< UHezekheli 10 >

1 Ngasengibona, khangela-ke, emkhathini owawungaphezu kwekhanda lamakherubhi kwakulokunjengelitshe lesafire, kunjengokubonakala komfanekiso wesihlalo sobukhosi; kwabonakala phezu kwawo.
Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
2 Wasekhuluma emuntwini ogqoke ilembu elicolekileyo, wathi: Ngena ngaphakathi kwamavili, ngaphansi kwekherubhi, ugcwalise intende zezandla zakho ngamalahle omlilo avela phakathi kwamakherubhi, uwahlakaze phezu komuzi. Wasengena phambi kwamehlo ami.
Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
3 Njalo amakherubhi ayemi ngakwesokunene kwendlu, lapho lowomuntu engena; iyezi laseligcwalisa iguma elingaphakathi.
Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
4 Inkazimulo yeNkosi yasiphakama isuka phezu kwekherubhi, phezu kombundu wendlu; indlu yasigcwaliswa liyezi, leguma lagcwala ukukhanya kwenkazimulo yeNkosi.
Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
5 Lomdumo wempiko zamakherubhi wezwakala kwaze kwaba segumeni elingaphandle, njengelizwi likaNkulunkulu uSomandla nxa ekhuluma.
Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
6 Kwasekusithi isimlayile umuntu ogqoke ilembu elicolekileyo isithi: Thatha umlilo phakathi kwamavili, phakathi kwamakherubhi; wangena, wema duze kwevili.
Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
7 Ikherubhi laseliselulela isandla salo sisuka phakathi kwamakherubhi kuwo umlilo owawuphakathi kwamakherubhi, lawuthatha, lawubeka ezandleni zalowo owayembethe ilembu elicolekileyo; owawuthatha waphuma.
Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
8 Kwasekubonakala kiwo amakherubhi isimo sesandla somuntu ngaphansi kwempiko zawo.
Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
9 Ngasengibona, khangela-ke amavili amane eceleni kwamakherubhi, ivili elilodwa eceleni kwelinye ikherubhi, levili elilodwa eceleni kwelinye ikherubhi; lokubonakala kwamavili kwakunjengombala welitshe lebherule.
Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
10 Mayelana lokubonakala kwawo, womane ayelesimo sinye, njengokungathi livili eliphakathi kwevili.
Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
11 Ekuhambeni kwawo, ahamba ngenhlangothi zawo zozine, awaphendukanga ekuhambeni kwawo, kodwa indawo lapho ikhanda elalikhangele khona, ayilandela, awaphendukanga ekuhambeni kwawo.
Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
12 Lomzimba wawo wonke, lemihlane yawo, lezandla zawo, lempiko zawo, lamavili, kwakugcwele amehlo inhlangothi zonke, amavili azo zozine ezazilawo.
Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
13 Mayelana lamavili, kwamenyezwa kiwo endlebeni zami ukuthi: Vili!
Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
14 Njalo yilelo lalelo lalilobuso obune; ubuso bokuqala babuyibuso bekherubhi, lobuso besibili babuyibuso bomuntu, lobesithathu buyibuso besilwane, lobesine buyibuso belinqe.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
15 Amakherubhi aseziphakamisa. Lesi yisidalwa esiphilayo engasibona ngasemfuleni iKebari.
Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
16 Kwathi lapho amakherubhi ehamba, amavili ahamba eceleni kwawo; lalapho amakherubhi ephakamisa impiko zawo ukuze enyuke asuke emhlabeni, lawomavili kawaphendukanga esuka eceleni lawo futhi.
Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
17 Lapho esima, lawo ema; lalapho ephakama, lawo aphakama; ngoba umoya wezidalwa eziphilayo wawukiwo.
Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
18 Inkazimulo yeNkosi yasiphuma yasuka phezu kombundu wendlu, yema phezu kwamakherubhi.
Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
19 Amakherubhi asephakamisa impiko zawo, enyuka esuka emhlabeni phambi kwamehlo ami, lapho ephuma, lamavili lawo ayemaqondana lawo; njalo yilelo lalelo lema emnyango wesango elingasempumalanga kwendlu yeNkosi; lenkazimulo kaNkulunkulu kaIsrayeli yayiphezu kwawo ngaphezulu.
Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
20 Lesi yisidalwa esiphilayo engasibona ngaphansi kukaNkulunkulu kaIsrayeli ngasemfuleni iKebari; ngasengisazi ukuthi ngamakherubhi.
Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
21 Yilelo lalelo lalilobuso obune, lalelo lalelo lilempiko ezine; lesimo sezandla zomuntu singaphansi kwempiko zazo.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
22 Lesimo sobuso bawo sasiyibuso engabubona ngasemfuleni iKebari, ukubonakala kwawo, lawo ngokwawo. Ahamba, yilelo lalelo ngaphambi kobuso balo.
Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.

< UHezekheli 10 >