< UHezekheli 1 >
1 Kwasekusithi-ke ngomnyaka wamatshumi amathathu, ngenyanga yesine, ngolwesihlanu lwenyanga, lapho ngangiphakathi kwabathunjiweyo ngasemfuleni iKebari, avuleka amazulu, ngasengibona imibono kaNkulunkulu.
Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.
2 Ngolwesihlanu lwenyanga, okungumnyaka wesihlanu wokuthunjwa kwenkosi uJehoyakhini,
Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende,
3 ilizwi leNkosi leza liqonde kuHezekeli, indodana kaBuzi, umpristi, elizweni lamaKhaladiya ngasemfuleni iKebari; lesandla seNkosi saba phezu kwakhe lapho.
Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.
4 Ngasengibona, khangela-ke, umoya wesivunguzane wavela enyakatho, iyezi elikhulu, lomlilo ozimumetheyo, lokucwazimula inhlangothi zonke zalo, laphakathi kwalo kwavela kwangathi libala lethusi, livela phakathi komlilo.
Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira.
5 Laphakathi kwalo kwavela umfanekiso wezidalwa ezine eziphilayo. Lalokhu kwakuyisimo sazo: Zazilomfanekiso womuntu.
Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu
6 Njalo yileso laleso sasilobuso obune, njalo yileso laleso sazo sasilempiko ezine.
koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi.
7 Lenyawo zazo zazizinyawo eziqondileyo, lengaphansi yezinyawo zazo yayinjengengaphansi yonyawo lwethole, zacwazimula njengombala wethusi elilolongiweyo.
Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira.
8 Njalo kwakulezandla zomuntu ngaphansi kwempiko zazo enhlangothini zazo zozine. Njalo zozine zazilobuso bazo lempiko zazo.
Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko,
9 Impiko zazo zazihlangene olunye kolunye; aziphendukanga ekuhambeni kwazo; zahamba, yileso laleso siqonde phambili.
ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.
10 Njalo umfanekiso wobuso bazo wawuyibuso bomuntu, njalo zozine zazilobuso besilwane ngakwesokunene; njalo zozine zazilobuso benkabi ngakwesokhohlo; futhi zozine zazilobuso belinqe.
Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga.
11 Babunjalo ubuso bazo; lempiko zazo zazehlukene ngaphezulu; yileso laleso sasilezimbili zihlanganisiwe kolunye, lezimbili zigubuzele imizimba yazo.
Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake.
12 Zahamba yileso laleso siqonde phambili; zaya lapho umoya owaya khona, zingaphenduki ekuhambeni kwazo.
Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita.
13 Mayelana lomfanekiso wezidalwa eziphilayo, ukubonakala kwazo kwakunjengamalahle omlilo avuthayo, njengokubonakala kwezibane; kwahamba kusiya le lale phakathi kwezidalwa eziphilayo; njalo umlilo wawulokukhazimula, njalo emlilweni kwakuphuma umbane.
Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo.
14 Lezidalwa eziphilayo zagijima zaphenduka njengokubonakala kokuphazima kombane.
Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.
15 Ngathi ngikhangela izidalwa eziphilayo, khangela-ke, ivili elilodwa lalisemhlabeni eceleni kwezidalwa eziphilayo, ebusweni baso obune.
Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi.
16 Ukubonakala kwamavili lomsebenzi wawo kwakufanana lombala webherule; njalo zozine zazilesimo sinye; lokubonakala kwazo lomsebenzi wazo kwakunjengokuthi livili phakathi kwevili.
Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana.
17 Ekuhambeni kwawo ahamba ngezinhlangothi zawo zozine; kawaphendukanga ekuhambeni kwawo.
Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka.
18 Mayelana lamarimu awo, ayephakeme kangangokuthi ayesesabeka; njalo amarimu awo ayegcwele amehlo inhlangothi zonke zawo zozine.
Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.
19 Ekuhambeni kwezidalwa eziphilayo amavili ahamba eceleni kwazo; lekuphakanyisweni kwezidalwa eziphilayo emhlabeni lamavili aphakanyiswa.
Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso.
20 Lapho umoya owawusiya khona zaya khona, kulapho umoya owawuzakuya khona; lamavili aphakanyiswa eqondene lawo; ngoba umoya wezidalwa eziphilayo wawusemavilini.
Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija.
21 Lapho lezi zihamba, lawo ahamba; lalapho lezi zisima, lawo ema; lalapho lezi ziphakanyiswa emhlabeni, amavili aphakanyiswa eqondene lazo; ngoba umoya wezidalwa eziphilayo wawusemavilini.
Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.
22 Njalo isimo somkhathi ngaphezu kwamakhanda ezidalwa eziphilayo sasinjengombala wekristali elesabekayo, seluliwe phezu kwamakhanda azo ngaphezulu.
Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake.
23 Langaphansi komkhathi impiko zazo zaziqondile, olunye lusiya kolunye; yileso laleso silezimbili ezembese imizimba yazo ngapha, njalo yileso laleso silezimbili ezembese ngaphayana.
Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake.
24 Lekuhambeni kwazo ngezwa umsindo wempiko zazo unjengomsindo wamanzi amanengi, njengelizwi likaSomandla, umsindo wokuhlokoma, njengomsindo wenkamba; lapho zisima zehlisa impiko zazo.
Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.
25 Kwasekusiba lelizwi elavela phezu komkhathi ongaphezu kwekhanda lazo lapho sezimi sezehlise impiko zazo.
Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake.
26 Langaphezu komkhathi owawuphezu kwekhanda lazo kwakunjengesimo selitshe lesafire, umfanekiso wesihlalo sobukhosi; langaphezu komfanekiso wesihlalo sobukhosi kwakulomfanekiso onjengokubonakala komuntu phezu kwakho ngaphezulu.
Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu.
27 Ngasengibona njengombala wethusi, njengokubonakala komlilo phakathi kwakho inhlangothi zonke, kusukela ekubonakaleni kokhalo lwakhe langaphezulu, njalo kusukela ekubonakaleni kokhalo lwakhe langaphansi, ngabona kunjengokubonakala komlilo, lokukhazimula inhlangothi zakhe zonke.
Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo.
28 Njengokubonakala komchilo wamakhosikazi osemayezini ngosuku lwezulu, kwakunjalo ukubonakala kokukhazimula inhlangothi zonke. Lokhu kwakuyikubonakala kwesimo senkazimulo yeNkosi. Ngathi ngikubona, ngathi mbo ngobuso, ngasengisizwa ilizwi lowakhulumayo.
Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.