< UHezekheli 42 >

1 Wasengikhuphela egumeni elingaphandle, ngendlela ekhangele ngasenyakatho; wangiletha ekamelweni eliqondene lendawo eyehlukeneyo, njalo eliqondene lesakhiwo ngasenyakatho.
Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku bwalo lakunja chakumpoto ndipo anafika nane ku zipinda zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ina yakumpoto.
2 Phambi kobude bezingalo ezilikhulu kwakulomnyango wenyakatho; lobubanzi babuzingalo ezingamatshumi amahlanu.
Nyumba yakumpotoyi mulitali mwake munali mamita makumi asanu, mulifupi mwake munali mamita 25.
3 Maqondana lezingalo ezingamatshumi amabili ezazingezeguma langaphakathi, lamaqondana lendawo egandelweyo eyayingeyeguma elingaphandle, kwakulomkhandlo maqondana lomkhandlo, ngezitezi ezintathu.
Panali midadada iwiri, umodzi umayangʼanana ndi bwalo lamʼkati la mamita khumi, winawo umayangʼanana ndi bwalo lakunja. Midadada iwiriyi inali ya nyumba zitatu zosanjikana ndipo imayangʼanana.
4 Laphambi kwamakamelo kwakulendawo yokuhamba ezingalo ezilitshumi ngobubanzi ngaphakathi, indlela eyingalo eyodwa, leminyango yawo yayingasenyakatho.
Kumaso kwa zipindazo kunali njira yamʼkati, mulifupi mwake munali mamita asanu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu. Makomo ake analoza chakumpoto.
5 Amakamelo angaphezulu-ke ayemafitshane; ngoba imikhandlo yayinciphisa kuwo, kulakwaphansi lakulakwaphakathi kwesakhiwo.
Zipinda zammwamba zinali zazifupi mʼmimbamu kupambana zipinda zamʼmunsi ndi zipinda zapakati chifukwa njira zake zinatenga malo ambiri.
6 Ngoba ayelezitezi ezintathu, kodwa zazingelazinsika njengezinsika zamaguma; ngakho-ke isakhiwo sasinciphile kulakwaphansi lakulakwaphakathi kusukela emhlabathini.
Popeza zipinda zinali zosanjikizana katatu ndipo zinalibe nsanamira monga za mabwalo, motero zipinda zamʼmwamba zinali zochepa kuyerekeza ndi zipinda zapansi ndi zipinda zapakati.
7 Lomduli owawungaphandle maqondana lamakamelo, indlela yeguma elingaphandle ngaphambi kwamakamelo, ubude bawo babuzingalo ezingamatshumi amahlanu.
Panali khoma lakunja lomwe limatsatana ndi zipindazo kutsogolo kwake pambali pabwalo lakunja, kutalika kwake kunali mamita 25.
8 Ngoba ubude bamakamelo ayesegumeni elingaphandle babuzingalo ezingamatshumi amahlanu; khangela-ke, ngaphambi kwethempeli kwakuzingalo ezilikhulu.
Zipinda za mʼmbali mwa bwalo lakunja mulitali mwake munali mamita 25. Koma zomwe zinali mʼmbali mwa Nyumba ya Mulungu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu.
9 Langaphansi kwalamakamelo kwakulokungena ngasempumalanga, lapho umuntu engena kuwo evela egumeni elingaphandle.
Pansi pa zipinda zimenezi panali khomo chakummawa kuchokera ku bwalo lakunja kumene khoma lake linkayambira.
10 Amakamelo ayesebubanzini bomduli weguma, indlela yempumalanga, ngaphambi kwendawo eyehlukanisiweyo, langaphambi kwesakhiwo.
Mbali yakummwera kuyangʼanana ndi bwalo ndi nyumbayo kunali zipinda zina.
11 Lendlela phambi kwawo yayinjengesimo samakamelo ayesendleleni yenyakatho, njengobude bawo, ngokunjalo njengobubanzi bawo. Lakho konke ukuphuma kwawo kwakunjengokwemikhuba yawo lanjengokweminyango yawo.
Kumaso kwa zipindazi kunali njira. Zipindazi mulitali mwake, mulifupi mwake ndiponso maonekedwe ake onse zinali zofanana ndi zipinda zoyangʼana zakumpoto zija. Makomo ndi zitseko zake zinalinso zofanana
12 Lanjengokweminyango yamakamelo ayesendleleni yeningizimu kwakulomnyango esihlokweni sendlela, indlela phambi komduli oqondileyo, lapho umuntu engena indlela yempumalanga.
ndi makomo a zipinda zakummwera. Kunali khomo mʼmbali ya kummawa kumene ankalowerako. Kunalinso khoma logawa zipinda.
13 Wasesithi kimi: Amakamelo enyakatho lamakamelo eningizimu, aphambi kwendawo eyehlukanisiweyo, angamakamelo angcwele, lapho abapristi abasondela eNkosini abazakudla khona izinto ezingcwelengcwele; babeke khona izinto ezingcwelengcwele, lomnikelo wokudla, lomnikelo wesono, lomnikelo wecala, ngoba indawo ingcwele.
Ndipo munthuyo anandiwuza kuti, “Zipinda zakumpoto ndi zakummwera zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi zoyera. Mʼmenemo ansembe amene amakhala pafupi ndi Yehova amadyeramo zopereka zopatulika kwambiri. Mʼmenemo adzayikamo zopereka zopatulika kwambiri, zopereka za chakudya, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula, poti malowo ndi opatulika.
14 Lapho abapristi bengena, kabayikuphuma endaweni engcwele baye egumeni elingaphandle, kodwa bazabeka lapho izembatho zabo abakhonza ngazo, ngoba zingcwele; bagqoke ezinye izembatho, basondele kukho okungokwabantu.
Pamene ansembe alowa ku malo opatulikawa, asatuluke kupita ku bwalo lakunja popanda kusiya momwemo zovala zimene anavala potumikira zija, pakuti zovalazi ndi zopatulika. Avale kaye zovala zina ndipo akhoza kufika kwa anthu.”
15 Eseqedile izilinganiso zendlu engaphakathi, wangikhupha ngendlela yesango elikhangele indlela yempumalanga, wayilinganisa inhlangothi zonke ezizingelezeleyo.
Munthuyo atamaliza kuyeza zimene zinali mʼkati mwa Nyumba ya Mulungu, anatuluka nane pa chipata chakummawa ndi kuyeza bwalo lonse.
16 Walinganisa uhlangothi lwempumalanga ngomhlanga wokulinganisa, imihlanga engamakhulu amahlanu, ngomhlanga wokulinganisa inhlangothi zonke.
Anayeza mbali yakummawa ndi ndodo yake yoyezera; kutalika kwake kunali mamita 250.
17 Walinganisa uhlangothi lwenyakatho, imihlanga engamakhulu amahlanu, ngomhlanga wokulinganisa inhlangothi zonke.
Anayeza mbali ya kumpoto ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250.
18 Walinganisa uhlangothi olungeningizimu, imihlanga engamakhulu amahlanu, ngomhlanga wokulinganisa.
Munthuyo anayeza mbali yakummwera; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake.
19 Wasephendukela kuhlangothi lwentshonalanga, walinganisa imihlanga engamakhulu amahlanu ngomhlanga wokulinganisa.
Kenaka anatembenukira ku mbali ya kumadzulo ndi kuyeza ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake.
20 Wayilinganisa ezinhlangothini zozine. Yayilomduli inhlangothi zonke uzingelezele, ubude bangamakhulu amahlanu, lobubanzi bungamakhulu amahlanu, ukwehlukanisa phakathi kokungcwele lokungangcwele.
Motero anayeza mbali zonse zinayi. Panali khoma lozungulira bwalolo mulitali mwake munali mamita 250 ndipo mulifupi mwake munalinso mamita 250. Khomalo linali lolekanitsa zinthu zoyera ndi zinthu wamba.

< UHezekheli 42 >