< U-Eksodusi 7 >

1 INkosi yasisithi kuMozisi: Bona, ngikwenze waba njengoNkulunkulu kuFaro; loAroni umnewenu uzakuba ngumprofethi wakho.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
2 Wena uzakhuluma konke engikulaya khona; loAroni umnewenu uzakhuluma kuFaro ukuthi ayekele abantwana bakoIsrayeli baphume elizweni lakhe.
Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
3 Kodwa mina ngizakwenza inhliziyo kaFaro ibe lukhuni, ngandise izibonakaliso zami lezimangaliso zami elizweni leGibhithe.
Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
4 Kodwa uFaro kayikulilalela; njalo ngizabeka isandla sami phezu kweGibhithe, ngikhuphe amabutho ami, isizwe sami, abantwana bakoIsrayeli, elizweni leGibhithe, ngezigwebo ezinkulu.
iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
5 Njalo amaGibhithe azakwazi ukuthi ngiyiNkosi, lapho ngiselula isandla sami phezu kweGibhithe, ngikhuphe abantwana bakoIsrayeli phakathi kwawo.
Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
6 OMozisi loAroni basebesenza njengoba iNkosi yabalaya; benza njalo.
Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
7 UMozisi wayeseleminyaka engamatshumi ayisificaminwembili, loAroni wayeleminyaka engamatshumi ayisificaminwembili lantathu lapho bekhuluma kuFaro.
Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
8 INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni, isithi:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
9 Nxa uFaro ekhuluma lani esithi: Zenzeleni isimangaliso; uzakuthi kuAroni: Thatha intonga yakho, uyiphosele phansi phambi kukaFaro, izakuba yinyoka.
“Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
10 UMozisi loAroni basebengena kuFaro, benza njalo njengoba iNkosi ilayile; uAroni wasephosela phansi intonga yakhe phambi kukaFaro laphambi kwenceku zakhe, yasisiba yinyoka.
Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
11 UFaro wasebiza laye izazi labathakathi; labalumbi beGibhithe labo benza njalo ngamalumbo abo.
Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
12 Ngoba ngulowo lalowo waphosela phansi intonga yakhe, zaba zinyoka; kodwa intonga kaAroni yaginya intonga zabo.
Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
13 Kodwa inhliziyo kaFaro yaba lukhuni, okokuthi kabalalelanga, njengokutsho kweNkosi.
Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
14 INkosi yasisithi kuMozisi: Inhliziyo kaFaro inzima, uyala ukuyekela isizwe sihambe.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
15 Yana kuFaro ekuseni; khangela, uzaphuma esiya emanzini, ume uqondane laye ekhunjini lomfula, lentonga eyaphenduka yaba yinyoka ithathe esandleni sakho.
Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
16 Uzakuthi kuye: INkosi uNkulunkulu wamaHebheru ingithume kuwe isithi: Yekela isizwe sami sihambe, singikhonze enkangala; kodwa khangela, kawulalelanga kuze kube khathesi.
Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
17 Itsho njalo iNkosi: Ngalokhu uzakwazi ukuthi ngiyiNkosi; khangela, ngizatshaya ngentonga esesandleni sami phezu kwamanzi asemfuleni, njalo azaphenduka abe ligazi.
Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
18 Lenhlanzi ezisemfuleni zizakufa, lomfula ube levumba; lamaGibhithe azadinwa yikunatha amanzi emfuleni.
Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
19 INkosi yasisithi kuMozisi: Tshono kuAroni uthi: Thatha intonga yakho, welule isandla sakho phezu kwamanzi eGibhithe, phezu kwemifula yabo, phezu kwezifula zabo, laphezu kweziziba zabo, laphezu kwamachibi wonke amanzi abo, ukuze abe ligazi. Kuzakuba legazi elizweni lonke leGibhithe, lezitsheni zezihlahla lezamatshe.
Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
20 UMozisi loAroni basebesenza njalo, njengokulaya kweNkosi; wasephakamisa intonga, watshaya amanzi ayesemfuleni phambi kwamehlo kaFaro laphambi kwamehlo ezinceku zakhe; lawo wonke amanzi ayesemfuleni aphendulwa aba ligazi.
Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
21 Lenhlanzi ezisemfuleni zafa; lomfula waba levumba, kwaze kwathi amaGibhithe ehluleka ukuwanatha amanzi emfuleni; njalo kwakulegazi elizweni lonke leGibhithe.
Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
22 Labalumbi beGibhithe benza njalo ngamalumbo abo, kwaze kwathi inhliziyo kaFaro yaba lukhuni, njalo kabalalelanga, njengokutsho kweNkosi.
Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
23 UFaro wasetshibilika waya endlini yakhe njalo kayibekanga inhliziyo yakhe lakulokhu.
Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
24 LamaGibhithe wonke agebha amanzi okunatha inhlangothi zonke zomfula, ngoba babengelakunatha emanzini omfula.
Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
25 Lensuku eziyisikhombisa zagcwaliseka emva kokuthi iNkosi isitshaye umfula.
Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.

< U-Eksodusi 7 >