< U-Eksodusi 35 >

1 UMozisi wasebuthanisa inhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli, wathi kubo: La ngamazwi iNkosi ewalayileyo ukuthi liwenze.
Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
2 Insuku eziyisithupha kuzakwenziwa umsebenzi, kodwa ngosuku lwesikhombisa kuzakuba yibungcwele kini, isabatha lokuphumula eNkosini; loba ngubani owenza umsebenzi ngalo uzabulawa.
Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3 Lingabasi umlilo ngosuku lwesabatha kuyo yonke imizi yenu.
Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
4 UMozisi wasekhuluma kunhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli esithi: Yile into iNkosi eyilayileyo isithi:
Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
5 Thathani phakathi kwenu umnikelo ube ngoweNkosi; loba ngubani olenhliziyo evumayo kawulethe, umnikelo weNkosi, igolide lesiliva lethusi,
Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
6 lokuluhlaza okwesibhakabhaka lokuyibubende lokubomvu, lelembu elicolekileyo kakhulu, loboya bembuzi,
nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
7 lezikhumba eziphendulwe zababomvu zezinqama, lezikhumba zikamantswane, lezihlahla zesinga,
zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
8 lamafutha ezibane, lamakha amafutha okugcoba lempepha elephunga elimnandi,
mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
9 lamatshe ama-onikse, lamatshe okubekwa awe-efodi lawesembatho sesifuba.
miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
10 Labo bonke abalenhliziyo ehlakaniphileyo phakathi kwenu kabeze benze konke iNkosi ekulayileyo;
“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
11 ithabhanekele, ithente lalo, lesifulelo salo, ingwegwe zalo, lamapulanka alo, imithando yalo, insika zalo, lezisekelo zalo;
Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
12 umtshokotsho, lemijabo yawo, isihlalo somusa, leveyili lesembeso;
Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
13 itafula, lemijabo yalo, lezitsha zalo zonke, lezinkwa zokubukiswa;
tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
14 loluthi lwesibane sesikhanyiso, lezitsha zalo, lezibane zalo, lamafutha esikhanyiso;
choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
15 lelathi lempepha, lemijabo yalo, lamafutha okugcoba, lempepha elephunga elimnandi, lesilenge somnyango emnyango wethabhanekele;
guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
16 ilathi lomnikelo wokutshiswa, lesihlengo sethusi elilaso, imijabo yalo, lazo zonke izitsha zalo, inditshi yokugezela lonyawo lwayo;
guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
17 amakhetheni eguma, insika zalo, lezisekelo zazo, lesilenge sesango leguma;
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
18 izikhonkwane zethabhanekele, lezikhonkwane zeguma, lentambo zazo;
zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
19 izembatho ezifekethisiweyo zokukhonza endaweni engcwele, izembatho ezingcwele zikaAroni umpristi, lezembatho zamadodana akhe, ukusebenza njengabapristi.
zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
20 Lenhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli yaphuma phambi kukaMozisi.
Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
21 Beza-ke, wonke onhliziyo yakhe eyamvusayo, laye wonke omoya wakhe owamenza wavuma, baletha umnikelo eNkosini emsebenzini wethente lenhlangano lowenkonzo yonke yalo lowezembatho ezingcwele.
ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
22 Beza-ke abesilisa kanye labesifazana, bonke abavumayo ngenhliziyo, baletha iziceco lamacici lendandatho lamasongo, zonke izinto zegolide; laye wonke owazunguza umnikelo wokuzunguzwa wegolide eNkosini.
Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
23 Laye wonke okwatholakala kuye okuluhlaza okwesibhakabhaka lokuyibubende lokubomvu lelembu elicolekileyo kakhulu loboya bembuzi lezikhumba eziphendulwe zababomvu zenqama lezikhumba zikamantswane bakuletha.
Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
24 Wonke owanikela umnikelo wokuzunguzwa wesiliva lowethusi bakuletha kungumnikelo wokuzunguzwa weNkosi; laye wonke okwatholakala kuye izihlahla zesinga ezawo wonke umsebenzi wenkonzo baziletha.
Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
25 Labo bonke abesifazana ababehlakaniphile ngenhliziyo baphotha ngezandla zabo, baletha okuphothiweyo, okuluhlaza okwesibhakabhaka, lokuyibubende, okubomvu, lelembu elicolekileyo kakhulu.
Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
26 Labo bonke abesifazana abanhliziyo zabo zabavusa enhlakanipheni baphotha uboya bembuzi.
Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
27 Lezinduna zaletha amatshe ama-onikse lamatshe okubekwa, awe-efodi lawesembatho sesifuba,
Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
28 lamakha lamafutha awesibane, lawamafutha okugcoba, lawempepha elephunga elimnandi.
Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
29 Abantwana bakoIsrayeli bawuletha umnikelo wesihle eNkosini. Bonke abesilisa labesifazana abanhliziyo zabo zabenza bavuma ukulethela wonke umsebenzi iNkosi eyayiwulayile ukuthi wenziwe ngesandla sikaMozisi.
Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
30 UMozisi wasesithi ebantwaneni bakoIsrayeli: Bonani, iNkosi imbizile ngebizo uBhezaleli indodana kaUri, indodana kaHuri owesizwe sakoJuda;
Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
31 imgcwalisile ngoMoya kaNkulunkulu enhlakanipheni, ekuqedisiseni, lelwazini, lemisebenzini yobungcitshi yonke,
ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
32 lokuthi acebe ubungcitshi ukusebenza ngegolide langesiliva langethusi,
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
33 lekubazeni amatshe okufakwa, lekubazeni izigodo, ukusebenza emisebenzini yonke yeminwe ngobungcitshi.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
34 Ifakile laye enhliziyweni yakhe ukufundisa, yena loOholiyaba indodana kaAhisamaki owesizwe sakoDani.
Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
35 Ibagcwalisile ngokuhlakanipha kwenhliziyo, ukwenza wonke umsebenzi wombazi, lowengcitshi, lowomfekethisi ngenalithi, ngokuluhlaza okwesibhakabhaka langokuyibubende, ngokubomvu langelembu elicolekileyo kakhulu, lowomeluki; besenza wonke umsebenzi beceba ubungcitshi.
Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.

< U-Eksodusi 35 >