< U-Ezra 1 >
1 Kwathi ngomnyaka wokuqala kaKoresi inkosi yePerisiya, ekugcwalisekeni kwelizwi leNkosi ngomlomo kaJeremiya, iNkosi yavusa umoya kaKoresi inkosi yePerisiya ukuthi edlulise isimemezelo embusweni wakhe wonke, njalo langombhalo, esithi:
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 Utsho njalo uKoresi inkosi yePerisiya: INkosi, uNkulunkulu wamazulu, inginikile yonke imibuso yomhlaba; layo ingilayile ukuyakhela indlu eJerusalema ekoJuda.
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 Ngubani ophakathi kwenu kubo bonke abantu bayo? UNkulunkulu wakhe kabe laye, enyukele eJerusalema ekoJuda, akhe indlu yeNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli (unguNkulunkulu) oseJerusalema.
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 Laloba ngubani oseleyo lakuyiphi yezindawo lapho ahlala njengowezizwe khona, kakuthi abantu bendawo yakibo bamsekele ngesiliva, langegolide, langempahla, langezifuyo, kanye lomnikelo wesihle wendlu kaNkulunkulu eseJerusalema.
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 Kwasekusukuma inhloko zaboyise bakoJuda loBhenjamini, labapristi lamaLevi, laye wonke uNkulunkulu ayevuse umoya wakhe, ukuthi benyukele ukwakha indlu yeNkosi eseJerusalema.
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 Labo bonke ababebaphahlile baqinisa izandla zabo ngezitsha zesiliva, ngegolide, ngempahla, langezifuyo, langezinto eziligugu, ngaphandle kwakho konke okwakunikelwe ngesihle.
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 UKoresi inkosi laye wakhupha izitsha zendlu yeNkosi, uNebhukadinezari ayezikhuphe eJerusalema wazifaka endlini yabonkulunkulu bakhe.
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 UKoresi inkosi yePerisiya wasezikhupha ngesandla sikaMithiredathi umphathisikhwama owazibalela uSheshibazari isiphathamandla sakoJuda.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 Leli-ke linani lazo: Imiganu yegolide engamatshumi amathathu, imiganu yesiliva eyinkulungwane, izingqamu ezingamatshumi amabili lesificamunwemunye,
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 inkezo zegolide ezingamatshumi amathathu, ezinye inkezo zesiliva ezingamakhulu amane letshumi, ezinye izitsha eziyinkulungwane.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 Zonke izitsha zegolide lezesiliva zazizinkulungwane ezinhlanu lamakhulu amane. Zonke lezi uSheshibazari wazenyusa lalabo ababenyuswe ekuthunjweni bevela eBhabhiloni besiya eJerusalema.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.