< U-Ezra 4 >
1 Kwathi izitha zakoJuda loBhenjamini sezizwile ukuthi abantwana bokuthunjwa babesakhela iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli ithempeli,
Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 basebesondela kuZerubhabheli lenhlokweni zaboyise bathi kibo: Kasakhe lani, ngoba siyamdinga uNkulunkulu wenu njengani, samhlabela kusukela ensukwini zikaEsarihadoni inkosi yeAsiriya owasenyusela lapha.
Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
3 Kodwa uZerubhabheli loJeshuwa lezinye inhloko zaboyise zakoIsrayeli bathi kibo: Kayisikho kwenu lathi ukwakhela uNkulunkulu wethu indlu, kodwa yithi sodwa esizakwakhela iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli njengokusilaya kwenkosi uKoresi inkosi yePerisiya.
Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
4 Kwasekusithi abantu balelolizwe badondisa izandla zabantu bakoJuda, babesabisa ekwakheni.
Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
5 Basebebaqhatshela abeluleki ukufubisa icebo labo zonke izinsuku zikaKoresi inkosi yePerisiya, kwaze kwaba sekubuseni kukaDariyusi inkosi yePerisiya.
Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
6 Ekubuseni-ke kukaAhasuwerusi, ekuqaleni kokubusa kwakhe, babhala isimangalelo bemelene labahlali bakoJuda leJerusalema.
Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
7 Njalo ensukwini zikaAthakisekisi oBishilamu, uMithiredathi, uTabeyeli labanye abakibo babhalela uAthakisekisi inkosi yePerisiya; lombhalo wencwadi wawubhalwe ngesiSiriya, uhunyutshwe ngesiSiriya.
Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
8 URehuma umlawuli loShimishayi umbhali babhala incwadi bemelene leJerusalema kuAthakisekisi inkosi, ngalindlela:
Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
9 Khonokho uRehuma umlawuli loShimishayi umbhali labanye babangane babo, amaDinayi, amaAfarisathiki, amaTharipheli, amaAfarisi, amaArikhevi, amaBhabhiloni, amaShushaniki, amaDehavi, amaElamu,
Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
10 lezinye izizwe uAsinaphari omkhulu lodumileyo azithumbayo wazihlalisa emzini ongoweSamariya, lezinye phetsheya komfula, lakhathesi.
ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
11 Le yikhophi yencwadi abayithumeza kuye, kuAthakisekisi inkosi: Izinceku, amadoda anganeno komfula, langesikhathi esinje.
Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
12 Kakwaziwe enkosini ukuthi amaJuda enyuka evela kuwe esiza kithi asefikile eJerusalema, ayawakha lowomuzi ovukelayo lomubi, aseqedisa imiduli, avuselela izisekelo.
Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
13 Khathesi kakwaziwe enkosini ukuthi uba lumuzi usakhiwa lemiduli iphele, kabayikupha umthelo, imali eyimfanelo, lemali yendlela, futhi uzalimaza isikhwama samakhosi.
Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
14 Khathesi njengoba sisidla itswayi etswayini lesigodlo njalo kakusifanelanga ukuthi sibone ihlazo lenkosi, ngakho sithumele sayazisa inkosi;
Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
15 ukuze kuhlolwe egwalweni lwezindaba zaboyihlo. Ngakho uzathola egwalweni lwezindaba, wazi ukuthi lumuzi ungumuzi ovukelayo, olimazayo emakhosini lemazweni, benza ukuhlamuka phakathi kwawo kwasezinsukwini zekadeni. Ngakho lumuzi wachithwa.
Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
16 Siyayazisa inkosi ukuthi uba lumuzi usakhiwa, lemiduli yawo iphele, ngalokho kawuyikuba lesabelo nganeno komfula.
Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
17 Inkosi yathuma impendulo kuRehuma umlawuli loShimishayi umbhali labanye babangane babo abahlala eSamariya labanye abaphetsheya komfula: Ukuthula, langesikhathi esinje.
Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
18 Incwadi elayithumela kithi ifundiwe ngokucacileyo phambi kwami.
Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
19 Umlayo wasubekwa yimi, basebedinga bathola ukuthi kusukela ensukwini zendulo lumuzi uziphakamisele amakhosi, lomvukela lokuhlamuka kwenziwe phakathi kwawo.
Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
20 Kwake kwaba khona amakhosi alamandla phezu kweJerusalema ayebusa phezu kwakho konke ngaphetsheya komfula; lomthelo, imali eyimfanelo, lemali yendlela kwaphiwa wona.
Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
21 Khathesi bekani umthetho ukwenza ukuthi lababantu bayekele ukuze lumuzi ungakhiwa kuze kwenziwe umthetho yimi.
Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
22 Njalo qaphelani ukuthi lingayekethisi ekwenzeni lokhu. Kungani ukonakala kuzakhula kukho ukulinyazwa kwamakhosi?
Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
23 Khonokho, kusukela ikhophi yencwadi kaAthakisekisi inkosi isifundiwe phambi kwaboRehuma loShimishayi umbhali labangane babo, baya masinyane eJerusalema kumaJuda, babenza bayekela ngengalo lamandla.
Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
24 Khonokho wema umsebenzi wendlu kaNkulunkulu eseJerusalema; wasusima kwaze kwaba ngumnyaka wesibili wokubusa kukaDariyusi inkosi yePerisiya.
Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.