wasezikhethela lonke igceke leJordani; uLothi wasesiya empumalanga; basebezehlukanisa omunye komunye.
Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
12 UAbrama wahlala elizweni leKhanani, uLothi wasehlala emizini yemagcekeni, wamisa ithente lakhe eduze leSodoma.
Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
13 Kodwa abantu beSodoma babebabi babeyizoni phambi kweNkosi kakhulu.
Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
14 INkosi yasisithi kuAbrama emva kokuthi uLothi esehlukaniswe laye: Phakamisa-ke amehlo akho, ukhangele endaweni lapho okhona, ngasenyakatho langaseningizimu langasempumalanga langasentshonalanga,
Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
15 ngoba ilizwe lonke olibonayo ngizalinika wena, lakunzalo yakho kuze kube nininini.
Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
16 Njalo ngizakwenza inzalo yakho ibe njengothuli lomhlaba, kuze kuthi uba umuntu engabala uthuli lomhlaba, izabalwa lenzalo yakho.
Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
17 Sukuma uhambe udabule ilizwe, ebudeni balo lebubanzini balo, ngoba ngizalinika wena.
Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
18 UAbrama wasesusa amathente wafika wahlala ezihlahleni zama-okhi zeMamre, eziseHebroni, wakhela lapho iNkosi ilathi.
Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

< UGenesisi 13 >