< UHezekheli 9 >

1 Wasememeza ezindlebeni zami ngelizwi elikhulu esithi: Yenza ababonisi bomuzi basondele, ngitsho wonke umuntu elesikhali sakhe sokuchitha esandleni sakhe.
Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
2 Khangela-ke, amadoda ayisithupha eza evela ngendlela yesango eliphezulu elikhangele ngasenyakatho; njalo wonke umuntu elesikhali sakhe sokuphahlaza esandleni sakhe; njalo umuntu oyedwa phakathi kwawo wayegqoke ilembu elicolekileyo, elophondo lweyinki lombhali ngasokhalweni lwakhe; asengena, ema duze kwelathi lethusi.
Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
3 Lenkazimulo kaNkulunkulu kaIsrayeli yenyuka isuka ngaphezu kwekherubhi eyayiphezu kwalo, yaya embundwini wendlu; wasememeza umuntu owayegqoke ilembu elicolekileyo owayelophondo lweyinki lombhali okhalweni lwakhe.
Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
4 INkosi yasisithi kuye: Dabula phakathi komuzi, phakathi kweJerusalema, ufake uphawu emabunzini abantu ababubulayo labakhalayo ngenxa yazo zonke izinengiso ezenziwa phakathi kwawo.
ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
5 Lakwabanye yathi endlebeni yami: Dabulani phakathi komuzi emva kwakhe, litshaye, ilihlo lenu lingahawukeli, njalo lingayekeli.
Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
6 Bulalani ngokuchitha abadala, abatsha, lezintombi, labantwana abancinyane, labesifazana; kodwa lingasondeli lakuwuphi umuntu okulophawu phezu kwakhe, liqalise endaweni yami engcwele. Basebeqalisa emadodeni amadala ayephambi kwendlu.
Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
7 Yasisithi kubo: Ngcolisani indlu, ligcwalise amaguma ngababuleweyo. Phumani. Basebephuma, babulala emzini.
Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
8 Kwasekusithi besababulala, mina-ke ngasala, ngathi mbo ngobuso bami, ngakhala ngathi: Hawu, Nkosi Jehova! Uzachitha yini yonke insali yakoIsrayeli ekuthululeni kwakho intukuthelo yakho phezu kweJerusalema?
Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
9 Khona yathi kimi: Ububi bendlu yakoIsrayeli loJuda bukhulu kakhulukazi, lelizwe ligcwele amacala egazi, lomuzi ugcwele ukuphambuka, ngoba bathi: INkosi ilidelile ilizwe, njalo iNkosi kayiboni.
Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
10 Lami-ke ilihlo lami kaliyikuhawukela, njalo kangiyikuyekela; ngizakwehlisela indlela yabo ekhanda labo.
Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
11 Khangela-ke, lowomuntu owayegqoke ilembu elicolekileyo, owayelophondo lweyinki okhalweni lwakhe, wabuyisela ilizwi esithi: Ngenzile njengoba ungilayile.
Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

< UHezekheli 9 >