< UHezekheli 7 >
1 Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 Wena-ke, ndodana yomuntu, itsho njalo iNkosi uJehova kulo ilizwe lakoIsrayeli: Isiphetho, isiphetho sesifikile phezu kwamagumbi womane elizwe.
“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti: “Chimaliziro! Chimaliziro chafika ku ngodya zinayi za dziko.
3 Khathesi isiphetho siphezu kwakho, njalo ngizathumela ukuthukuthela kwami phakathi kwakho, ngikwahlulele njengokwezenzo zakho, ngehlisele phezu kwakho wonke amanyala akho.
Chimaliziro chili pa iwe tsopano. Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe. Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4 Lelihlo lami kaliyikukuhawukela, kangiyikuyekela, kodwa ngizakwehlisela izindlela zakho phezu kwakho, lamanyala akho azakuba phakathi kwakho. Khona lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako. Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5 Itsho njalo iNkosi uJehova: Ububi, ububi obubodwa, khangela, sebufikile.
“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo! Taona chikubwera!
6 Isiphetho sesifikile, isiphetho sesifikile, siyakuvukela; khangela, sesifikile.
Chimaliziro chafika! Chimaliziro chafika! Chiwonongeko chakugwera. Taona chafika!
7 Ukusa sekufikile kuwe, wena mhlali welizwe; isikhathi sesifikile, usuku lwenkathazo luseduze, njalo kungeyisikho ukumemeza ngenjabulo kwezintaba.
Inu anthu okhala mʼdziko, chiwonongeko chakugwerani. Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8 Khathesi, kuseduze ukuthi ngithululele ulaka lwami phezu kwakho, ngiphelelise intukuthelo yami phakathi kwakho, ngikwahlulele njengokwezindlela zakho, ngehlisele phezu kwakho wonke amanyala akho.
Ine ndili pafupi kukukwiyirani, ndipo ukali wanga udzathera pa iwe; Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9 Lelihlo lami kaliyikuhawukela, njalo kangiyikuyekela; ngizanika njengokwezindlela zakho phezu kwakho, lamanyala akho azakuba phakathi kwakho. Khona lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi etshayayo.
Ine sindidzakumvera chisoni kapena kukuleka. Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
10 Khangela usuku, khangela, selufikile; ukusa sekuphumile; intonga ihlumile, ukuziqhenya kukhahlele.
“Taona, tsikulo! Taona, lafika! Chiwonongeko chako chabwera. Ndodo yaphuka mphundu za maluwa. Kudzitama kwaphuka.
11 Udlakela lusukume lwaba yintonga yobubi; kakuyikusala kubo, hatshi-ke exukwini labo, hatshi-ke okwabo, njalo kakuyikuba khona ukuqhinqa isililo phakathi kwabo.
Chiwawa chasanduka ndodo yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo. Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo. Palibiretu ndipo sipadzapezeka munthu wowalira maliro.
12 Isikhathi sesifikile, usuku selusondele; umthengi kangathokozi, lomthengisi angalili, ngoba ulaka luphezu kwexuku lonke lalo.
Nthawi yafika! Tsiku layandikira! Munthu wogula asakondwere ndipo wogulitsa asamve chisoni, popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 Ngoba umthengisi kayikubuyela kokuthengisiweyo, lanxa impilo yabo isesephakathi kwabaphilayo; ngoba umbono mayelana lexuku lonke lalo kawuyikuphenduka; futhi kakulamuntu ongaqinisa impilo yakhe ngesiphambeko sakhe.
Wogulitsa sadzazipezanso zinthu zimene anagulitsa kwa wina chinkana onse awiri akanali ndi moyo, pakuti chilango chidzagwera onsewo ndipo sichingasinthike. Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense amene adzapulumutsa moyo wake.
14 Baluvuthele uphondo ukuthi balungise konke, kodwa kakho oya empini, ngoba ulaka lwami luphezu kwexuku lalo lonke.
“Lipenga lalira, ndipo zonse zakonzeka. Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo, pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 Inkemba ingaphandle, lomatshayabhuqe wesifo lendlala kungaphakathi; osegangeni uzakufa ngenkemba, losemzini indlala lomatshayabhuqe wesifo kuzamqeda.
Ku bwalo kuli kumenyana ndipo mʼkati muli mliri ndi njala. Anthu okhala ku midzi adzafa ndi nkhondo. Iwo okhala ku mizinda adzafa ndi mliri ndi njala.
16 Kodwa abaphunyukayo babo bazaphunyuka, babe sezintabeni njengamajuba ezihotsha, bonke belila, ngulowo lalowo ngenxa yesiphambeko sakhe.
Onse amene adzapulumuka ndi kumakakhala ku mapiri, azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa. Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 Zonke izandla zizaphela amandla, lamadolo wonke ageleze njengamanzi.
Dzanja lililonse lidzalefuka, ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 Njalo bazabhinca amasaka, lovalo luzabembesa, lenhloni zibe sebusweni bonke, lempabanga phezu kwamakhanda abo wonke.
Iwo adzavala ziguduli ndipo adzagwidwa ndi mantha. Adzakhala ndi nkhope zamanyazi ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19 Bazalahla isiliva sabo ezitaladeni, legolide labo libe yikungcola; isiliva sabo legolide labo kakuyikuba lakho ukubophula ngosuku lokuthukuthela kweNkosi; kabayikonelisa umphefumulo wabo, bangagcwalisi amathumbu abo; ngoba kuyisikhubekiso sesiphambeko sabo.
“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa. Siliva ndi golide wawo sizidzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala, kapena kukhala okhuta, pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 Lobuhle besiceciso sakhe wabumisa ebukhosini, kodwa benza kubo imifanekiso yokunengekayo kwabo lezinengiso zabo; ngenxa yalokho ngibumise bube yinto engcolileyo kubo.
Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina. Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa kukhala zowanyansa.
21 Njalo ngizakunikela esandleni sabezizwe kube yimpango, lakwabakhohlakeleyo bomhlaba kube yimpango, njalo bazakungcolisa.
Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe. Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda ndi kudziyipitsa.
22 Njalo ngizaphendula ubuso bami busuke kubo, bangcolise indawo yami yensitha; ngoba abaphangi bazangena kuyo, bayingcolise.
Ine ndidzawalekerera anthuwo ndipo adzayipitsa malo anga apamtima. Adzalowamo ngati mbala ndi kuyipitsamo.
23 Yenza iketane, ngoba ilizwe ligcwele amacala egazi, lomuzi ugcwele udlakela.
“Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Ngakho ngizaletha ababi bezizwe, abazakudla ilifa lezindlu zabo; ngikwenze kuphele ukuziqhenya kwabalamandla; lendawo zabo ezingcwele zizangcoliswa.
Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa kuti idzalande nyumba zawo. Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Ukwethuka kuyeza; bazadinga-ke ukuthula, kodwa kakuyikuba khona.
Nkhawa ikadzawafikira adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Incithakalo izakuza phezu kwencithakalo, lombiko ube phezu kombiko; khona bezadinga umbono kumprofethi, kodwa umlayo uzabhubha kumpristi, leseluleko kubadala.
Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake, ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake. Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri. Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo, ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 Inkosi izalila, lesiphathamandla sembathiswe incithakalo, lezandla zabantu belizwe zizathuthumela. Ngizakwenza kubo ngokwendlela yabo, ngibahlulele ngezahlulelo zabo; khona bezakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Mfumu idzalira, kalonga adzagwidwa ndi mantha. Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha. Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo, ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.