< UHezekheli 22 >

1 Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Wena-ke, ndodana yomuntu, uzakwehlulela yini, wahlulele umuzi wegazi? Yebo uzawazisa zonke izinengiso zawo.
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 Ubususithi: Itsho njalo iNkosi uJehova: Umuzi ochitha igazi phakathi kwawo, ukuze isikhathi sawo sifike, wenze izithombe ezimelene lawo, ukuze uzingcolise.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 Wena usulecala ngegazi olichithileyo, wazingcolisa ngezithombe zakho ozenzileyo, wasondeza insuku zakho, usufikile eminyakeni yakho. Ngalokho ngikwenzile waba lihlazo ezizweni lenhlekisa kuwo wonke amazwe.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 Abaseduze labakhatshana lawe bazakuhleka usulu, wena ongcolileyo ngebizo, ogcwele isiphithiphithi.
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Khangela, iziphathamandla zakoIsrayeli zaziphakathi kwakho, yileso laleso ngengalo yaso, ukuthi sichithe igazi.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 Baphathe uyihlo lonyoko ngokweyisa kuwe; benze ngocindezelo kowemzini phakathi kwakho; bacindezele izintandane lomfelokazi kuwe.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 Uzidelele izinto zami ezingcwele, wangcolisa amasabatha ami.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 Abantu abahlebayo babekuwe ukuze bachithe igazi; badla kuwe phezu kwezintaba; benza amanyala phakathi kwakho.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 Bembule ubunqunu baboyise phakathi kwakho; bathobise kuwe owesifazana ongcoliswe yikuba semfuleni.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 Futhi omunye wenze amanyala lomfazi kamakhelwane wakhe, lomunye wangcolisa umalokazana wakhe ngokuhlazisayo, lomunye uthobise udadewabo phakathi kwakho, indodakazi kayise.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 Phakathi kwakho bemukele izipho ukuze bachithe igazi; uyemukela inzalo lokwengezelelweyo, uphangile umakhelwane wakho ngocindezelo, wangikhohlwa, itsho iNkosi uJehova.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 Khangela-ke ngitshayile isandla sami ngenzuzo yakho embi oyenzileyo, langegazi lakho ebeliphakathi kwakho.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Inhliziyo yakho izakuma yini, kumbe izandla zakho ziqine, ensukwini engizaphathana lawe kizo? Mina Nkosi ngikhulumile, njalo ngizakwenza.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 Ngikuhlakaze phakathi kwezizwe, ngikusabalalise phakathi kwamazwe, ngiqede ukungcola kwakho kuwe.
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 Njalo uzangcoliswa phakathi kwakho emehlweni abezizwe; ubususazi ukuthi ngiyiNkosi.
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
Yehova anandiyankhula nati:
18 Ndodana yomuntu, indlu kaIsrayeli isibengamanyele kimi; bonke balithusi, lezenge, lensimbi, lomnuso, phakathi kwesithando; bangamanyele esiliva.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Ngoba lonke selibengamanyele, ngakho khangelani, ngizalibuthelela phakathi kweJerusalema.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 Njengoba bebuthelela isiliva lethusi lensimbi lomnuso lezenge phakathi kwesithando, ukuze bafuthe umlilo phezu kwakho ukukuncibilikisa; ngokunjalo ngizalibuthelela ekuthukutheleni kwami lelakeni lwami, ngilitshiye, ngilincibilikise.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 Yebo, ngizalibuthelela, ngivuthele phezu kwenu emlilweni wentukuthelo yami, beselincibilikiswa phakathi kwawo.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 Njengesiliva sincibilikiswa phakathi kwesithando, ngokunjalo lizancibilikiswa phakathi kwaso; njalo lizakwazi ukuthi mina Nkosi ngithulule ulaka lwami phezu kwenu.
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 Ndodana yomuntu, wothi kiyo: Wena uyilizwe elingahlanjululwanga, lelinganethwanga ngosuku lwentukuthelo.
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 Ugobe lwabaprofethi bayo phakathi kwayo lunjengesilwane esibhongayo esidlithiza impango; bayidlile imiphefumulo, bathatha inotho lezinto eziligugu, benza abafelokazi baba banengi phakathi kwayo.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Abapristi bayo baphathe umlayo wami ngodlakela, bangcolisa izinto zami ezingcwele; kabenzanga mehluko phakathi kokungcwele lokungcolileyo; kabazisanga umehluko phakathi kokungcolileyo lokuhlambulukileyo; bafihla amehlo abo kumasabatha ami; ngakho ngangcoliswa phakathi kwabo.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Iziphathamandla zayo phakathi kwayo zinjengezimpisi ezidlithiza impango, ukuthi zichithe igazi, zibhubhise imiphefumulo, ukuze zizuze inzuzo embi.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 Labaprofethi bayo babacombe ngekalaga, bebona okuyize, bebavumisa amanga, besithi: Itsho njalo iNkosi uJehova; kanti iNkosi ingakhulumanga.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 Abantu belizwe bacindezele ngocindezelo, baphanga impango, bacindezela umyanga loswelayo, bacindezela owezizwe kungelakulunga.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 Njalo ngadinga umuntu phakathi kwabo ongabiya uthango, ame esikhexeni phambi kwami emele ilizwe ukuze ngingalichithi, kodwa kangimtholanga.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 Ngakho ngithululele intukuthelo yami phezu kwabo, ngibaqede ngomlilo wolaka lwami; ngehlisele indlela yabo phezu kwekhanda labo, itsho iNkosi uJehova.
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

< UHezekheli 22 >