< UHezekheli 35 >
1 Ilizwi leNkosi lafika kimi futhi lisithi:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Ndodana yomuntu, misa ubuso bakho bumelene lentaba iSeyiri, uprofethe umelene layo,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 uthi kuyo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, ngimelane lawe, wena ntaba yeSeyiri, njalo ngizakwelula isandla sami simelene lawe, ngikwenze ube lunxiwa lencithakalo.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Ngizakwenza imizi yakho ibe lunxiwa, wena-ke ube yincithakalo; njalo uzakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Ngoba waba lenzondo engapheliyo, wathululela abantwana bakoIsrayeli emandleni enkemba ngesikhathi sokuhlupheka kwabo, ngesikhathi sesiphambeko sokuphela;
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 ngakho, kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, isibili ngizakulungiselela igazi, legazi lizakuzingela; ngoba ungalizondanga igazi, igazi lizakuzingela.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Njalo ngizakwenza intaba yeSeyiri ibe yincithakalo lonxiwa, ngiqume kiyo odlulayo lophendukayo.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 Ngigcwalise intaba zayo ngababuleweyo bayo; amaqaqa akho, lezihotsha zakho, layo yonke imifula yakho, ababuleweyo ngenkemba bazakuwa kukho.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Ngizakwenza ube ngamanxiwa aphakade, lemizi yakho kayiyikuhlalwa; khona uzakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Ngoba uthi: Lezizizwe ezimbili lala amazwe amabili kuzakuba ngokwami, sidle ilifa lakho; lanxa iNkosi ibikhona lapho;
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 ngakho, kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, lami ngizakwenza ngokolaka lwakho lanjengokomhawu wakho owakusebenzisayo ngenzondo yakho umelene labo; ngizenze ngaziwe phakathi kwabo, lapho sengikwahlulele.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Khona uzakwazi ukuthi mina Nkosi ngizwile zonke izithuko zakho owazikhuluma umelene lezintaba zakoIsrayeli usithi: Zichithekile, sizinikiwe zibe yikudla.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Ngokunjalo lizikhulisile limelene lami ngomlomo wenu, landisa amazwi enu limelene lami; mina ngizwile.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Itsho njalo iNkosi uJehova: Njengokwentokozo yelizwe lonke, ngizakwenza ube yincithakalo.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 Njengoba lathokoza ngelifa lendlu kaIsrayeli ngenxa yokuthi lichitheka, ngokunjalo ngizakwenza kuwe; uzakuba yincithakalo, wena ntaba yeSeyiri, leEdoma yonke, yona yonke. Khona bazakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”