< U-Eksodusi 40 >
1 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
2 Ngosuku lwenyanga yokuqala, ngolokuqala lwenyanga, uzamisa ithabhanekele, ithente lenhlangano,
“Imika chihema, tenti ya msonkhano, tsiku loyamba la mwezi.
3 ubusufaka lapho umtshokotsho wobufakazi, umbomboze umtshokotsho ngeveyili.
Uyikemo bokosi la umboni ndipo uphimbe bokosilo ndi katani.
4 Ungenise itafula, uhlele okuhlelwayo phezu kwalo; ungenise uluthi lwesibane, ulumathise izibane zalo.
Ulowetsemo tebulo ndi kuyika zimene zimakhala pamenepo. Kenaka ulowetse choyikapo nyale ndipo uyikepo nyale zake.
5 Ubeke ilathi legolide lempepha phambi komtshokotsho wobufakazi, ulengise isilenge somnyango wethabhanekele.
Uyike guwa lofukiza la golide patsogolo pa bokosi la umboni ndipo uyike katani ya pa chipata cha chihema.
6 Ubeke ilathi lomnikelo wokutshiswa phambi komnyango wethabhanekele wethente lenhlangano,
“Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano.
7 ubeke inditshi yokugezela phakathi kwethente lenhlangano lelathi, uthele amanzi lapho.
Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi.
8 Umise iguma inhlangothi zonke, ulengise isilenge sesango leguma.
Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo.
9 Uthathe amafutha okugcoba, ugcobe ithabhanekele lakho konke okukulo, ulingcwelise lempahla yalo yonke, njalo lizakuba ngcwele.
“Utenge mafuta wodzozera ndipo udzoze chihema ndi chilichonse chili mʼmenemo ndipo zidzakhala zoyeretsedwa.
10 Njalo ugcobe ilathi lomnikelo wokutshiswa lezitsha zalo zonke, ulingcwelise ilathi, njalo ilathi lizakuba yingcwelengcwele.
Kenaka udzoze guwa lansembe lopsereza ndi ziwiya zake zonse. Ulipatule guwalo ndipo lidzakhala loyera kwambiri.
11 Njalo ugcobe inditshi yokugezela lonyawo lwayo, uyingcwelise.
Udzoze beseni ndi miyendo yake ndipo uzipatule.
12 Usondeze uAroni lamadodana akhe emnyango wethente lenhlangano, ubagezise ngamanzi.
“Ubwere ndi Aaroni ndi ana ake pa chipata cha tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi.
13 Ugqokise uAroni izembatho ezingcwele, umgcobe, umngcwelise, ukuze angisebenzele njengompristi.
Kenaka umuveke Aaroni zovala zopatulika, umudzoze ndi kumupatula kotero kuti athe kunditumikira monga wansembe.
14 Usondeze amadodana akhe, uwagqokise izigqoko,
Ubweretse ana ake ndipo uwaveke minjiro.
15 uwagcobe njengalokhu ugcobe uyise, ukuze angisebenzele njengabapristi; kuzakuthi-ke ukugcotshwa kwabo kuzakuba kubo yibupristi obuphakade kuzizukulwana zabo.
Uwadzoze monga momwe unadzozera abambo awo, kotero kuti anditumikire monga ansembe. Kudzozedwako kudzakhala unsembe wawo pa mibado ndi mibado”
16 UMozisi wenza njengakho konke iNkosi eyayimlaye khona; wenza njalo.
Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira.
17 Kwasekusithi ngenyanga yokuqala ngomnyaka wesibili ngolokuqala lwenyanga ithabhanekele lamiswa.
Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri.
18 UMozisi wasemisa ithabhanekele; wabeka phansi izisekelo zalo, wamisa amapulanka alo, wafaka imithando yalo, wamisa insika zalo.
Nthawi imene Mose anayimika chihema, anayika matsinde mʼmalo ake, kuyimitsa maferemu, kulowetsa mitanda ndi kuyika nsichi.
19 Wendlala ithente phezu kwethabhanekele, wabeka isifulelo sethente phezu kwalo phezulu, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
Kenaka anayika tenti pamwamba pa chihema ndipo anayika chophimba pa tenti monga momwe Yehova analamulira Mose.
20 Wathatha wafaka ubufakazi emtshokotshweni, wafaka imijabo emtshokotshweni, wafaka isihlalo somusa ngaphezu komtshokotsho phezulu.
Iye anatenga miyala ya umboni nayika mʼbokosi lija ndi kuyika chivundikiro pamwamba pake.
21 Wangenisa umtshokotsho ethabhanekeleni, wamisa iveyili lesembeso wambomboza umtshokotsho wobufakazi, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
Kenaka analowetsa bokosilo mʼchihema ndipo anapachika katani ndi kubisa bokosi la umboni monga momwe Yehova analamulira iye.
22 Wasefaka itafula ethenteni lenhlangano, eceleni kwethabhanekele ngenyakatho ngaphandle kweveyili,
Mose anayika tebulo mu tenti ya msonkhano kumpoto kwa chihema, kunja kwa katani,
23 wahlela isinkwa ngohlelo phezu kwalo phambi kweNkosi, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose.
24 Wafaka uluthi lwesibane ethenteni lenhlangano, maqondana letafula, eceleni kwethabhanekele ngeningizimu.
Iye anayikanso choyikapo nyale mu tenti ya msonkhano moyangʼanana ndi tebulo mbali yakummwera kwa chihema.
25 Walumathisa izibane phambi kweNkosi, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
Ndipo anayikapo nyale zija pamaso pa Yehova, monga Yehova analamulira Mose.
26 Wafaka ilathi legolide ethenteni lenhlangano phambi kweveyili,
Mose anayika guwa la golide mu tenti ya msonkhano patsogolo pa katani
27 watshisa kulo impepha elephunga elimnandi, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
ndipo anapserezapo lubani wonunkhira monga Yehova anamulamulira.
28 Walengisa isilenge somnyango wethabhanekele.
Kenaka anayika katani ya pa chipata cha chihema.
29 Wabeka ilathi lomnikelo wokutshiswa emnyango wethabhanekele lethente lenhlangano, wanikela kulo umnikelo wokutshiswa lomnikelo wokudla, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
Iye anayika guwa lansembe yopsereza pafupi ndi chipata cha chihema, tenti ya msonkhano, ndipo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya ufa monga Yehova anamulamulira.
30 Wabeka inditshi yokugezela phakathi kwethente lenhlangano lelathi, wathela lapho amanzi okugeza.
Iye anayika beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo anathiramo madzi wosamba,
31 UMozisi loAroni lamadodana akhe bagezela kuyo izandla zabo lenyawo zabo;
ndipo Mose, Aaroni ndi ana ake amasamba manja ndi mapazi awo.
32 ekungeneni kwabo ethenteni lenhlangano lekusondeleni kwabo elathini bageza, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
Iwo amasamba nthawi zonse akamalowa mu tenti ya msonkhano kapena kuyandikira guwa lansembe monga Yehova analamulira Mose.
33 Wasemisa iguma lazingelezela ithabhanekele lelathi, walengisa isilenge sesango leguma. UMozisi wasewuqeda umsebenzi.
Kenaka Mose anamanga bwalo kuzungulira chihema ndi guwa lansembe ndipo anayika katani ya pa chipata cha bwalo. Kotero Mose anamaliza ntchito.
34 Iyezi laselisibekela ithente lenhlangano, lenkazimulo yeNkosi yagcwalisa ithabhanekele.
Kenaka mtambo unaphimba tenti ya msonkhano, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho.
35 Ngakho uMozisi wayengelakungena ethenteni lenhlangano, ngoba iyezi lahlala phezu kwalo lenkazimulo yeNkosi yagcwalisa ithabhanekele.
Mose sanathe kulowa mu tenti ya msonkhano chifukwa mtambo unali utakhazikika pa chihemacho, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho.
36 Lalapho iyezi lisenyuswa lisuka ethabhanekeleni, abantwana bakoIsrayeli baqhubekela phambili enhambeni zabo zonke,
Pa maulendo awo onse, mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso pamene analipo.
37 kodwa lapho iyezi lingenyuswanga kabahambanga kuze kufike usuku lokwenyuswa kwalo.
Koma ngati mtambo sunachoke, iwo sankasamukanso mpaka tsiku limene udzachoke.
38 Ngoba iyezi leNkosi laliphezu kwethabhanekele emini, lomlilo wawuphezu kwalo ebusuku, phambi kwamehlo endlu yonke yakoIsrayeli, enhambeni zabo zonke.
Kotero mtambo wa Yehova unkakhala pamwamba pa chihema usana, ndi mtambo wamoto umakhala usiku, pamaso pa nyumba yonse ya Israeli pa masiku onse aulendo wawo.