< UHezekheli 37 >
1 Isandla seNkosi sasiphezu kwami, sangikhupha ngoMoya weNkosi, sangibeka phakathi kwesihotsha esasigcwele amathambo.
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 Yangidlulisa kuwo ngibhoda inhlangothi zonke; khangela-ke, ayemanengi kakhulu ebusweni besihotsha, njalo khangela, ayomile kakhulu.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 Yasisithi kimi: Ndodana yomuntu, amathambo la angaphila yini? Ngasengisithi: Nkosi Jehova, nguwe owaziyo.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 Yasisithi kimi: Profetha phezu kwalamathambo, uthi kiwo: Lina mathambo omileyo, zwanini ilizwi leNkosi.
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Itsho njalo iNkosi uJehova kula amathambo: Khangelani, ngizakwenza umoya ungene kini, liphile.
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 Ngibeke imisipha phezu kwenu, ngivuselele inyama phezu kwenu, ngilembese ngesikhumba, ngifake umoya kini, liphile. Khona lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 Ngasengiprofetha njengokulaywa kwami; kwasekusiba lomsindo ngisaprofetha, khangela-ke ukunyikinyeka, amathambo asesondelelana, ithambo kuthambo lalo.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 Ngasengibona, khangela-ke, kwakulemisipha phezu kwawo, yavela inyama, lesikhumba sawasibekela ngaphezulu; kodwa kwakungelamoya kiwo.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 Yasisithi kimi: Profetha emoyeni, profetha ndodana yomuntu, uthi emoyeni: Itsho njalo iNkosi uJehova: Woza uvela emimoyeni emine, wena moya, uphefumulele kulaba ababuleweyo ukuze baphile.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 Ngasengiprofetha njengalokho yayingilayile; umoya wasungena kiwo, aphila, ema ngenyawo zawo, ibutho elikhulu kakhulukazi.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 Yasisithi kimi: Ndodana yomuntu, la amathambo ayindlu yonke kaIsrayeli. Khangela, bathi: Amathambo ethu omile, lethemba lethu libhubhile, siqunyiwe ngokwethu.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Ngakho profetha uthi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Khangelani, ngizavula amangcwaba enu, ngilikhuphule emangcwabeni enu, lina bantu bami, ngilise elizweni lakoIsrayeli.
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 Khona lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi, lapho ngivula amangcwaba enu, ngilikhuphule emangcwabeni enu, lina bantu bami.
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 Besengifaka umoya wami kini, liphile, besengilibeka elizweni lenu; khona lizakwazi ukuthi mina Nkosi ngikhulumile, ngakwenza, itsho iNkosi.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 Ilizwi leNkosi lafika kimi futhi lisithi:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Wena-ke ndodana yomuntu, zithathele intonga eyodwa, ubhale phezu kwayo uthi: EkaJuda, leyabantwana bakaIsrayeli abangane bakhe; ubusuthatha enye intonga, ubhale phezu kwayo uthi: EkaJosefa, intonga kaEfrayimi, layo yonke indlu kaIsrayeli abangane bakhe.
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 Ubusuzisondeza, enye kwenye kuwe, zibe yintonga eyodwa; njalo zizakuba ngeyodwa esandleni sakho.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 Lalapho abantwana babantu bakini bekhuluma kuwe besithi: Kawuyikusitshela yini ukuthi lezi ziyini kuwe?
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 Tshono kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, ngizathatha intonga kaJosefa, esesandleni sikaEfrayimi, lezizwe zakoIsrayeli abangane bakhe, ngizibeke kuyo, kuyo intonga kaJuda, ngizenze zibe yintonga eyodwa, zibe ngeyodwa esandleni sami.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 Njalo izintonga obhale kizo zizakuba sesandleni sakho phambi kwamehlo abo.
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 Ubususithi kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Khangelani, ngizathatha abantwana bakoIsrayeli phakathi kwezizwe, abaye kizo, ngibabuthe inhlangothi zonke, ngibalethe elizweni labo;
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 ngibenze babe yisizwe esisodwa elizweni phezu kwezintaba zakoIsrayeli; njalo inkosi eyodwa izakuba yinkosi yabo bonke; njalo kabasayikuba yizizwe ezimbili, kabasayikwehlukaniswa babe yimibuso emibili futhi.
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Kabasayikuzingcolisa ngezithombe zabo, langamanyala abo, langasiphi seziphambeko zabo; kodwa ngizabasindisa baphume kuzo zonke indawo zabo zokuhlala, abona kizo, ngibahlambulule. Ngalokho bazakuba ngabantu bami, lami ngibe nguNkulunkulu wabo.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 Njalo inceku yami uDavida izakuba yinkosi phezu kwabo; labo bonke bazakuba lomalusi munye; futhi bazahamba kuzahlulelo zami, bagcine izimiso zami, bazenze.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 Bahlale elizweni engalinika inceku yami uJakobe, ababehlala kulo oyihlo, yebo, bazahlala kulo, bona, labantwana babo, labantwana babantwana babo, kuze kube phakade. Futhi uDavida inceku yami uzakuba yisiphathamandla sabo kuze kube phakade.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 Futhi ngizakwenza isivumelwano sokuthula labo; sizakuba yisivumelwano esilaphakade labo; ngibamise, ngibandise, ngibeke indawo yami engcwele phakathi kwabo kuze kube phakade.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 Ithabhanekele lami lalo lizakuba kubo, njalo ngizakuba nguNkulunkulu wabo, labo bazakuba ngabantu bami.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 Lezizwe zizakwazi ukuthi mina Nkosi ngenza uIsrayeli abe ngcwele, nxa indawo yami engcwele izakuba phakathi kwabo kuze kube phakade.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”