< U-Eksodusi 4 >
1 UMozisi wasephendula wathi: Kodwa khangela, kabayikungikholwa, kabayikulilalela ilizwi lami; ngoba bazakuthi: INkosi kayibonakalanga kuwe.
Mose anayankha, “Aisraeliwo sakandikhulupirira ndipo sakandimvera. Iwowo adzati, ‘Yehova sanakuonekere iwe.’”
2 INkosi yasisithi kuye: Kuyini lokho okusesandleni sakho? Wasesithi: Yintonga.
Ndipo Yehova anamufunsa nati, “Nʼchiyani chili mʼdzanja lakolo?” Mose anayankha kuti, “Ndodo.”
3 Yasisithi: Iphosele emhlabathini. Waseyiphosela emhlabathini, yasisiba yinyoka. UMozisi waseyibalekela.
Yehova anati, “Tayiponya pansi.” Mose anayiponya pansi ndipo inasanduka njoka ndipo anayithawa.
4 INkosi yasisithi kuMozisi: Yelula isandla sakho, uyibambe ngomsila. Waselula isandla sakhe, wayithi xhaka; yasisiba yintonga esandleni sakhe,
Kenaka Yehova anati kwa iye, “Igwire mtchira.” Ndipo Mose anayigwira mchira njokayo ndipo inasandukanso ndodo mʼdzanja lake.
5 ukuze bakholwe ukuthi ibonakele kuwe iNkosi, uNkulunkulu waboyise, uNkulunkulu kaAbrahama, uNkulunkulu kaIsaka, loNkulunkulu kaJakobe.
Yehova anati, “Ukachite zimenezi ndipo akakukhulupirira kuti Yehova, Mulungu wa makolo awo, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo, wakuonekera iwe.”
6 INkosi yasisithi njalo kuye: Ake ufake isandla sakho esifubeni sakho. Wasesifaka isandla sakhe esifubeni sakhe; esesikhuphile, khangela-ke, isandla sakhe sasesilobulephero njengeliqhwa elikhithikileyo.
Yehova anatinso, “Pisa dzanja lako mʼmalaya akowo.” Choncho Mose anapisa dzanja lake mʼmalaya ake ndipo pamene analitulutsa, linali la khate kuchita kuti mbuu ngati ufa.
7 Yasisithi: Buyisela isandla sakho esifubeni sakho. Wasesibuyisela isandla sakhe esifubeni sakhe; esesikhuphile esifubeni sakhe, khangela-ke, sasesiphenduke saba njengenyama yakhe.
Yehova anati, “Tsopano pisanso dzanja lako mʼmalaya.” Mose anapisanso dzanja lakelo mʼmalaya ake ndipo atalitulutsa, linali labwinobwino, ngati thupi lake lonse.
8 Njalo kuzakuthi uba bengakukholwa, bengalaleli ilizwi lesibonakaliso sokuqala, bazakholwa ilizwi lesibonakaliso sokucina.
Tsono Yehova anati “Akakapanda kukukhulupirira, osalabadira chozizwitsa choyambacho, akakhulupirira ndithu chifukwa cha chozizwitsa chachiwiricho.
9 Kuzakuthi-ke, uba bengakholwa lalezizibonakaliso ezimbili, bengalaleli ilizwi lakho, uzakukha okwamanzi omfula, uwathele emhlabathini owomileyo; njalo kuzakuthi amanzi ozawakha emfuleni azakuba ligazi emhlabathini owomileyo.
Koma ngati sakakhulupirira zizindikiro ziwiri izi kapena kukumvera, ukatunge madzi a mu mtsinje wa Nailo ndi kuwathira pa mtunda powuma ndipo madziwo adzasanduka magazi.”
10 UMozisi wasesithi eNkosini: Uxolo, Nkosi yami, kangisiso sikhulumi, ngitsho kusukela endulo, ngitsho kusukela usukhulume lenceku yakho; ngoba kunzima emlonyeni wami njalo kunzima olimini.
Mose anati kwa Yehova, “Chonde Ambuye, chikhalire ine ndakhala munthu wosatha kuyankhula bwino. Ngakhale tsopano pamene mukundiyankhula, lilime langa ndi lolemera. Ndine wachibwibwi.”
11 INkosi yasisithi kuye: Ngubani owenzela umuntu umlomo? Kumbe ngubani owenza isimungulu, kumbe isacuthe, kumbe obonayo, kumbe isiphofu? Kakusimi yini iNkosi?
Yehova anati kwa iye, “Kodi anapatsa munthu pakamwa ndani? Ndani amasandutsa munthu kuti akhale wosayankhula kapena wosamva? Ndani amapanga munthu kukhala wopenya kapena wosaona? Kodi si Ine Yehova?
12 Khathesi-ke hamba, njalo mina ngizakuba lomlomo wakho, ngikufundise lokho ozakukhuluma.
Tsopano pita, Ine ndidzakuthandiza kuyankhula ndipo ndidzakulangiza zoti ukanene.”
13 Kodwa wathi: Uxolo, Nkosi yami, akuthume ngesandla salowo ozamthuma.
Koma Mose anati, “Chonde Ambuye, pepani, tumani wina kuti akachite zimenezi.”
14 Lwaseluvutha ulaka lweNkosi kuMozisi, yasisithi: Angithi uAroni umLevi ngumnewenu? Ngiyazi ukuthi angakhuluma kuhle. Njalo khangela-ke, uzaphuma ukukuhlangabeza; nxa ekubona, uzathaba enhliziyweni yakhe.
Kenaka Yehova anamupsera mtima Mose ndipo anati, “Kodi suli ndi mʼbale wako Aaroni wa fuko la Levi? Ine ndikudziwa kuti iye amayankhula bwino. Iye wanyamuka kale kudzakumana nawe ndipo adzasangalala akadzakuona.
15 Njalo uzakhuluma kuye, ufake amazwi emlonyeni wakhe; mina-ke ngizakuba lomlomo wakho lomlomo wakhe, ngizalifundisa lokho elizakwenza.
Iwe udzayankhula naye ndi kumuwuza mawu oti akanene. Ine ndidzakuthandizani kuyankhula nonse awirinu ndi kukulangizani zoti mukachite.
16 Yena-ke uzakhuluma esizweni esikhundleni sakho, kuzakuthi abe ngumlomo kuwe, wena ube njengoNkulunkulu kuye.
Iye akayankhula kwa anthu mʼmalo mwako. Iye adzakhala wokuyankhulira ndipo iweyo udzakhala ngati Mulungu kwa iye.
17 Njalo uzathatha lintonga esandleni sakho, ozakwenza izibonakaliso ngayo.
Koma utenge ndodo imene ili mʼdzanja lakoyo kuti ukachite nayo zizindikiro zozizwitsa.”
18 UMozisi wasehamba wabuyela kuJetro uyisezala, wathi kuye: Ake ungiyekele ngihambe, ngibuyele kubafowethu abaseGibhithe, ngibone ukuthi basaphila yini. UJetro wasesithi kuMozisi: Hamba ngokuthula.
Tsono Mose anabwerera kwa Yetero, mpongozi wake ndipo anati kwa Iye, “Chonde ndiloleni kuti ndibwerere ku Igupto kwa anthu anga kuti ndikaone ngati ali moyo.” Yeteri anati, “Pitani mu mtendere.”
19 INkosi yasisithi kuMozisi eMidiyani: Hamba, ubuyele eGibhithe; ngoba wonke amadoda asafa, ayedinga umphefumulo wakho.
Nthawiyi Yehova anali atamuwuza kale Mose ku Midiyani kuti, “Bwerera ku Igupto, pakuti anthu onse amene amafuna kukupha aja anamwalira.”
20 UMozisi wasethatha umkakhe lamadodana akhe, wabakhwelisa phezu kukababhemi, wabuyela elizweni leGibhithe. UMozisi wasethatha intonga kaNkulunkulu esandleni sakhe.
Kotero Mose anatenga mkazi wake ndi ana ake aamuna, ndipo anawakweza pa bulu nayamba ulendo wobwerera ku Igupto. Ndipo anatenga ndodo ya Mulungu ija mʼdzanja lake.
21 INkosi yasisithi kuMozisi: Ekuhambeni kwakho ubuyela eGibhithe, bona ukuthi, zonke izimangaliso engizibeke esandleni sakho, uzenze phambi kukaFaro. Kodwa ngizakwenza inhliziyo yakhe ibe lukhuni ukuze angasiyekeli isizwe sihambe.
Yehova anati kwa Mose, “Ukaonetsetse kuti wachita pamaso pa Farao zodabwitsa zonse zimene ndayika mphamvu mwa iwe kuti ukachite. Koma Ine ndidzawumitsa mtima wake kotero kuti sadzalola anthuwo kuti apite.
22 Njalo uzakuthi kuFaro: Itsho njalo iNkosi: Indodana yami, izibulo lami, nguIsrayeli;
Ndipo iwe ukati kwa Farao, ‘Yehova akuti, Israeli ali ngati mwana wanga wachisamba.’
23 njalo sengithe kuwe: Yekela indodana yami ihambe ukuthi ingikhonze; kodwa walile ukuyiyekela ihambe, khangela, ngizabulala indodana yakho, izibulo lakho.
Choncho ndikuti, ‘Mulole mwana wanga apite kuti akandipembedze. Koma ngati ukana, Ine ndidzapha mwana wako wachisamba.’”
24 Kwasekusithi esendleleni, endlini yezihambi, iNkosi yahlangana laye, yadinga ukumbulala.
Pambuyo pake Mose ali mʼnjira, pamalo wogona, Yehova anakumana naye, ndipo anafuna kumupha.
25 UZipora wasethatha insengetshe, waquma ijwabu laphambili lendodana yakhe, walithintisa inyawo zakhe wathi: Isibili ungumyeni wegazi kimi.
Koma Zipora anatenga mwala wakuthwa nachita mdulidwe mwana wake ndipo khungulo analikhudzitsa pa mapazi a Mose. Iye anati “Zoonadi, kwa ine ndiwe mkwati wamagazi.”
26 Yasimyekela. Ngalesosikhathi wathi: Umyeni wegazi, ngenxa yokusoka.
Choncho Yehova anamuleka Mose wosamupha. Pa nthawiyo, Zipora anati, “Mkwati wa magazi,” ponena za mdulidwe.
27 INkosi yasisithi kuAroni: Hamba, uyehlangabeza uMozisi enkangala. Wahamba-ke, wahlangana laye entabeni kaNkulunkulu, wamanga.
Yehova anati kwa Aaroni, “Pita ku chipululu ukakumane ndi Mose.” Iye anapitadi nakakumana ndi Mose pa phiri la Mulungu namupsompsona.
28 UMozisi wasemtshela uAroni wonke amazwi eNkosi eyayimthumile, lazo zonke izibonakaliso eyayimlaye zona.
Kenaka Mose anamufotokozera Aaroni chilichonse chimene Yehova anamutuma kuti akanene. Anamufotokozera za zizindikiro zozizwitsa zimene anamulamulira kuti akazichite.
29 OMozisi loAroni basebehamba, babuthanisa bonke abadala babantwana bakoIsrayeli.
Mose ndi Aaroni anapita kukasonkhanitsa pamodzi akuluakulu onse a Aisraeli.
30 UAroni wasekhuluma amazwi wonke iNkosi eyayiwakhulume kuMozisi, wenza izibonakaliso phambi kwamehlo abantu.
Ndipo Aaroni anawafotokozera zonse zimene Yehova ananena kwa Mose. Anachita zizindikirozo pamaso pa anthu onse,
31 Abantu basebekholwa; bezwa ukuthi iNkosi ihambele abantwana bakoIsrayeli, lokuthi ibonile inhlupheko yabo, bakhothama, bakhonza.
ndipo anakhulupirira. Iwo atamva kuti Yehova anadzawayendera ndi kuti waona mmene akuzunzikira, anaweramitsa mitu pansi napembedza.