< UGenesisi 11 >

1 Umhlaba wonke-ke wawulolimi lunye, lamazwi manye.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 Kwasekusithi ekuhambeni kwabo bevela empumalanga bafica igceke elizweni leShinari, basebehlala khona.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 Basebesithi ngulowo lalowo kumakhelwane wakhe: Wozani, asenzeni izitina sizitshise lokuzitshisa; lesitina saba lilitshe kubo, lengcino yaba ludaka kubo.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 Basebesithi: Wozani, asizakheleni umuzi lomphotshongo osihloko sawo sisemazulwini, besesizenzela ibizo, hlezi sihlakazeke ebusweni bomhlaba wonke.
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 INkosi yasisehla ukubona umuzi lomphotshongo abantwana babantu abawakhayo.
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 INkosi yasisithi: Khangela, yisizwe sinye, njalo balolimi lunye bonke, njalo yikho abaqala ukukwenza; khathesi-ke akulalutho olungabehlula abamisa ukulwenza.
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 Wozani, asehle, siphambanise lapho ulimi lwabo, ukuze bangezwa, ngulowo lalowo ulimi lomakhelwane wakhe.
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 Ngakho iNkosi yabahlakazela ebusweni bomhlaba wonke besuka lapho; basebesima ukwakha umuzi.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 Ngalokho kwabizwa ibizo lawo ngokuthi iBabeli, ngoba lapho iNkosi yaphambanisa ulimi lomhlaba wonke; kusukela lapho iNkosi yabahlakaza ebusweni bomhlaba wonke.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 Lezi yizizukulwana zikaShemu. UShemu wayeleminyaka elikhulu, wasezala uArpakishadi, iminyaka emibili emva kukazamcolo.
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 UShemu wasephila, esezele uArpakishadi, iminyaka engamakhulu amahlanu; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 UArpakishadi wasephila iminyaka engamatshumi amathathu lanhlanu, wazala uShela.
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 UArpakishadi wasephila, esezele uShela, iminyaka engamakhulu amane lantathu; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 UShela wasephila iminyaka engamatshumi amathathu, wazala uEberi.
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 UShela wasephila, esezele uEberi, iminyaka engamakhulu amane lantathu; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 UEberi wasephila iminyaka engamatshumi amathathu lane, wazala uPelegi.
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 UEberi wasephila, esezele uPelegi, iminyaka engamakhulu amane lamatshumi amathathu; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 UPelegi wasephila iminyaka engamatshumi amathathu, wazala uRewu.
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 UPelegi wasephila, esezele uRewu, iminyaka engamakhulu amabili layisificamunwemunye; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 URewu wasephila iminyaka engamatshumi amathathu lambili, wazala uSerugi.
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 URewu wasephila, esezele uSerugi, iminyaka engamakhulu amabili lesikhombisa; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 USerugi wasephila iminyaka engamatshumi amathathu, wazala uNahori.
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 USerugi wasephila, esezele uNahori, iminyaka engamakhulu amabili; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 UNahori wasephila iminyaka engamatshumi amabili lesificamunwemunye, wazala uTera.
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 UNahori wasephila, esezele uTera, iminyaka elikhulu lamatshumi ayisificamunwemunye; wazala amadodana lamadodakazi.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 UTera wasephila iminyaka engamatshumi ayisikhombisa, wazala uAbrama, uNahori loHarani.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Lalezi yizizukulwana zikaTera. UTera wazala uAbrama, uNahori loHarani; uHarani wasezala uLothi.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 UHarani wasesifa phambi kukayise uTera, elizweni lokuzalwa kwakhe, eUri yamaKhaladiya.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 OAbrama loNahori basebezithathela abafazi; ibizo lomkaAbrama nguSarayi, lebizo lomkaNahori nguMilka, indodakazi kaHarani, uyise kaMilka loyise kaIska.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 Kodwa uSarayi wayeyinyumba; wayengelamntwana.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 UTera wasethatha uAbrama indodana yakhe, loLothi indodana kaHarani, indodana yendodana yakhe, loSarayi umalokazana wakhe, umkaAbrama indodana yakhe; basebesuka labo eUri yamaKhaladiya, ukuya elizweni leKhanani; basebefika eHarani, bahlala khona.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 Lensuku zikaTera zaziyiminyaka engamakhulu amabili lanhlanu; uTera wasefela eHarani.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

< UGenesisi 11 >